< Salmos 20 >

1 Salmo de Davi, para o regente: Que o SENHOR te responda no dia da angústia; o nome do Deus de Jacó te ponha em lugar seguro.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Yehova akuyankhe pamene uli pa msautso; dzina la Mulungu wa Yakobo likuteteze.
2 Que ele envie a ti ajuda desde [seu] santuário; e desde Sião ele te sustenha.
Iye atumize thandizo kuchokera ku malo ake opatulika; akugwirizize kuchokera ku Ziyoni.
3 Que ele se lembre de todas as tuas ofertas, e aceite os teus holocaustos. (Selá)
Iye akumbukire nsembe zako zonse ndipo alandire nsembe zako zopsereza. (Sela)
4 Que ele de a ti conforme o teu coração, e faça cumprir todo o teu propósito.
Akupatse chokhumba cha mtima wako ndipo akuthandize kuti zonse wakonza zichitike.
5 Nós alegraremos muito por tua salvação, e no nome do nosso Deus levantaremos bandeiras; que o SENHOR cumpra todos os teus pedidos.
Ife tidzafuwula ndi chimwemwe pamene iwe wapambana ndipo tidzanyamula mbendera zathu mʼdzina la Mulungu wathu, Yehova ayankhe zopempha zako zonse.
6 Agora eu sei que o SENHOR salva a seu ungido; desde os céus de sua santidade ele lhe responderá, com o poder salvador de sua mão direita.
Tsopano ndadziwa kuti Yehova amapulumutsa wodzozedwa wake; Iye amamuyankha kuchokera kumwamba ku malo ake opatulika ndi mphamvu yopulumutsa ya dzanja lake lamanja.
7 Alguns confiam em carruagens, e outros em cavalos; mas nós nos lembraremos do nome do SENHOR nosso Deus.
Ena amadalira magaleta ndipo ena akavalo koma ife tidzadalira dzina la Yehova Mulungu wathu.
8 Eles se encurvam, e caem; mas nós nos levantamos, e ficamos em pé.
Iwo amagonjetsedwa ndi kugwa, koma ife timadzuka ndi kuyima chilili.
9 Salva [-nos], SENHOR! Que o Rei nos ouça no dia de nosso clamor.
Inu Yehova, pulumutsani mfumu! Tiyankheni pamene tikuyitanani!

< Salmos 20 >