< Êxodo 12 >

1 Yahweh falou com Moisés e Aarão na terra do Egito, dizendo:
Yehova anayankhula kwa Mose ndi Aaroni mʼdziko la Igupto kuti,
2 “Este mês será para vocês o início dos meses. Será para vocês o primeiro mês do ano.
“Mwezi uno uzikhala mwezi wanu woyamba wa chaka.
3 Falou a toda a congregação de Israel, dizendo: “No décimo dia deste mês, levarão a cada homem um cordeiro, de acordo com a casa de seus pais, um cordeiro para uma casa;
Muliwuze khamu lonse la Israeli kuti pa tsiku la khumi la mwezi uno, munthu aliyense asankhire banja lake mwana wankhosa mmodzi. Banja lililonse litenge mwana wankhosa mmodzi.
4 e se a casa for muito pequena para um cordeiro, então ele e seu vizinho ao lado de sua casa levarão um de acordo com o número de almas. Você fará sua contagem para o cordeiro de acordo com o que todos podem comer.
Ngati banja lili lochepa moti silingathe kudya nyama yonse ya nkhosa, ligawane ndi banja lomwe layandikana nalo nyumba. Mabanja adziwiretu chiwerengero cha anthu amene alipo pokonzekera zimenezi. Muwerengere kuchuluka kwa nyama imene anthu adzadye potengera mmene munthu mmodzi angadyere.
5 Seu cordeiro deve ser sem defeito, um macho de um ano. Você o tirará das ovelhas ou dos cabritos.
Ziweto zimene musankhe ziyenera kukhala zazimuna za chaka chimodzi, zopanda chilema, ndipo zikhale nkhosa kapena mbuzi.
6 Você o guardará até o décimo quarto dia do mesmo mês; e toda a assembléia da congregação de Israel o matará à noite.
Muzisunge mpaka tsiku la khumi ndi chinayi la mwezi, pamene gulu lonse la Aisraeli lidzaphe nyamazo madzulo.
7 Pegarão um pouco do sangue e o colocarão nos dois postes das portas e no lintel, nas casas em que o comerão.
Ndipo adzatengeko magazi anyamazo ndi kuwaza pa mphuthu ziwiri za chitseko ndiponso pamwamba pa chitseko cha nyumba mmene adzadyeremo ana ankhosawo.
8 comerão a carne naquela noite, assada com fogo, com pão ázimo. Eles a comerão com ervas amargas.
Adzawotche nyamayo ndi kudya usiku womwewo, ndipo adzayidye ndi buledi wophikidwa popanda yisiti pamodzi ndi masamba wowawa.
9 Não a comerão crua, nem cozida com água, mas assada com fogo; com sua cabeça, suas pernas e suas partes internas.
Musadzadye yayiwisi kapena yophika, koma mudzawotche yonse, mutu, miyendo ndi zamʼmimba.
10 Nada restará dele até a manhã; mas o que restar dele até a manhã, queimará com fogo.
Musadzasiye nyama ina mpaka mmawa, ngati ina idzatsala mpaka mmawa, mudzayitenthe.
11 Assim o comerás: com teu cinto na cintura, tuas sandálias nos pés e teu cajado na mão; e o comerás apressadamente: é a Páscoa de Yahweh.
Muzidzadya nyamayo mutavala chotere, pokonzekera ulendo: mudzazimangirire lamba mʼchiwuno, nsapato zanu kuphazi ndi ndodo yanu kumanja. Mudzadye mofulumira. Imeneyi ndi Paska ya Yehova.
12 Pois eu atravessarei a terra do Egito naquela noite, e atingirei todos os primogênitos na terra do Egito, tanto o homem como o animal. Executarei julgamentos contra todos os deuses do Egito. Eu sou Yahweh.
“Usiku umenewo Ine ndidzadutsa mʼdziko la Igupto ndipo ndidzapha chilichonse choyamba kubadwa kuyambira mwana wa munthu aliyense mpaka ana aziweto. Ndidzalanganso milungu yonse ya Igupto. Ine ndine Yehova.
13 O sangue será para vocês um sinal sobre as casas onde vocês estão. Quando eu vir o sangue, passarei por cima de vocês, e nenhuma praga estará sobre vocês para destruí-los quando eu atacar a terra do Egito.
Magazi amene mudzawaze pa mphuthu za zitseko ndi pamwamba pa zitseko aja adzakhala ngati chizindikiro. Ine ndikadzaona magaziwo ndidzakudutsani, ndipo ndikadzamakantha anthu a Igupto, mliri wosakazawu sudzakukhudzani.
