< Salmos 44 >
1 Instrução para o regente; dos filhos de Coré: Ó Deus, com nossos ouvidos ouvimos, nossos pais nos contaram a obra que tu fizeste nos seus dias, nos dias antigos.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Ife tamva ndi makutu athu, Inu Mulungu; makolo athu atiwuza zimene munachita mʼmasiku awo, masiku akalekalewo.
2 Para plantá-los, expulsaste as nações com a tua própria mão; para fazê-los crescer, afligiste os povos.
Ndi dzanja lanu munathamangitsa mitundu ya anthu ena ndi kudzala makolo athu; Inu munakantha mitundu ya anthu, koma makolo athuwo Inu munawapatsa ufulu.
3 Porque não conquistaram a terra pelas espadas deles, nem o braço deles os salvou; mas sim tua mão direita e o teu braço, e a luz de teu rosto; porque tu os favoreceste.
Sanalande dziko ndi lupanga lawo, si mkono wawo umene unawabweretsera chigonjetso, koma ndi dzanja lanu lamanja, mkono wanu ndi kuwala kwa nkhope yanu, pakuti munawakonda.
4 Deus, tu és meu Rei; ordena salvações a Jacó.
Inu ndinu Mfumu yanga ndi Mulungu wanga amene mumalamulira chigonjetso cha Yakobo.
5 Por ti venceremos nossos adversários; por teu nome passaremos por cima dos que se levantam contra nós.
Kudzera kwa inu ife timabweza adani athu; kudzera mʼdzina lanu timapondereza otiwukirawo.
6 Porque minha confiança não está em meu arco; nem minha espada me salvará.
Sindidalira uta wanga, lupanga langa silindibweretsera chigonjetso;
7 Pois tu nos salvaste de nossos adversários, e envergonhaste aos que nos odeiam.
koma Inu mumatigonjetsera adani athu, mumachititsa manyazi amene amadana nafe.
8 Nós exaltamos a Deus o dia todo; e louvaremos o teu nome para sempre. (Selá)
Timanyadira mwa Mulungu wathu tsiku lonse, ndipo tidzatamanda dzina lanu kwamuyaya.
9 Mas [agora] tu tens nos rejeitado e envergonhado; e tu não tens saído junto com nossos exércitos.
Koma tsopano mwatikana ndi kutichepetsa; Inu simupitanso ndi ankhondo athu.
10 Tu nos fazes fugir do adversário, e aqueles que nos odeiam saqueiam [de nós] para si.
Munachititsa ife kubwerera mʼmbuyo pamaso pa mdani ndipo amene amadana nafe atilanda katundu.
11 Tu nos entregas como ovelhas para serem comidas, e nos espalhas entre as nações.
Inu munatipereka kuti tiwonongedwe monga nkhosa ndipo mwatibalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina.
12 Tu vendes a teu povo ao preço de nada, e não aumentas o seu valor.
Inu munagulitsa anthu anu pa mtengo wotsika, osapindulapo kanthu pa malondawo.
13 Tu nos pões como humilhação por nossos vizinhos; como escárnio e zombaria pelos que estão ao redor de nós.
Mwachititsa kuti tikhale chochititsa manyazi kwa anthu a mitundu ina, chonyozeka ndi chothetsa nzeru kwa iwo amene atizungulira.
14 Tu nos pões como provérbio de escárnio entre as nações; como balançar de cabeça entre os povos;
Mwachititsa kuti tikhale onyozeka pakati pa anthu a mitundu ina; anthu amapukusa mitu yawo akationa.
15 Minha humilhação está o dia todo diante de mim; e a vergonha cobre o meu rosto,
Manyazi anga ali pamaso panga tsiku lonse ndipo nkhope yanga yaphimbidwa ndi manyazi
16 Pela voz do adversário e do que insulta; por causa do inimigo e do vingador.
chifukwa cha mawu otonza a iwo amene amandinyoza ndi kundichita chipongwe, chifukwa cha mdani amene watsimikiza kubwezera.
17 Tudo isto veio sobre nós; porém não nos esquecemos de ti, nem traímos o teu pacto.
Zonsezi zinatichitikira ngakhale kuti ifeyo sitinayiwale Inu kapena kuonetsa kusakhulupirika pa pangano lanu.
18 Nosso coração não se voltou para trás, nem nossos passos de desviaram de teu caminho.
Mitima yathu sinabwerere mʼmbuyo; mapazi athu sanatayike pa njira yanu.
19 Tu tens nos afligido num lugar de chacais, e nos cobriste com sobra de morte.
Koma Inu mwatiphwanya ndi kuchititsa kuti tikhale ozunzidwa ndi ankhandwe ndipo mwatiphimba ndi mdima waukulu.
20 Se tivéssemos esquecido do nome do nosso Deus, e estendido nossas mãos a um outro deus,
Tikanayiwala dzina la Mulungu wathu kapena kutambasulira manja athu kwa mulungu wachilendo,
21 por acaso Deus não o descobriria? Pois ele conhece os segredos do coração.
kodi Mulungu wathu sakanazidziwa zimenezi, pakuti Iye amadziwa zinsinsi zamumtima?
22 Mas por causa de ti somos mortos o dia todo; somos considerados como ovelhas para o matadouro.
Komabe chifukwa cha Inu timakumana ndi imfa tsiku lonse, tili ngati nkhosa zoyenera kuti ziphedwe.
23 Desperta; por que estás dormindo, Senhor? Acorda, não [nos] rejeites para sempre.
Dzukani Ambuye! Nʼchifukwa chiyani mukugona! Dziwutseni nokha! Musatikane kwamuyaya.
24 Por que escondes tua face, e te esqueces de nossa humilhação e de nossa opressão?
Nʼchifukwa chiyani mukubisa nkhope yanu, ndi kuyiwala mavuto athu ndi kuponderezedwa kwathu?
25 Pois nossa alma está abatida ao pó; nosso ventre está junto à terra.
Tatsitsidwa pansi mpaka pa fumbi; matupi athu amatirira pa dothi.
26 Levanta-te para nosso socorro; e resgata-nos por tua bondade.
Imirirani ndi kutithandiza, tiwomboleni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.