< Salmos 50 >

1 Salmo de Asafe: Deus, o SENHOR Deus fala e chama a terra, desde onde o sol nasce até onde ele se põe.
Salimo la Asafu. Wamphamvuyo, Yehova Mulungu, akuyankhula ndi kuyitanitsa dziko lapansi kuyambira kotulukira dzuwa mpaka kumene limalowera.
2 Desde Sião, a perfeição da beleza, Deus mostra seu imenso brilho.
Kuchokera ku Ziyoni, mokongola kwambiri Mulungu akuwala.
3 Nosso Deus virá, e não ficará calado; fogo queimará adiante dele, e ao redor dele haverá grande tormenta.
Mulungu wathu akubwera ndipo sadzakhala chete; moto ukunyeketsa patsogolo pake, ndipo pomuzungulira pali mphepo yamkuntho
4 Ele chamará aos céus do alto, e à terra, para julgar a seu povo.
Iye akuyitanitsa zamumlengalenga ndi za pa dziko lapansi kuti aweruze anthu ake.
5 Ajuntai-me meus santos, que confirmam meu pacto por meio de sacrifício.
Mundisonkhanitsire okhulupirika anga, amene anachita pangano ndi ine pochita nsembe.
6 E os céus anunciarão sua justiça, pois o próprio Deus é o juiz. (Selá)
Ndipo mayiko akumwamba akulengeza chilungamo chake, pakuti Mulungu mwini ndi woweruza.
7 Ouve, povo meu, e eu falarei; eu darei testemunho contra ti, Israel; eu sou Deus, o teu Deus.
Imvani inu anthu anga, ndipo Ine ndidzayankhula, iwe Israeli, ndipo Ine ndidzayankhula mokutsutsa; ndine Mulungu, Mulungu wako.
8 Eu não te repreenderei por causa de teus sacrifícios, porque teus holocaustos estão continuamente perante mim.
Sindikudzudzula chifukwa cha nsembe zako, kapena nsembe zako zopsereza zimene zili pamaso panga nthawi zonse.
9 Não tomarei bezerro de tua casa, [nem] bodes de teus currais;
Ine sindikufuna ngʼombe yayimuna kuchokera mʼkhola lako kapena mbuzi za mʼkhola lako,
10 Porque todo animal das matas é meu, [e também] os milhares de animais selvagens das montanhas.
pakuti nyama iliyonse yakunkhalango ndi yanga ndiponso ngʼombe za ku mapiri ochuluka.
11 Conheço todas as aves das montanhas, e as feras do campo [estão] comigo.
Ine ndimadziwa mbalame iliyonse mʼmapiri ndiponso zolengedwa zonse zakutchire ndi zanga.
12 Se eu tivesse fome, não te diria, porque meu é o mundo, e tudo o que nele há.
Ndikanakhala ndi njala sindikanakuwuzani, pakuti dziko lonse ndi zonse zimene zili mʼmenemo ndi zanga.
13 Comeria eu carne de touros, ou beberia sangue de bodes?
Kodi ndimadya nyama ya ngʼombe zazimuna kapena kumwa magazi a mbuzi?
14 Oferece a Deus sacrifício de louvor, e paga ao Altíssimo os teus votos.
“Pereka nsembe zachiyamiko kwa Mulungu, kwaniritsa malonjezo ako kwa Wammwambamwamba.
15 E clama a mim no dia da angústia; e eu te farei livre, e tu me glorificarás.
Ndipo undiyitane pa tsiku lako la masautso; Ine ndidzakulanditsa, ndipo udzandilemekeza.”
16 Mas Deus diz ao perverso: Para que tu recitas meus estatutos, e pões meu pacto em tua boca?
Koma kwa woyipa, Mulungu akuti, “Kodi uli ndi mphamvu yanji kuti uzinena malamulo anga kapena kutenga pangano langa pa milomo yako?
17 Pois tu odeias a repreensão, e lança minhas palavras para detrás de ti.
Iwe umadana ndi malangizo anga ndipo umaponyera kumbuyo kwako mawu anga.
18 Se vês ao ladrão, tu consentes com ele; e tens tua parte com os adúlteros.
Ukaona wakuba umamutsatira, umachita maere ako pamodzi ndi achigololo
19 Com tua boca pronuncias o mal, e tua língua gera falsidades.
Umagwiritsa ntchito pakamwa pako pa zinthu zoyipa ndipo umakonza lilime lako kuchita chinyengo.
20 Tu te sentas [e] falas contra teu irmão; contra o filho de tua mãe tu dizes ofensas.
Nthawi zonse umayankhula motsutsana ndi mʼbale wako ndipo umasinjirira mwana wa amayi ako enieni.
21 Tu fazes estas coisas, e eu fico calado; pensavas que eu seria como tu? Eu te condenarei, e mostrarei [teus males] diante de teus olhos.
Wachita zimenezi ndipo Ine ndinali chete; umaganiza kuti ndine wofanana nawe koma ndidzakudzudzula ndipo ndidzakutsutsa pamaso pako.
22 Entendei, pois, isto, vós que vos esqueceis de Deus; para que eu não [vos] faça em pedaços, e não haja quem [vos] livre.
“Ganizira izi, iwe amene umayiwala Mulungu kuti ndingakukadzule popanda wokupulumutsa:
23 Quem oferece sacrifício de louvor me glorificará, e ao que cuida de seu caminho, eu lhe mostrarei a salvação de Deus.
Iye amene amapereka nsembe yamayamiko amandilemekeza, ndipo amakonza njira zake kuti ndimuonetse chipulumutso cha Mulungu.”

< Salmos 50 >