< Provérbios 19 >

1 Melhor é o pobre que caminha em sua integridade do que aquele que é perverso em seus lábios e é um tolo.
Ndi wabwino munthu wosauka amene amayenda mu ungwiro, aposa munthu wopusa woyankhula zokhota.
2 Não é bom ter zelo sem conhecimento, nem ser apressado com os pés e perder o caminho.
Si bwino kuti munthu akhale wopanda nzeru; ndipo munthu woyenda mofulumira amaphonya njira.
3 A insensatez do homem subverte seu caminho; seu coração se enfurece contra Yahweh.
Uchitsiru wa munthu umamubweretsera zovuta, mtima wake umakwiyira Yehova.
4 Wealth adiciona muitos amigos, mas os pobres estão separados de seu amigo.
Chuma chimachulukitsa abwenzi; koma munthu wosauka bwenzi lake limamuthawa.
5 Uma falsa testemunha não ficará impune. Aquele que derrama mentiras não deve sair livre.
Mboni yonama sidzalephera kulangidwa; ndipo iye amene amanena mabodza sadzapulumuka.
6 Muitos suplicarão o favor de um governante, e todos são amigos de um homem que dá presentes.
Anthu ambiri amafuna munthu wopatsa kuti awakomere mtima, ndipo munthu amene amapereka mphatso ndi bwenzi la munthu aliyense.
7 Todos os parentes dos pobres o evitam; quanto mais seus amigos o evitam! Ele os persegue com prazer, mas eles se foram.
Ngati munthu wosauka abale ake omwe amadana naye, nanji abwenzi ake tsono! Iwo adzamuthawa kupita kutali. Amayesa kuwatsatira mowapembedza koma iwo samapezeka konse.
8 Aquele que adquire sabedoria ama sua própria alma. Aquele que mantém a compreensão deve encontrar o bem.
Iye amene amapeza nzeru ndiye kuti amakonda moyo wake. Wosamalitsa kukhala wanzeru, zinthu zimamuyendera bwino.
9 Uma falsa testemunha não ficará impune. Aquele que profere mentiras perecerá.
Mboni yonama sidzalephera kulangidwa, ndipo iye amene amanena mabodza adzawonongeka.
10 Delicate viver não é apropriado para um tolo, muito menos para que um servo tenha domínio sobre príncipes.
Nʼkosayenera kuti chitsiru chizikhala ndi moyo wamanyado, nanjinso kuti kapolo azilamulira akalonga!
11 A discrição de um homem o torna lento para a raiva. É sua glória ignorar uma ofensa.
Nzeru zimapangitsa munthu kukhala wosakwiya msanga; ulemerero wake uli posalabadira kuchitiridwa zoyipa.
12 A ira do rei é como o rugido de um leão, mas seu favor é como o orvalho na grama.
Mkwiyo wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango, koma kukoma mtima kwake kuli ngati mame pa udzu.
13 Um filho insensato é a calamidade de seu pai. As brigas de uma esposa são um gotejamento contínuo.
Mwana wopusa ndiye tsoka la abambo ake ndipo mkazi wolongolola ndi wotopetsa ngati mvula yamvumbi.
14 Casa e riquezas são uma herança dos pais, mas uma esposa prudente é de Yahweh.
Nyumba ndi chuma ndiye cholowa chochokera kwa makolo; koma mkazi wanzeru ndi wochokera kwa Yehova.
15 Slothfulness entra em um sono profundo. A alma ociosa deve passar fome.
Ulesi umagonetsa tulo tofa nato ndipo munthu wosatakataka amakhala ndi njala.
16 He que mantém o mandamento mantém sua alma, mas aquele que for desdenhoso em seus caminhos morrerá.
Amene amamvera malangizo amasunga moyo wake, koma amene sasamala malamulo a Yehova adzafa.
17 Aquele que tem piedade dos pobres empresta a Javé; ele irá recompensá-lo.
Amene amakomera mtima osauka amachita ngati wakongoletsa Yehova, ndipo Yehovayo ndiye adzamubwezere.
18 Discipline seu filho, pois há esperança; não seja uma parte disposta à sua morte.
Langa mwana wako, chiyembekezo chikanalipo; ngati sutero udzawononga moyo wake.
19 Um homem de temperamento quente deve pagar a penalidade, pois, se você o resgatar, deverá fazê-lo novamente.
Munthu waukali woopsa ayenera kulandira chilango; pakuti akamulekelera ndiye zidzayipa kuposa kale.
20 Ouça o conselho e receba instruções, que você possa ser sábio em seu último fim.
Mvera uphungu ndipo landira malangizo; pa mapeto pake udzakhala wanzeru.
21 Há muitos planos no coração de um homem, mas o conselho de Yahweh prevalecerá.
Munthu amakonzekera zambiri mu mtima mwake, koma cholinga cha Yehova ndiye chidzachitike.
22 O que faz com que um homem seja desejado é sua bondade. Um homem pobre é melhor que um mentiroso.
Chimene munthu amafuna ndi chikondi chosatha; nʼkwabwino kukhala wosauka kusiyana ndi kukhala wabodza.
23 O medo de Yahweh leva à vida, depois ao contentamento; ele descansa e não será tocado por problemas.
Kuopa Yehova kumabweretsa moyo; wotereyo amakhala mu mtendere; ndiye kuti choyipa sichidzamugwera.
24 O preguiçoso enterra sua mão no prato; ele não o levará nem mesmo à boca novamente.
Munthu waulesi amapisa dzanja lake mʼmbale; koma sangathe kufikitsa dzanja lakelo pakamwa pake.
25 Flog a scoffer, e o simples aprenderá a prudência; repreenda aquele que tem entendimento, e ele ganhará conhecimento.
Menya munthu wonyoza, ndipo anthu opanda nzeru adzachenjererapo; dzudzula munthu wozindikira zinthu, ndipo iye adzapezapo chidziwitso.
26 Aquele que rouba seu pai e expulsa sua mãe é um filho que causa vergonha e traz censuras.
Mwana wochita ndewu ndi abambo ake ndi kuthamangitsa amayi ake, ndi mwana wochititsa manyazi ndi wonyozetsa.
27 Se você parar de ouvir as instruções, meu filho, você se desviará das palavras do conhecimento.
Mwana wanga, ukaleka kumvera malangizo, udzapatukana ndi mawu opatsa nzeru.
28 Uma testemunha corrupta escarnece da justiça, e a boca do malvado engula a iniqüidade.
Mboni yopanda pake imanyoza cholungama, ndipo pakamwa pa anthu oyipa pamameza zoyipa.
29 Penalties estão preparados para os zombadores, e espancamentos para as costas dos tolos.
Chilango chakonzedwa kale kuti chigwere anthu oyipa, ndipo mkwapulo wakonzedwa kale kuti ukwapule misana ya anthu opusa.

< Provérbios 19 >