14 Este dia será um memorial para vocês. Você o guardará como um banquete para Iavé. Guardá-lo-eis para sempre como um banquete ao longo de vossas gerações por uma portaria.
“Ili ndi tsiku la chikumbutso. Tsiku limeneli muzidzachita chikondwerero, kupembedza Yehova. Mibado yonse imene ikubwera izidzakumbukira tsiku limeneli ngati lamulo lamuyaya ndi kuti pa tsikuli azidzachita chikondwerero cholemekeza Yehova.
15 “'Sete dias comereis pães ázimos; mesmo no primeiro dia tirareis fermento de vossas casas, pois quem comer pão fermentado desde o primeiro dia até o sétimo dia, essa alma será extirpada de Israel.
Kwa masiku asanu ndi awiri muzidya buledi wopanda yisiti. Tsiku loyamba muzichotsa yisiti mʼnyumba zanu, ngati aliyense adzadya kanthu kalikonse kali ndi yisiti kuyambira tsiku loyamba mpaka tsiku lachisanu ndi chiwiri, munthu ameneyo adzayenera kuchotsedwa mʼgulu la Israeli.
16 No primeiro dia haverá para vós uma santa convocação, e no sétimo dia uma santa convocação; nenhum tipo de trabalho será feito neles, exceto o que todo homem deve comer, somente o que pode ser feito por vós.
Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika, ndipo winanso uzikhala pa tsiku lachisanu ndi chiwiri. Musamagwire ntchito masiku onsewa, koma ntchito yokonza chakudya yokha kuti aliyense adye. Izi ndi zimene muzichita.
17 Observareis a festa dos pães ázimos; pois neste mesmo dia trouxe vossos exércitos para fora da terra do Egito. Portanto, observareis este dia através de vossas gerações por uma ordenança para sempre.
“Muzichita chikondwerero cha buledi wopanda yisiti, chifukwa ndi pa tsiku limeneli ndinatulutsa magulu anu mʼdziko la Igupto. Muzikondwerera tsiku limeneli pa mibado yonse ngati lamulo lamuyaya.
18 No primeiro mês, no décimo quarto dia do mês à noite, comereis pães ázimos, até o vigésimo primeiro dia do mês à noite.
Mwezi woyamba muzidzadya buledi wopanda yisiti kuyambira madzulo tsiku la 14 la mweziwo mpaka tsiku la 21 mwezi womwewo.
19 Não será encontrado fermento em vossas casas durante sete dias, pois quem comer o fermento, essa alma será excluída da congregação de Israel, seja estrangeiro, seja nascido na terra.
Yisiti asamapezeka mʼnyumba zanu kwa masiku asanu ndi awiri. Ndipo aliyense amene adya chakudya chimene muli yisiti, munthu ameneyo ayenera kuchotsedwa mʼgulu la Aisraeli, kaya iyeyo ndi mlendo kapena mbadwa.
20 Nada comerá fermentado. Em todas as vossas habitações comereis pão ázimo”.
Musadye chilichonse chokhala ndi yisiti. Kulikonse kumene mukukhala, muyenera kudya buledi wopanda yisiti.”
21 Então Moisés chamou todos os anciãos de Israel e lhes disse: “Saiam e levem cordeiros de acordo com suas famílias, e matem a Páscoa”.
Ndipo Mose anasonkhanitsa akuluakulu onse a Israeli nati, “Pitani msanga kukasankha nkhosa zokwanira pa mabanja anu, ndipo muziphe ngati Paska.
22 Pegue um monte de hissopo e mergulhe-o no sangue que está na bacia, e bata o lintel e os dois postes da porta com o sangue que está na bacia. Nenhum de vocês deve sair da porta de sua casa até a manhã seguinte.
Mutengenso nthambi ya chitsamba cha hisope, muchiviyike mʼmagazi amene mwawayika mʼbeseni ndipo muwaze ena mwa magaziwo pamwamba ndi mʼmbali mwa mphuthu za chitseko. Palibe aliyense wa inu amene adzatuluke mʼnyumba yake mpaka mmawa.
23 Pois Yahweh passará para atingir os egípcios; e quando vir o sangue no lintel, e nos dois postes da porta, Yahweh passará por cima da porta, e não permitirá que o destruidor entre em suas casas para atingi-lo.
