< Isaías 36 >

1 Agora no décimo quarto ano do rei Ezequias, Sennacheribe, rei da Assíria, atacou todas as cidades fortificadas de Judá e as capturou.
Chaka cha khumi ndi chinayi cha ulamuliro wa Mfumu Hezekiya, Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anathira nkhondo mizinda yonse yotetezedwa ya ku Yuda, nayilanda.
2 O rei da Assíria enviou Rabsaqué de Laquis a Jerusalém para o rei Ezequias com um grande exército. Ele ficou ao lado do aqueduto da piscina superior da rodovia de campo mais cheia.
Kenaka mfumu ya ku Asiriya inatuma kazembe wake wankhondo pamodzi ndi gulu lalikulu lankhondo kuchokera ku Lakisi kupita kwa mfumu Hezekiya ku Yerusalemu. Tsono kazembeyo anayima pafupi ndi ngalande yamadzi yochokera ku Dziwe lakumtunda pa msewu wopita ku malo a munda wa mmisiri wochapa zovala.
3 Então Eliakim, o filho de Hilquias, que estava sobre a casa, e Shebna, o escriba, e Joaquim, o filho de Asafe, o gravador, saíram para ele.
Panali anthu atatu. Woyamba anali Eliyakimu mwana wa Hilikiya komanso ndiye woyangʼanira nyumba ya mfumu. Wachiwiri anali Sebina amene anali mlembi wa bwalo; ndipo wachitatu anali Yowa mwana wa Asafu komanso anali wolemba zochitika. Anthu awa anatuluka kukakumana ndi kazembe wa ankhondo uja.
4 Rabshakeh disse-lhes: “Agora digam a Ezequias: 'O grande rei, o rei da Assíria, diz: “Que confiança é essa em que vocês confiam?
Kazembe wa ankhondo anawawuza kuti, “Kamuwuzeni Hezekiya kuti, “Mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya ikunena kuti, Kodi chikukulimbitsa mtima ndi chiyani?
5 Eu digo que seus conselhos e sua força para a guerra são apenas palavras vãs. Em quem você confia, que você se rebelou contra mim?
Iwe ukuti uli ndi luso ndiponso mphamvu pa nkhondo, komatu ukuyankhula mawu opanda pake. Kodi tsono iwe ukudalira yani kuti undiwukire ine?
6 Eis que você confia no bastão desta cana machucada, mesmo no Egito, que se um homem se inclina sobre ela, ela entrará em sua mão e a perfurará. Assim é o faraó rei do Egito para todos os que confiam nele.
Taona tsono, iwe ukudalira Igupto, bango lothyokalo, limene limalasa mʼmanja mwa munthu ngati waliyesa ndodo yoyendera! Umo ndi mmene Farao mfumu ya ku Igupto imachitira aliyense amene akuyidalira.
7 Mas se vocês me disserem: 'Nós confiamos em Javé nosso Deus', não é aquele cujos lugares altos e cujos altares Ezequias tirou, e disse a Judá e a Jerusalém: 'Vocês adorarão diante deste altar...'”.
Ndipo ngati ukunena kwa ine kuti, ‘Ife tikudalira Yehova Mulungu wathu,’ kodi si Mulungu yemweyo amene nyumba zake ndi maguwa ake, Hezekiya anachotsa, nawuza anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu kuti, ‘Muzipembedza pa guwa lansembe ili?’
8 Agora, portanto, por favor, faça um juramento ao meu senhor, o rei da Assíria, e eu lhe darei dois mil cavalos, se você puder de sua parte colocar cavaleiros sobre eles.
“Ndipo tsopano bwera udzakambirane ndi mbuye wanga, mfumu ya ku Asiriya: Ine ndidzakupatsa akavalo 2,000 ngati ungathe kupeza okwerapo!
9 Como, então, você pode afastar o rosto de um capitão do menor dos servos de meu senhor, e depositar sua confiança no Egito para as carruagens e para os cavaleiros?
Iwe ungathe bwanji kugonjetsa ngakhale mmodzi mwa akazembe angʼonoangʼono a mbuye wanga, pamene ukudalira Igupto kuti akupatse magaleta ndi anthu okwera pa akavalo.
10 Será que eu subi agora sem Iavé contra esta terra para destruí-la? Javé me disse: “Suba contra esta terra, e a destrua””.
Kuwonjezera pamenepa, kodi ine ndabwera kudzathira nkhondo ndi kuwononga dziko lino popanda chilolezo cha Yehova? Yehova mwini ndiye anandiwuza kuti ndidzathire nkhondo ndi kuwononga dziko lino.”
11 Então Eliakim, Shebna e Joah disseram a Rabshakeh: “Por favor, fale com seus servos em Aramaico, pois nós entendemos isso. Não nos fale na língua dos judeus na audição das pessoas que estão no muro”.
