< Isaías 33 >

1 Ai de vocês que destroem, mas não foram destruídos, e quem o traiu, mas ninguém o traiu! Quando você tiver terminado de destruir, será destruído; e quando você tiver terminado a traição, será traído.
Tsoka kwa iwe, iwe wowonongawe, amene sunawonongedwepo! Tsoka kwa iwe, iwe mthirakuwiri, iwe amene sunanyengedwepo! Iwe ukadzaleka kuwononga, udzawonongedwa, ukadzasiya umʼthirakuwiri, adzakuwononga, ndipo ukadzaleka kuchita zachinyengo adzakunyenga.
2 Yahweh, seja gracioso conosco. Nós esperamos por você. Seja nossa força todas as manhãs, nossa salvação também no momento de problemas.
Inu Yehova, mutikomere mtima ife; tikulakalaka Inu. Tsiku ndi tsiku mutitchinjirize ndi mkono wanu, ndipo mutipulumutse pa nthawi ya masautso.
3 Com o barulho do trovão, os povos fugiram. Quando você se levanta, as nações estão dispersas.
Mukatulutsa liwu lanu longa bingu mitundu ya anthu imathawa; pamene Inu mwadzambatuka mitundu ya anthu imabalalika.
4 Seu saque será recolhido quando a lagarta se reunir. Os homens saltarão sobre ele como os gafanhotos saltam.
Zofunkha za ku nkhondo za mitundu ina Aisraeli adzazisonkhanitsa ngati mmene limachitira dzombe. Iwo adzalumphira zofunkhazo monga mmene limachitira dzombe.
5 Yahweh é exaltado, pois mora nas alturas. Ele encheu Zion de justiça e retidão.
Yehova wakwezeka kwambiri pakuti amakhala pamwamba pa zonse adzadzaza Ziyoni ndi chilungamo ndi chipulumutso.
6 Haverá estabilidade em seu tempo, abundância de salvação, sabedoria e conhecimento. O medo de Yahweh é seu tesouro.
Iye adzakupatsani mtendere pa nthawi yanu, adzakupatsani chipulumutso chochuluka, nzeru zambiri ndi chidziwitso chochuluka; kuopa Yehova ngati madalitso.
7 Veja, seus valentes choram lá fora; os embaixadores da paz choram amargamente.
Taonani, anthu awo amphamvu akulira mofuwula mʼmisewu; akazembe okhazikitsa mtendere akulira kwambiri.
8 As rodovias estão desoladas. O homem viajante cessa. O convênio é quebrado. Ele desprezou as cidades. Ele não respeita o homem.
Mʼmisewu yayikulu mulibe anthu, mʼmisewu mulibe anthu a paulendo. Mdaniyo ndi wosasunga pangano. Iye amanyoza mboni. Palibe kulemekezana.
9 A terra chora e definha. O Líbano está confuso e murcha. Sharon é como um deserto, e Bashan e Carmel são despojados.
Dziko likulira ndipo likunka likutha. Nkhalango ya Lebanoni ikuchita manyazi, yafota. Chigwa cha chonde cha Saroni chasanduka chachidalala. Masamba a mitengo ya ku Basani ndi Karimeli akuyoyoka.
10 “Agora eu me levantarei”, diz Yahweh. “Agora eu me levantarei”. Agora vou ser exaltado.
Yehova akunena kuti, “Tsopano ndidzadzambatuka ndipo ndidzaonetsa mphamvu zanga, ndipo ndidzakwezedwa.
11 Você irá conceber o palhiço. Você dará à luz o restolho. Seu fôlego é um fogo que vai devorá-lo.
Zolingalira zanu nʼzachabechabe ngati udzu wamanyowa. Mpweya wamoto udzakupserezani.
12 Os povos serão como a queima de cal, como espinhos que são cortados e queimados no fogo.
Anthu a mitundu ina adzatenthedwa ngati miyala ya njereza; ndi ngati minga yodulidwa.”
13 Ouça, você que está muito longe, o que eu fiz; e, vocês que estão perto, reconheçam minha força”.
Inu amene muli kutali, imvani zimene ndachita; inu amene muli pafupi, dziwani mphamvu zanga
14 Os pecadores em Sião têm medo. O tremor tomou conta dos que não têm Deus. Quem entre nós pode viver com o fogo devorador? Quem entre nós pode viver com a queima eterna?
