< Isaías 45 >

1 Yahweh diz a seu ungido, a Cyrus, cuja mão direita segurei para subjugar nações diante dele e despojar reis de suas armaduras, para abrir as portas diante dele, e os portões não devem ser fechados:
Yehova akuyankhula ndi wodzozedwa wake Koresi amene anamugwira dzanja lamanja kuti agonjetse mitundu ya anthu ndi kuwalanda mafumu zida zawo zankhondo, ndi kutsekula zitseko kuti zipatazo zisadzatsekedwenso ndi ichi:
2 “Eu irei antes de você e tornar os lugares ásperos mais suaves. Quebrarei as portas de bronze em pedaços e cortar as barras de ferro.
Ine ndidzayenda patsogolo pako, ndi kusalaza mapiri; ndidzaphwanya zitseko za mkuwa ndi kuthyola mipiringidzo ya chitsulo.
3 Eu lhe darei os tesouros das trevas e riquezas escondidas de lugares secretos, que você pode saber que sou eu, Yahweh, que o chamo pelo seu nome, até mesmo o Deus de Israel.
Ndidzakupatsa chuma chobisika mu mdima, katundu wa pamalo obisika, kotero kuti udziwe kuti Ine ndine Yehova Mulungu wa Israeli, amene ndakuyitana pokutchula dzina.
4 Para o bem de Jacob meu servo, e Israel, meu escolhido, Eu o chamei pelo seu nome. Eu lhe dei um título, embora você não me conheça.
Chifukwa cha mtumiki wanga Yakobo, chifukwa cha wosankhidwa wanga Israeli, Ine ndakuyitana pokutchula dzina ndipo ndakupatsa dzina laulemu ngakhale iwe sukundidziwa Ine.
5 Eu sou Yahweh, e não há mais ninguém. Além de mim, não há Deus. Eu os fortalecerei, embora você não me conheça,
Ine ndine Yehova ndipo palibenso wina; kupatula Ine palibenso Mulungu wina. Ndidzakupatsa mphamvu, ngakhale sukundidziwa Ine,
6 que eles podem saber do nascer do sol, e do oeste, que não há ninguém além de mim. Eu sou Yahweh, e não há mais ninguém.
kotero kuti kuchokera kummawa mpaka kumadzulo anthu adzadziwa kuti palibe wina koma Ine ndekha. Ine ndine Yehova, ndipo palibenso wina.
7 Eu formo a luz e criar escuridão. Eu faço a paz e criar uma calamidade. Eu sou Yahweh, que faz todas essas coisas.
Ndimalenga kuwala ndi mdima, ndimabweretsa madalitso ndi tsoka; ndine Yehova, amene ndimachita zonsezi.
8 Chuva, céus, vinda de cima, e deixar os céus derramar a justiça. Deixe a terra se abrir, para que ela possa produzir salvação, e deixar que ela faça surgir a retidão com ela. Eu, Yahweh, o criei.
“Iwe thambo gwetsa mvula kuchokera kumwamba; mitambo ivumbwe mivumbi ya chilungamo. Dziko lapansi litsekuke, ndipo chipulumutso chiphuke kuti chilungamo chimereponso; Ine Yehova, ndine ndalenga zimenezi.
9 Ai daquele que se esforça com seu Criador... um pote de barro entre os potes de barro da terra! O barro deve perguntar a ele quem o modela: “O que você está fazendo? ou seu trabalho, “Ele não tem mãos...
“Tsoka kwa wokangana ndi mlengi wake, ngakhale kuti ali ngati phale chabe pakati pa mapale anzake. Kodi dongo lingafunse munthu wowumba kuti, ‘Kodi ukuwumba chiyani?’ Kodi ntchito yako inganene kuti, ‘Ulibe luso?’
10 Ai daquele que diz a um pai: “De que você se tornou o pai de? ou a uma mãe, “O que você deu à luz?””
Tsoka kwa wofunsa abambo ake kuti, ‘Kodi munabereka chiyani?’ Kapena amayi ake kuti, ‘Kodi mufuna kubereka chiyani?’
11 Yahweh, o Santo de Israel e seu Criador diz: “Você me pergunta sobre as coisas que estão por vir, a respeito de meus filhos”, e vocês me comandam a respeito do trabalho de minhas mãos!
“Yehova Woyerayo wa Israeli, ndiponso Mlengi wake akunena, zokhudza zinthu zimene zikubwera ndi izi: Kodi iwe ukundifunsa za ana anga, kapena kundilamula pa zokhudza ntchito zanga?
12 Eu fiz a terra, e criei o homem sobre ela. Eu, até mesmo minhas mãos, estendi os céus. Eu comandei todo o exército deles.
Ndine amene ndinapanga dziko lapansi ndikulenga munthu kuti akhalemo. Ine ndi manja anga ndinayalika thambo; ndimalamulira zolengedwa zonse za mlengalenga.
13 Eu o criei em retidão, e eu vou tornar todos os seus caminhos retos. Ele construirá minha cidade, e deixará meus exilados ir em liberdade, não pelo preço nem pela recompensa”, diz Yahweh dos exércitos.
Ndine amene ndidzawutsa Koresi kuti chilungamo changa chikwaniritsidwe: ndipo ndidzawongolera njira zake zonse. Iye adzamanganso mzinda wanga ndi kumasula anthu anga amene ali mu ukapolo, wopanda kupereka ndalama kapena mphotho, akutero Yehova Wamphamvuzonse.”
