< 2 Reis 20 >
1 Naqueles dias, Hezekiah estava doente e morrendo. Isaías, o profeta filho de Amoz, veio até ele e lhe disse: “Javé diz: 'Ponha sua casa em ordem, pois você morrerá e não viverá'”.
Masiku amenewo Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Mneneri Yesaya, mwana wa Amozi anapita kukamuona ndipo anamuwuza kuti, “Yehova akuti: Konza nyumba yako chifukwa umwalira ndipo suchira.”
2 Então ele virou seu rosto para a parede e rezou a Javé, dizendo:
Hezekiya anatembenuka nayangʼana ku khoma ndipo anapemphera kwa Yehova kuti,
3 “Lembre-se agora, Javé, eu lhe imploro, como eu caminhei diante de você em verdade e com um coração perfeito, e fiz o que é bom à sua vista”. E Hezekiah chorou amargamente.
“Inu Yehova, kumbukirani ndithu mmene ndayendera mokhulupirika ndi mtima wonse ndipo ndachita zolungama pamaso panu.” Hezekiya analira kwambiri.
4 Antes de Isaías ter saído para a parte central da cidade, a palavra de Javé veio a ele, dizendo:
Yesaya asanatuluke mʼbwalo lapakati, Yehova anayankhula kuti,
5 “Volte para trás e diga a Ezequias, o príncipe do meu povo: 'Javé, o Deus de Davi, seu pai, diz: “Ouvi a sua oração. Eu vi suas lágrimas. Eis que eu te curarei”. No terceiro dia, você irá até a casa de Iavé.
“Bwerera, kamuwuze Hezekiya mtsogoleri wa anthu anga kuti, ‘Yehova Mulungu wa Davide kholo lako akuti: Ndamva pemphero lako ndipo misozi yako ndayiona ndipo ndidzakuchiritsa. Tsiku lachitatu kuchokera lero udzapita ku Nyumba ya Yehova.
6 Acrescentarei a seus dias quinze anos. Eu te entregarei a ti e a esta cidade da mão do rei da Assíria. Defenderei esta cidade por mim e pelo meu servo Davi””.
Ndidzawonjezera zaka khumi ndi zisanu pa moyo wako. Ndidzakupulumutsa iwe pamodzi ndi mzinda umenewu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya. Ndidzateteza mzinda umenewu chifukwa cha Ine mwini ndiponso chifukwa cha Davide mtumiki wanga.’”
7 Isaías disse: “Pegue um bolo de figos”. Eles o pegaram e colocaram em ebulição, e ele se recuperou.
Pamenepo Yesaya anati, “Konzani phala lankhuyu.” Iwo anakonza phalalo nalipaka pa chithupsacho ndipo Hezekiya anachira.
8 Hezekiah disse a Isaías: “Qual será o sinal de que Javé me curará e que eu subirei à casa de Javé no terceiro dia?
Tsono Hezekiya anafunsa Yesaya kuti, “Kodi padzakhala chizindikiro chanji choonetsa kuti Yehova adzandichiritsa ndi kuti ndidzapita ku Nyumba ya Yehova pa tsiku lachitatu kuchokera lero lino?”
9 Isaías disse: “Este será o sinal para você de Javé, que Javé fará o que ele falou: a sombra deve avançar dez passos, ou retroceder dez passos”?
Yesaya anayankha kuti, “Chizindikiro cha Yehova chosonyeza kuti Iye adzachita chimene walonjeza ndi ichi: Kodi chithunzithunzi chipite patsogolo kapena chibwerere pambuyo makwerero khumi?”
10 Hezekiah respondeu: “É uma coisa leve para a sombra dar dez passos à frente. Não, mas deixe a sombra voltar dez passos para trás”.
Hezekiya anati, “Nʼchapafupi kuti chithunzithunzi chipite patsogolo makwerero khumi, kulekana nʼkuti chithunzithunzicho chibwerere mʼmbuyo makwerero khumi.”
11 Isaías, o profeta, chorou a Javé; e trouxe a sombra dez passos para trás, através dos quais ela tinha descido sobre o relógio de sol de Ahaz.
Pamenepo mneneri Yesaya anapemphera kwa Yehova ndipo Yehova anachititsa kuti chithunzithunzi chibwerere mʼmbuyo makwerero khumi pa makwerero amene mfumu Ahazi anamanga.