Mu mzinda wa Ziyoni anthu ochimwa agwidwa ndi mantha; anthu osapembedza Mulungu akunjenjemera: Iwo akunena kuti, “Ndani wa ife angathe kukhala mʼmoto wonyeketsa? Ndani wa ife angathe kukhala moto wosatha?”
15 Aquele que caminha com retidão e fala sem culpa, aquele que despreza o ganho das opressões, que gesticula com suas mãos, recusando-se a aceitar um suborno, que impede seus ouvidos de ouvir falar de derramamento de sangue, e fecha os olhos para não olhar para o mal...
Angathe kuti ndi amene amachita zolungama ndi kuyankhula zoona, amene amakana phindu lolipeza monyenga ndipo salola manja ake kulandira ziphuphu, amene amatseka makutu ake kuti angamve mawu opangana kupha anzawo ndipo amatsinzina kuti angaone zoyipa.
16 ele vai morar no alto. Seu lugar de defesa será a fortaleza das rochas. Seu pão será fornecido. Suas águas estarão certas.
Munthu wotere ndiye adzakhale pa nsanja, kothawira kwake kudzakhala mʼmalinga a mʼmapiri. Azidzalandira chakudya chake ndipo madzi sadzamusowa.
17 Seus olhos verão o rei em sua beleza. Eles verão uma terra distante.
Nthawi imeneyo maso a ana adzaona mfumu ya maonekedwe wokongola ndi kuona dziko lotambasukira kutali.
18 Seu coração meditará sobre o terror. Onde está aquele que contou? Onde está aquele que pesou? Onde está aquele que contou as torres?
Mu mtima mwanu muzidzalingalira zoopsa zinachitika kale zija: “Ali kuti mkulu wa Asilikali uja? Ali kuti wokhometsa misonkho uja? Ali kuti mkulu woyangʼanira nsanja?”
19 Você não verá mais as pessoas ferozes, um povo de um discurso profundo que você não consegue compreender, com uma linguagem estranha que você não consegue entender.
Simudzawaonanso anthu odzikuza aja, anthu aja achiyankhulo chosadziwika, chachilendo ndi chosamveka.
20 Veja em Zion, a cidade de nossos festivais nomeados. Seus olhos verão Jerusalém, uma morada tranqüila, uma tenda que não será removida. Suas estacas nunca serão arrancadas, nem nenhum de seus cordões será quebrado.
Taonani Ziyoni, mzinda wa zikondwerero zachipembedzo chathu; maso anu adzaona Yerusalemu, mzinda wamtendere, tenti imene sidzachotsedwa, zikhomo zake sizidzazulidwa, kapena zingwe zake kuduka.
21 Mas lá Yahweh estará conosco em majestade, um lugar de amplos rios e riachos, na qual nenhuma galera com remos irá, nem nenhum navio galante passará por lá.
Kumeneko Yehova adzaonetsa ulemerero wake ndipo mzindawo udzakhala kasupe wa mitsinje yayikulu. Ngalawa za zopalasa sizidzapitamo, sitima zapamadzi zikuluzikulu sizidzayendamo.
22 Pois Yahweh é nosso juiz. Yahweh é nosso legislador. Yahweh é nosso rei. Ele nos salvará.
Pakuti Yehova ndi woweruza wathu, Yehova ndiye wotilamulira, Yehova ndiye mfumu yathu; ndipo ndiye amene adzatipulumutse.
23 Seu armamento é desvinculado. Eles não puderam fortalecer o pé de seu mastro. Eles não conseguiam espalhar a vela. Então a presa de um grande saque foi dividida. O coxo levou a presa.
Zingwe za sitima zapamadzi za adani athu zamasuka, sizikutha kulimbitsa mlongoti wake, matanga ake sakutheka kutambasuka. Ngakhale tidzagawana zofunkha zochuluka kwambiri ndipo ngakhale olumala adzatenga zofunkhazo.
24 O habitante não vai dizer: “Estou doente”. As pessoas que habitam ali serão perdoadas de sua iniqüidade.
Palibe ndi mmodzi yemwe wokhala mʼZiyoni adzanene kuti, “Ndikudwala” ndipo anthu onse okhala mʼmenemo machimo awo adzakhululukidwa.

< Isaías 33 >