14 Yahweh diz: “O trabalho do Egito”, e a mercadoria da Etiópia, e os Sabeanos, homens de estatura, virão até você, e eles serão seus. Eles irão atrás de você. Eles devem vir acorrentados. Eles se curvarão diante de você. Eles farão súplicas a você: “Certamente Deus está em você; e não há mais ninguém”. Não há outro deus.
Yehova akuti, “Chuma cha ku Igupto ndi chuma cha malonda cha Kusi chidzakhala chanu. Anthu amphamvu zawo ndi athanzi a ku Seba adzabwera kwa inu ndipo adzakhala anthu anu; iwo adzidzakutsatani pambuyo panu ali mʼmaunyolo. Adzakugwadirani ndi kukupemphani, ponena kuti, ‘Ndithudi Mulungu ali ndi inu, ndipo palibenso wina; palibenso mulungu wina.’”
15 Most certamente você é um Deus que se escondeu, Deus de Israel, o Salvador”.
Zoonadi inu muli ndi Mulungu wobisika amene ali Mulungu ndi Mpulumutsi wa Israeli.
16 Eles ficarão desapontados, sim, confusos, todos eles. Aqueles que são criadores de ídolos entrarão em confusão juntos.
Onse amene amapanga mafano adzawachititsa manyazi ndi kuwanyozetsa. Adzakhala osokonezeka maganizo.
17 Israel será salvo por Yahweh com uma salvação eterna. Você não ficará desapontado nem confundido com as idades eternas.
Koma Yehova adzapulumutsa Israeli ndi chipulumutso chamuyaya; simudzachitanso manyazi kapena kunyozeka mpaka kalekale.
18 Para Yahweh, que criou os céus, o Deus que formou a terra e a fez, que a estabeleceram e não a criaram um desperdício, que a formou para ser habitada diz: “Eu sou Yahweh. Não há outro.
Yehova analenga zinthu zakumwamba, Iye ndiye Mulungu; amene akulenga dziko lapansi, ndi kulikhazikitsa, sanalipange kuti likhale lopanda kanthu, koma analipanga kuti anthu akhalemo. Iyeyu akunena kuti: Ine ndine Yehova, ndipo palibenso wina.
19 Eu não tenho falado em segredo, em um lugar da terra das trevas. Eu não disse à descendência de Jacob: “Procure-me em vão”. Eu, Yahweh, falo a justiça. Declaro que as coisas estão certas.
Ine sindinayankhule mwachinsinsi, pamalo ena a mdima; Ine sindinaziwuze zidzukulu za Yakobo kuti, “Ndifunefuneni ku malo kopanda kanthu.” Ine Yehova, ndimayankhula zoona; ndikunena zolungama.
20 “Reúnam-se e venham. Aproximem-se juntos, vocês que escaparam das nações. Aqueles que não têm conhecimento de quem carrega a madeira de sua imagem gravada, e rezar a um deus que não pode salvar.
Yehova akuti, “Sonkhanani pamodzi ndipo mubwere; yandikirani, inu amene munapulumuka pothawa nkhondo kwa anthu a mitundu ina. Ndinu opanda nzeru amene mumanyamula mafano a mitengo, amene mumapemphera kwa milungu imene singathe kupulumutsa.
21 Declare e apresente-o. Sim, deixe-os se aconselharem juntos. Quem já mostrou isso desde a antiguidade? Quem o declarou como antigo? Não tenho, Yahweh? Não há outro Deus além de mim, um Deus justo e um Salvador. Não há ninguém além de mim.
Fotokozani mlandu wanu, mupatsane nzeru nonse pamodzi. Kodi ndani ananeneratu zimenezi kalekale? Ndani anazifotokozeratu zimenezi nthawi yamakedzana? Kodi si Ineyo Yehova? Ndipo palibenso Mulungu wina kupatula Ine, Mulungu wolungama ndi Wopulumutsa, palibenso wina kupatula Ine.
22 “Olhe para mim, e seja salvo, todos os confins do mundo; pois eu sou Deus, e não há outro.
“Tembenukirani kwa Ine kuti mupulumuke, inu anthu onse a pa dziko lapansi, pakuti Ine ndine Mulungu ndipo palibenso wina.
23 Jurei por mim mesmo. A palavra saiu de minha boca em retidão e não será revogada, que para mim cada joelho deve se curvar, cada língua fará um juramento.
Ndalumbira ndekha, pakamwa panga patulutsa mawu owona, mawu amene sadzasinthika konse akuti, bondo lililonse lidzagwada pamaso panga; anthu onse adzalumbira potchula dzina langa.
24 Eles dirão de mim, “Só há retidão e força em Yahweh”. Até mesmo a ele virão homens. Todos aqueles que se enfureceram contra ele ficarão decepcionados.
Iwo adzanene kwa Ine kuti, ‘Chilungamo ndi mphamvu zimapezeka mwa Yehova yekha.’” Onse amene anamuwukira Iye adzabwera kwa Iye ndipo adzachita manyazi.
25 Toda a descendência de Israel será justificada em Yahweh, e se regozijarão!
Koma mwa Yehova zidzukulu zonse za Israeli zidzapambana ndi kupeza ulemerero.

< Isaías 45 >