12 Naquele tempo Berodach Baladan, filho de Baladan, rei da Babilônia, enviou cartas e um presente a Ezequias, pois tinha ouvido dizer que Ezequias tinha estado doente.
Pa nthawi imeneyo Merodaki-Baladani mwana wa Baladani mfumu ya Babuloni anatumiza amithenga kwa Hezekiya kukapereka makalata ndi mphatso, chifukwa nʼkuti atamva za kudwala kwa Hezekiyayo.
13 Ezequias ouviu-os e mostrou-lhes todo o depósito de suas preciosidades - a prata, o ouro, as especiarias e o óleo precioso, e a casa de sua armadura, e tudo o que foi encontrado em seus tesouros. Não havia nada em sua casa, ou em todo seu domínio, que Hezekiah não lhes mostrasse.
Hezekiya analandira amithengawo ndipo anawaonetsa zonse zimene zinali mʼnyumba zake zosungiramo chuma. Anawaonetsa siliva, golide, zonunkhiritsa zakudya ndi mafuta abwino kwambiri, zida zake zankhondo ndiponso china chilichonse chimene chinali mosungiramo zinthu zake. Panalibe chinthu mʼnyumba yake yaufumu kapena mu ufumu wake wonse chimene Hezekiya sanawaonetse.
14 Então o profeta Isaías veio ao rei Ezequias e lhe disse: “O que estes homens disseram? De onde eles vieram até você”? Hezekiah disse: “Eles vieram de um país distante, mesmo da Babilônia”.
Tsono mneneri Yesaya anapita kwa Mfumu Hezekiya namufunsa kuti, “Kodi anthu aja anakuwuzani zotani ndipo anachokera kuti?” Hezekiya anayankha kuti, “Anachokera ku dziko lakutali, ku Babuloni.”
15 Ele disse: “O que eles viram em sua casa”? Hezekiah respondeu: “Eles viram tudo o que há em minha casa. Não há nada entre meus tesouros que eu não tenha mostrado a eles”.
Mneneriyo anafunsa kuti, “Kodi anaona chiyani mʼnyumba yanu yaufumu?” Hezekiya anayankha kuti, “Anaona china chilichonse mʼnyumba yanga yaufumu ndipo palibe ndi chinthu chimodzi chomwe chimene sindinawaonetse mʼnyumba zanga zosungiramo chuma.”
16 Isaías disse a Hezekiah: “Escutai a palavra de Javé”.
Pamenepo Yesaya anawuza Hezekiya kuti, “Imvani zimene Yehova akunena:
17 'Eis que vêm os dias em que tudo o que está em sua casa, e tudo o que seus pais guardaram até hoje, será levado para a Babilônia. Nada restará”, diz Javé.
Taonani, masiku akubwera ndithu pamene zonse za mʼnyumba yanu yaufumu, zonse zimene makolo anu anazisunga mpaka lero, zidzatengedwa kupita ku Babuloni. Palibe chimene chidzatsale, akutero Yehova.
18 'Eles tirarão alguns de seus filhos que emitirão de você, que você será pai; e eles serão eunucos no palácio do rei da Babilônia'”.
Ndipo ena mwa ana anu omwe, amene mudzabereke adzatengedwa ndipo adzawasandutsa anthu ofulidwa mʼnyumba yaufumu ya mfumu ya Babuloni.”
19 Então Hezekiah disse a Isaías: “A palavra de Javé que você falou é boa”. Ele disse ainda: “Não é assim, se a paz e a verdade estiverem em meus dias?”
Hezekiya anayankha kuti, “Mawu a Yehova amene mwayankhulawa ndi abwino. Pakuti iye ankaganiza kuti, ‘Kodi pa nthawi yanga sipadzakhala mtendere ndi bata?’”
20 Agora o resto dos atos de Ezequias, e todas as suas forças, e como ele fez a piscina, e o conduto, e trouxe água para a cidade, não estão escritos no livro das crônicas dos reis de Judá?
Ntchito zina za Hezekiya ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
21 Ezequias dormiu com seus pais, e Manassés seu filho reinou em seu lugar.
Hezekiya anamwalira nagona pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Manase mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.