Pamene Yehova adzadutsa mʼdziko kudzakantha Aigupto, nʼkuona magazi pamwamba ndi mʼmbali mwa mphuthu za chitseko, Iye adzadutsa khomo limenelo ndipo sadzalola woonongayo kuti alowe mʼnyumba zanu kuti akukantheni.
24 Você observará isto para uma ordenança a você e a seus filhos para sempre.
“Muzimvera malamulo amenewa kwa muyaya, inu ndi zidzukulu zanu.
25 Acontecerá quando vocês chegarem à terra que Yahweh lhes dará, como ele prometeu, que vocês manterão este serviço.
Mukakalowa mʼdziko limene Yehova adzakupatseni monga analonjeza, mukasunge mwambo umenewu.
26 Acontecerá, quando seus filhos lhe perguntarem: 'O que você quer dizer com este serviço?
Ndipo ana anu akakakufunsani kuti, ‘Mwambo umenewu ukutanthauza chiyani?’
27 que você dirá: 'É o sacrifício da Páscoa de Javé, que passou por cima das casas dos filhos de Israel no Egito, quando ele atingiu os egípcios, e poupou nossas casas'”. O povo curvou a cabeça e adorou.
Inu mukawawuze kuti, ‘Ndi nsembe ya Paska ya Yehova, popeza pamene ankakantha nyumba za Aigupto anasiya nyumba zathu.’” Kenaka anthu anawerama napembedza.
28 Os filhos de Israel foram e o fizeram; como Javé havia ordenado a Moisés e Arão, assim o fizeram.
Aisraeli anachita monga momwe Yehova analamulira Mose ndi Aaroni.
29 À meia-noite, Javé atingiu todos os primogênitos na terra do Egito, desde o primogênito do Faraó que se sentou em seu trono até o primogênito do cativo que estava no calabouço, e todos os primogênitos do gado.
Pakati pa usiku Yehova anakantha ana onse oyamba kubadwa mʼdziko la Igupto, kuyambira woyamba kubadwa wa Farao, amene amakhala pa mpando waufumu wa Faraoyo, mpaka mwana woyamba kubadwa wa munthu amene anali mʼdzenje, pamodzinso ndi ana oyamba kubadwa a ziweto zawo.
30 O Faraó levantou-se à noite, ele, e todos os seus servos, e todos os egípcios; e houve um grande grito no Egito, pois não havia uma casa onde não houvesse um morto.
Farao ndi nduna zake zonse ndiponso Aigupto onse anadzuka pakati pa usiku, ndipo kunali kulira kwakukulu mʼdziko lonse la Igupto, pakuti panalibe nyumba imene munalibe munthu wakufa.
31 Ele chamou por Moisés e Aarão à noite, e disse: “Levantai-vos, saí do meio do meu povo, tanto vós como os filhos de Israel; e ide, servi a Iavé, como haveis dito!
Pakati pa usiku Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni ndipo anati, “Nyamukani! Asiyeni anthu anga, inu ndi Aisraeli! Pitani, kapembedzeni Yehova monga munapempha.
32 Levem seus rebanhos e seus rebanhos, como vocês disseram, e desapareçam; e abençoem-me também”!
Tengani ziweto ndi ngʼombe zanu ndipo pitani kapembedzeni Mulungu wanu monga munanenera kuti ine ndidalitsike.”
33 Os egípcios tinham urgência com o povo, para enviá-los para fora da terra à pressa, pois diziam: “Somos todos homens mortos”.
Aigupto anawawumiriza anthuwo kuti atuluke mofulumira ndi kusiya dziko lawo. Iwo anati, “Ngati sitiwalola kutero, tonse tidzafa.”
34 O povo tomou sua massa antes que ela fosse fermentada, suas cochos de amassar sendo amarrados em suas roupas sobre seus ombros.
Motero anthuwo ananyamula ufa wawo wopangira buledi asanathiremo yisiti ndipo anasenza pa mapewa awo pamodzi ndi zokandiramo buledi atazikulunga mu nsalu.
35 Os filhos de Israel fizeram de acordo com a palavra de Moisés; e pediram aos egípcios jóias de prata, e jóias de ouro, e roupas.
Aisraeli anachita monga anawawuzira Mose kuti apemphe kwa Aigupto zozikongoletsera zasiliva ndi zagolide ndi zovala.
36 Yahweh deu ao povo um favor aos olhos dos egípcios, para que eles pudessem ter o que pediram. Eles saquearam os egípcios.
