< Salmos 75 >
1 Para o regente, conforme “altachete”; salmo e cântico de Asafe: Louvamos a ti, ó Deus; louvamos, e perto [está] o teu nome; são anunciadas as tuas maravilhas.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Salimo la Asafu. Nyimbo. Tikuthokoza Inu Mulungu, tikuthokoza, pakuti dzina lanu lili pafupi nafe, anthutu amafotokoza za ntchito zanu zodabwitsa.
2 O que eu recebi, no [tempo] determinado, julgarei de forma justa.
Mumati, “Ine ndimayika nthawi yoyenera, ndine amene ndimaweruza mwachilungamo.
3 A terra e todos os seus moradores [são] dissolvidos; [porém] eu fortifiquei suas colunas. (Selá)
Pamene dziko lapansi ndi anthu ake onse anjenjemera, ndine amene ndimagwiriziza mizati yake molimba. (Sela)
4 Eu disse aos orgulhosos: Não sejais orgulhosos! E aos perversos: Não exalteis o vosso poder!
Kwa odzitama ndikuti, ‘Musadzitamenso,’ ndipo kwa oyipa, ‘Musatukulenso nyanga zanu.
5 Não confieis em vosso poder, nem faleis com arrogância.
Musatukule nyanga zanu motsutsana ndi kumwamba; musayankhule ndi khosi losololoka.’”
6 Porque a exaltação não vem do oriente, nem do ocidente, nem do deserto;
Kugamula milandu sikuchokera kummawa kapena kumadzulo kapena ku chipululu.
7 Mas sim [de] Deus, que é o Juiz; ele abate a um, e exalta a outro.
Koma ndi Mulungu amene amaweruza: Iyeyo amatsitsa wina, nakwezanso wina.
8 Porque o SENHOR [tem] um copo na mão; com vinho espumado, cheio de mistura, e ele o derramará; e os perversos da terra o beberão e sugarão até seus restos.
Mʼdzanja la Yehova muli chikho chodzaza ndi vinyo wochita thovu, wosakanizidwa ndi zokometsera; Iye amamutsanulira pansi ndipo onse oyipa a dziko lapansi amamwa ndi senga zake zonse.
9 Mas eu [o] anunciarei para sempre; cantarei louvores ao Deus de Jacó.
Kunena za ine, ndidzalengeza izi kwamuyaya; ndidzayimba matamando kwa Mulungu wa Yakobo.
10 E cortarei todas as arrogâncias dos perversos; [mas] os rostos dos justos serão exaltados.
Ndidzadula nyanga za onse oyipa koma nyanga za olungama zidzakwezedwa.