< Jeremias 48 >

1 De Moab. Yahweh dos exércitos, o Deus de Israel, diz: “Ai do Nebo! Pois é um desperdício colocado. O Kiriathaim está desapontado. É tomada. Misgab é envergonhado e decomposto.
Ponena za Mowabu: Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Tsoka kwa mzinda wa Nebo, chifukwa wawonongedwa. Mzinda wa Kiriyataimu wachititsidwa manyazi ndipo wagonjetsedwa; linga lichititsidwa manyazi ndipo lagumulidwa.
2 Os elogios de Moab já não são mais. Em Heshbon, eles inventaram o mal contra ela: Venha! Vamos impedi-la de ser uma nação”. Você também, Madmen, será levado ao silêncio. A espada o perseguirá.
Palibenso amene akutamanda Mowabu; ku Hesiboni anthu anamupanganira zoyipa: ‘Bwerani, tiyeni timuwonongeretu kuti asakhalenso mtundu wa anthu.’ Inunso anthu a ku Madimena, adzakukhalitsani chete; ankhondo adzakupirikitsani.
3 O som de um grito de Horonaim, desolação e grande destruição!
Tamvani mfuwu wa anthu a ku Horonaimu. Iwo akulira kuti, ‘Kusakazika ndi kuwonongeka kwakukulu.’
4 Moab é destruído. Seus pequeninos fizeram com que um grito fosse ouvido.
Mowabu wawonongeka; ana ake angʼonoangʼono akulira kwambiri.
5 Pois eles subirão pela subida de Luhith com lágrimas contínuas. Pois na descida de Horonaim eles ouviram a angústia do grito de destruição.
Anthu akukwera chikweza cha ku Luhiti, akulira kwambiri pamene akupita. Kulira chifukwa cha chiwonongeko kukumveka pa njira yotsikira ku Horonaimu.
6 Fuja! Salvem suas vidas! Ser como o arbusto do zimbro no deserto.
Thawani! Dzipulumutseni; khalani ngati mbidzi ya mʼchipululu.
7 Pois, porque você tem confiado em suas obras e em seus tesouros, você também será levado. Chemosh sairá para o cativeiro, seus padres e seus príncipes juntos.
Popeza inu munkadalira ntchito zanu ndi chuma chanu, nanunso mudzatengedwa ukapolo, ndipo Kemosi adzapita ku ukapolo, pamodzi ndi ansembe ake ndi akuluakulu ake.
8 O contratorpedeiro virá em todas as cidades, e nenhuma cidade escapará; o vale também perecerá, e a planície será destruída, como Yahweh já falou.
Wowononga adzabwera ndi kusakaza mzinda uliwonse, ndipo palibe mzinda umene udzapulumuke. Chigwa chidzasanduka bwinja ndipo malo athyathyathya a pamwamba pa phiri adzawonongedwa monga Yehova wayankhulira.
9 Dê as asas à Moab, que ela possa voar e se afastar: e suas cidades se tornarão uma desolação, sem ninguém para morar neles.
Mtsineni khutu Mowabu chifukwa adzasakazika; mizinda yake idzasanduka mabwinja, wopanda munthu wokhalamo.
10 “Maldito é aquele que faz o trabalho de Javé de forma negligente; e amaldiçoado é aquele que mantém sua espada longe do sangue.
“Wotembereredwa munthu amene amagwira ntchito ya Yehova monyinyirika! Wotembereredwa munthu amene amaletsa lupanga lake kupha anthu!
11 “Moab tem estado à vontade desde sua juventude, e ele se acomodou em suas borras, e não foi esvaziado de navio para navio, nem ele foi para o cativeiro; portanto, seu gosto permanece nele, e seu cheiro não é alterado.
“Mowabu wakhala pa mtendere kuyambira ubwana wake, ngati vinyo wokhazikika pa masese ake, osapungulidwa kuchoka mu mtsuko wina kuthira mu mtsuko wina; iye sanatengedwepo ukapolo. Nʼchifukwa chake kukoma kwake nʼkomwe kuja ndipo fungo lake silinasinthe.