Yehova anafewetsa mtima Aigupto kuti akomere mtima Aisraeliwo ndipo anawapatsa zimene anawapempha. Motero Aisraeli anawalanda zinthu Aigupto.
37 As crianças de Israel viajaram de Ramsés a Succoth, cerca de seiscentos mil a pé, que eram homens, além de crianças.
Aisraeli anayenda ulendo kuchokera ku Ramesesi mpaka kukafika ku Sukoti. Anthu aamuna oyenda pansi analipo 600,000 osawerengera akazi ndi ana.
38 Uma multidão mista subiu também com eles, com rebanhos, rebanhos e até mesmo muito gado.
Anthu enanso ambiri anapita nawo, kuphatikizanso gulu lalikulu la ziweto, mbuzi, nkhosa pamodzi ndi ngʼombe.
39 Cozinharam bolos ázimos da massa que trouxeram do Egito; pois não era fermentado, porque foram expulsos do Egito, e não podiam esperar, e não tinham preparado nenhum alimento para si mesmos.
Iwo anapanga buledi wopanda yisiti ndi ufa umene anachoka nawo ku Igupto. Ufawo unalibe yisiti chifukwa anachita kuthamangitsidwa ku Igupto ndipo analibe nthawi yokonzera chakudya chawo.
40 Agora o tempo em que as crianças de Israel viviam no Egito era de quatrocentos e trinta anos.
Ndipo Aisraeli anakhala ku Igupto kwa zaka 430.
41 Ao final de quatrocentos e trinta anos, até hoje, todos os exércitos de Iavé saíram da terra do Egito.
Pa tsiku lomwelo limene anakwanitsa zaka 430, magulu onse a Yehova anatuluka mʼdziko la Igupto.
42 É uma noite a ser muito observada para Iavé por tirá-los da terra do Egito. Esta é aquela noite de Iavé, a ser muito observada por todos os filhos de Israel através de suas gerações.
Usiku wonse Yehova anachezera kutulutsa ana a Israeli mʼdziko la Igupto. Nʼchifukwa chake pa tsiku limeneli Aisraeli onse azichezera usiku wonse kulemekeza Mulungu kamba ka mibado yonse ya mʼtsogolo.
43 Yahweh disse a Moisés e Arão: “Esta é a ordenança da Páscoa. Nenhum estrangeiro comerá dela,
Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni, “Malamulo a Paska ndi awa: “Mlendo asadye Paska.
44 mas o servo de todo homem que for comprado por dinheiro, quando o tiver circuncidado, então ele comerá dela.
Kapolo aliyense amene munagula angadye ngati atayamba wachita mdulidwe.
45 Um estrangeiro e um servo contratado não comerão dela.
Koma amene mukukhala naye kwa kanthawi kapena waganyu asadye Paska.
46 Deve ser comido em uma casa. Não deverá carregar nenhuma das carnes fora da casa. Não deve quebrar nenhum de seus ossos.
“Muzidyera Paska mʼnyumba imodzi. Musatulutse nyama iliyonse kunja kwa nyumba. Musaswe mafupa aliwonse.
47 Toda a congregação de Israel deve guardá-la.
Gulu lonse la Israeli lizichita mwambo wachikondwererochi.
48 Quando um estranho viver como estrangeiro com você, e quiser guardar a Páscoa para Javé, que todos os seus machos sejam circuncidados, e então que ele se aproxime e a guarde. Ele será como aquele que nasce na terra; mas nenhuma pessoa incircuncisada comerá dela.
“Ngati mlendo wokhala pakati panu angafune kuchita nawo mwambo wa chikondwerero cha Paska, cha Yehovachi, amuna onse a mʼnyumba mwake ayenera kuchita mdulidwe. Akatero muzimutenga ngati mbadwa pakati panu. Koma aliyense wosachita mdulidwe asadye Paska.
49 Uma lei será para aquele que nasceu em casa, e para o estrangeiro que vive como um estrangeiro entre vós”.
Lamulo limeneli likhudza mbadwa ngakhalenso alendo wochita mdulidwe wokhala pakati panu.
50 Todos os filhos de Israel o fizeram. Como Javé ordenou a Moisés e Arão, assim o fizeram.
“Aisraeli onse anachita monga momwe Yehova analamulira Mose ndi Aaroni.
51 Nesse mesmo dia, Javé tirou os filhos de Israel da terra do Egito por seus exércitos.
Ndipo tsiku lomwelo Yehova anatulutsa gulu lonse la ana a Israeli mʼdziko la Igupto.”

< Êxodo 12 >