Pamenepo Eliyakimu, Sebina ndi Yowa anawuza kazembeyo kuti, “Chonde yankhulani kwa atumiki anufe mʼChiaramu, popeza timachimva. Musayankhule nafe mu Chihebri kuopa kuti anthu onse amene ali pa khomapa angamve.”
12 Mas Rabshakeh disse: “Meu mestre me enviou apenas a seu mestre e a você, para dizer estas palavras, e não aos homens que se sentam na parede, que comerão seu próprio esterco e beberão sua própria urina com você”?
Koma kazembeyo anayankha kuti, “Kodi mbuye wanga wandituma kuti ndidzanene zinthu izi kwa mbuye wanu yekha ndi inu nokha basi? Ayi, komanso kwa anthu amene akhala pa khomawa. Iwowa adzadya chimbudzi chawo chomwe ndi kumwa mkodzo wawo womwe monga momwe mudzachitire inuyonso.”
13 Então Rabshakeh levantou-se, e gritou com voz alta na língua dos judeus, e disse: “Ouvi as palavras do grande rei, o rei da Assíria!
Tsono kazembeyo anayimirira nafuwula mu Chihebri kuti, “Imvani mawu a mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya!
14 O rei diz: “Não deixeis que Ezequias vos engane, pois ele não poderá entregar-vos.
Zimene mfumu ikunena ndi izi: Musalole kuti Hezekiya akunamizeni. Iye sangakupulumutseni!
15 Não deixe que Ezequias o faça confiar em Iavé, dizendo: “Iavé certamente nos entregará”. Esta cidade não será entregue na mão do rei da Assíria”.
Hezekiya asakukakamizeni kudalira Yehova ndi mawu akuti, ‘Ndithu, Yehova adzatipulumutsa; ndipo sadzapereka mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya.’
16 Não dê ouvidos a Ezequias, pois o rei da Assíria diz: 'Façam as pazes comigo e venham a mim; e cada um de vocês coma de sua videira, e cada um de sua figueira, e cada um de vocês beba as águas de sua própria cisterna;
“Musamumvere Hezekiya. Zimene mfumu ya ku Asiriya ikunena ndi izi: Pangani mtendere ndi ine ndipo mutuluke mu mzinda. Mukatero aliyense wa inu adzadya mphesa ndi nkhuyu za mʼmunda mwake ndiponso adzamwa madzi a mʼchitsime chake,
17 até que eu venha e os leve para uma terra como sua própria terra, uma terra de grãos e vinho novo, uma terra de pão e vinhedos.
mpaka mfumuyo itabwera kudzakutengani kupita ku dziko lofanana ndi lanulo, dziko limene lili ndi tirigu ndi vinyo watsopano, dziko loyenda mkaka ndi uchi.
18 Cuidado para que Hezekiah não vos convença, dizendo: “Yahweh nos entregará”. Algum dos deuses das nações entregou suas terras da mão do rei da Assíria?
“Inu musalole kuti Hezekiya akusocheretseni pamene iye akuti, ‘Yehova adzatipulumutsa.’ Kodi alipo mulungu wa anthu a mtundu wina amene anapulumutsa dziko lake mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya?
19 Onde estão os deuses de Hamath e Arpad? Onde estão os deuses de Sefarvaim? Eles entregaram Samaria da minha mão?
Kodi ili kuti milungu ya Hamati ndi Aripadi? Ili kuti milungu ya Sefaravaimu? Kodi inapulumutsa Samariya mʼdzanja langa?
20 Quem são eles entre todos os deuses desses países que libertaram seu país da minha mão, que Javé deveria libertar Jerusalém da minha mão?'”.
Kodi ndi milungu iti mwa milungu yonse ya mayiko awa amene anapulumutsa dziko lake mʼdzanja? Nanga tsono Yehova adzapulumutsa Yerusalemu mʼdzanja langa motani?”
21 Mas eles permaneceram em silêncio, e nada disseram em resposta, pois o mandamento do rei era: “Não lhe responda”.
Koma anthu anakhala chete ndipo sanayankhepo kanthu, chifukwa mfumu inawalamula kuti, “Musayankhe.”
22 Então Eliakim, o filho de Hilkiah, que estava sobre a casa, e Shebna, o escriba, e Joah, o filho de Asaph, o gravador, vieram a Hezekiah com suas roupas rasgadas, e lhe contaram as palavras de Rabshakeh.
Pamenepo anthu atatu aja Eliyakimu, mwana wa Hilikiya amene ankayangʼanira nyumba ya mfumu; Sebina mlembi wa bwalo; ndi Yowa, mwana wa Asafu mlembi wa zochitika anapita kwa Hezekiya atangʼamba zovala zawo ndipo anamuwuza zonse zimene anayankhula kazembe uja.

< Isaías 36 >