12 Portanto, eis que os dias vêm”, diz Yahweh, “que eu lhe enviarei aqueles que despejarem”, e eles o despejarão; e eles esvaziarão suas embarcações, e quebrar seus recipientes em pedaços.
Nʼchifukwa chake masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzatuma anthu amene amakhuthula vinyo mʼmitsuko ndipo adzamukhutula; adzakhuthula vinyo yense mitsuko yake pambuyo pake nʼkuphwanya mitsukoyo.
13 Moab terá vergonha de Chemosh, como a casa de Israel tinha vergonha de Betel, sua confiança.
Pamenepo Mowabu adzachita manyazi ndi Kemosi, monga momwe Aisraeli anachitira manyazi ndi Beteli amene ankamukhutulira.
14 “Como se diz: “Somos homens poderosos”, e homens corajosos para a guerra”?
“Kodi munganene bwanji kuti, ‘Ife ndife asilikali. Ife ndife ngwazi, anthu amphamvu pa nkhondo?’
15 Moab é um resíduo depositado, e eles subiram em suas cidades, e seus jovens escolhidos foram para o abate”. diz o Rei, cujo nome é Yahweh dos Exércitos.
Owononga Mowabu ndi mizinda yake abwera ndipo ankhondo adzalowa mʼmidzi yake; anyamata ake okongola apita kukaphedwa,” ikutero Mfumu, imene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
16 “A calamidade de Moab está próxima de chegar, e sua aflição se apressa rapidamente.
Kugwa kwa Mowabu kuli pafupi; masautso ake akubwera posachedwa.
17 Todos vocês que estão ao seu redor, lamentam-no; e todos vocês que conhecem seu nome, dizem, “Como o pessoal forte está quebrado”, a bela vara”!
Mulireni kwambiri, inu nonse amene mwamuzungulira, inu nonse amene mumadziwa za kutchuka kwake; nenani kuti, “Taonani momwe yathyokera ndodo yamphamvu yaufumu ija, taonani momwe ndodo yaulemu yathyokera!”
18 “Sua filha que mora em Dibon, desça de sua glória, e sentar-se na sede; pois o destruidor de Moab se deparou com você. Ele destruiu seus bastiões.
“Tsikani pa ulemerero wanu ndipo khalani pansi powuma, inu anthu okhala ku Diboni, pakuti wowononga Mowabu wabwera kudzamenyana nanu, wasakaza mizinda yanu yotetezedwa.
19 Habitante de Aroer, fique a caminho e assista. Pergunte a ele quem foge, e a ela quem foge; dizer: “O que foi feito?
Inu amene mumakhala ku Aroeri, imani mʼmbali mwa msewu ndi kumaonerera. Funsani mwamuna amene akuthawa ndiponso mkazi amene wapulumuka, afunseni kuti, ‘Kodi chachitika nʼchiyani?’”
20 Moab está desapontado; pois está quebrado. Lamentai e chorai! Diga pelo Arnon, que o Moab é um resíduo.
Iwo adzayankha kuti, “Mowabu wachititsidwa manyazi, pakuti wasakazika. Lirani mwachisoni ndipo fuwulani! Lengezani ku mtsinje wa Arinoni kuti Mowabu wawonongedwa.
21 O julgamento foi feito no país simples... em Holon, em Jahzah, em Mephaath,
Chiweruzo chabwera ku mizinda ya ku mapiri, ndiyo Holoni, Yaza, Mefaati,
22 em Dibon, em Nebo, em Beth Diblathaim,
Diboni, Nebo, Beti-Dibilataimu,
23 sobre Kiriathaim, sobre Beth Gamul, sobre Beth Meon,
Kiriyataimu, Beti-Gamuli, Beti-Meoni,
24 em Kerioth, em Bozrah, e em todas as cidades da terra de Moab, longe ou perto.
Keriyoti ndi Bozira ndi mizinda yonse ya Mowabu, yakutali ndi yapafupi yomwe.
25 O chifre de Moab está cortado, e seu braço está quebrado”, diz Yahweh.
Mphamvu za Mowabu zawonongeka; mkono wake wathyoka,” akutero Yehova.
26 “Deixe-o bêbado, pois ele se engrandeceu contra Yahweh. Moab vai chafurdar em seu vômito, e ele também estará em zombaria.
“Muledzeretseni Mowabu, chifukwa anadzikuza powukira Yehova. Mulekeni Mowabu avivinizike mʼmasanzi ake; mulekeni akhale chinthu chomachiseka.
27 Pois Israel não foi um escárnio para você? Ele foi encontrado entre ladrões? Por todas as vezes que você fala dele, você abana a cabeça.
Kodi suja Israeli anali kwa iwe ngati chinthu chomachiseka? Kodi Israeli anapezeka pakati pa akuba kuti nthawi zonse poyankhula za iye, iwe uzimupukusira mutu momunyoza?
28 Vocês, habitantes de Moab, deixam as cidades e moram na rocha. Seja como a pomba que faz seu ninho sobre a boca do abismo.
Inu amene mumakhala ku Mowabu, siyani mizinda yanu ndi kukakhala pakati pa matanthwe. Khalani ngati nkhunda imene imamanga chisa chake pa khomo la phanga.
29 “Já ouvimos falar do orgulho de Moab. Ele está muito orgulhoso de sua altura, de seu orgulho, sua arrogância, e a arrogância de seu coração.
“Tamva za kunyada kwa Mowabu, kunyada kwake nʼkwakukulu. Ndi wodzitama, wonyada ndi wodzitukumula. Ali ndi mtima wodzikweza.
30 Eu conheço sua ira”, diz Yahweh, “que não é nada”; suas jactâncias não fizeram nada.
Ine ndikuzidziwa ntchito zake, akutero Yehova. Ntchitozo ndi nʼzosapindulitsa kanthu.
31 Portanto, lamentarei por Moab. Sim, eu clamarei por todos os Moab. Eles farão o luto pelos homens de Kir Heres.
Nʼchifukwa chake ndidzamulira Mowabu, ine ndikulira chifukwa cha anthu onse a ku Mowabu, ndikubuwula chifukwa cha anthu a ku Kiri Heresi.
32 Com mais do que o pranto da Jazer Vou chorar por você, videira de Sibmah. Seus ramos passaram por cima do mar. Eles chegaram até o mar de Jazer. O contratorpedeiro caiu sobre suas frutas de verão e em sua safra.
Ndikukhetsa misozi chifukwa cha inu, kupambana momwe ndinalirira Yazeri. Inu anthu a ku Sibina muli ngati mipesa imene nthambi zake zatambalala mpaka ku Nyanja; zafika mpaka ku nyanja ya Yazeri. Wowononga wasakaza zipatso zake zachilimwe ndi mpesa.
33 A alegria e a alegria são tiradas do campo fértil e da terra de Moab. Fiz com que o vinho parasse das prensas de vinho. Ninguém vai pisar com gritos. A gritaria não será gritada.
Chimwemwe ndi chisangalalo zatha ku minda ya zipatso ya ku Mowabu. Ndaletsa kuchucha kwa vinyo mopsinyira mphesa; palibe amene akufuwula mokondwa akamapsinya mphesa. Ngakhale kufuwula kulipo, koma sikufuwula kwa chimwemwe.
34 Desde o grito de Heshbon até a Elealeh, mesmo para Jahaz, eles pronunciaram sua voz, desde Zoar até Horonaim, passando por Eglath Shelishiyah; pois as águas de Nimrim também se tornarão desoladas.
“A ku Hesiboni ndi Eleali akulira ndipo mfuwu wawo ukumveka mpaka ku Yahazi, kuchokera ku Zowari mpaka ku Horonaimu ndi ku Egilati Selisiya. Ngakhale madzi a ku Nimurimu aphwa.
35 Moreover Vou fazer cessar em Moab”, diz Yahweh, “aquele que oferece no lugar alto, e aquele que queima incenso para seus deuses.
Ndidzawaletsa anthu a ku Mowabu kupereka nsembe mʼmalo awo opembedzera ndi kufukiza lubani kwa milungu yawo,” akutero Yehova.
36 Portanto, meu coração soa para Moab como flautas, e meu coração soa como flautas para os homens de Kir Heres. Portanto, a abundância que ele obteve pereceu.
“Nʼchifukwa chake mtima wanga ukulirira Mowabu ngati chitoliro. Mtima wanga ukulirira anthu a ku Kiri Heresi ngati chitoliro chifukwa chuma chimene anachipata chatha.
37 Para cada cabeça é careca, e cada barba cortada. Há recortes em todas as mãos, e pano de saco na cintura.
Aliyense wameta mutu wake ndi ndevu zake; manja a munthu aliyense ndi ochekacheka, ndipo munthu aliyense wavala chiguduli mʼchiwuno mwake.
38 Em todos os telhados da casa de Moab, e, em suas ruas, há lamentações por toda parte; pois quebrei o Moab como um navio no qual ninguém se deleita”, diz Yahweh.
Pa madenga onse a ku Mowabu ndiponso mʼmisewu yake anthu akungolira, pakuti ndaphwanya Mowabu ngati mtsuko wopanda ntchito,” akutero Yehova.
39 “Como está quebrado! Como eles lamentam! Como Moab virou as costas com vergonha! Assim Moab se tornará um escárnio e um terror para todos os que estão ao seu redor”.
“Taonani mmene waphwanyikira! Tamvani momwe akulirira! Taonani momwe Mowabu wachititsidwira manyazi. Mowabu wasanduka chinthu chonyozeka, chinthu chochititsa mantha kwa onse amene amuzungulira.”
40 Para Iavé diz: “Eis que ele voará como uma águia”, e estenderá suas asas contra Moab.
Yehova akuti, “Mtundu wina udzachita kuwuluka nʼkugwera pa Mowabu ngati chiwombankhanga chimene chatambalitsa mapiko ake.
41 Kerioth é tomado, e as fortalezas são apreendidas. O coração dos homens poderosos de Moab naquele dia será como o coração de uma mulher em suas dores.
Mizinda idzagwidwa ndipo malinga adzalandidwa. Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Mowabu idzakhala ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.
42 Moab será destruído por ser um povo, porque ele se engrandeceu contra Yahweh.
Mowabu sudzakhala mtundu wa anthu chifukwa unadzikuza powukira Yehova.
43 Terror, o poço e a armadilha estão sobre você, habitante de Moab”, diz Yahweh.
Zoopsa, dzenje ndi msampha zikudikira inu anthu a ku Mowabu,” akutero Yehova.
44 “Aquele que foge do terror cairá no poço; e aquele que se levantar do poço será levado na armadilha, pois eu o trarei, mesmo em Moab, o ano de sua visitação”, diz Yahweh.
“Aliyense wothawa zoopsa adzagwera mʼdzenje, aliyense wotuluka mʼdzenje adzakodwa mu msampha. Ndigwetsa zimenezi pa Mowabu pa nthawi ya chilango chake,” akutero Yehova.
45 “Aqueles que fugiram ficam de pé sem forças sob a sombra de Heshbon; por um incêndio que saiu de Heshbon, e uma chama do meio de Sihon, e devorou a esquina da Moab, e a coroa da cabeça dos tumultuados.
“Anthu othawa nkhondo ayima pa mthunzi wa Hesiboni chifukwa chotopa. Koma moto wayaka kuchokera ku Hesiboni, malawi a moto abuka kuchokera ku nyumba ya mfumu Sihoni. Motowo ukuwononga mapiri a ku Mowabu, dziko la anthu onyada.
46 Ai de você, ó Moab! As pessoas de Chemosh estão desfeitas; para seus filhos são levados em cativeiro, e suas filhas em cativeiro.
Tsoka kwa iwe Mowabu! Anthu opembedza Kemosi awonongeka. Ana ako aamuna ndi aakazi atengedwa ukapolo.
47 “No entanto, nos últimos dias, vou reverter o cativeiro de Moab”. diz Yahweh. Até agora é o julgamento de Moab.
“Komabe masiku akutsogolo ndidzabwezeranso Mowabu chuma chake,” akutero Yehova. Chiweruzo cha Mowabu chathera pamenepa.

< Jeremias 48 >