< Salmos 139 >

1 Salmo de Davi, para o regente: SENHOR, tu me examinas e me conheces.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Inu Yehova, mwandisanthula ndipo mukundidziwa.
2 Tu sabes o meu sentar e o meu caminhar; de longe entendes meus pensamentos.
Inu mumadziwa pamene ndikhala pansi ndi pamene ndidzuka; mumazindikira maganizo anga muli kutali.
3 Tu cercas o meu andar e meu deitar; conheces desde antes os meus caminhos.
Mumapenyetsetsa pamene ndikutuluka ndi kugona kwanga; mumadziwa njira zanga zonse.
4 Mesmo não havendo [ainda] palavra [alguma] em minha língua, eis, SENHOR, que já sabes tudo.
Mawu asanatuluke pa lilime langa mumawadziwa bwinobwino, Inu Yehova.
5 Tu me envolves por detrás e pela frente, e pões tua mão sobre mim.
Mumandizinga kumbuyo ndi kutsogolo komwe; mwasanjika dzanja lanu pa ine.
6 [Teu] conhecimento é maravilhoso demais para mim, tão alto que não posso [alcançá] -lo.
Nzeru zimenezi ndi zopitirira nzeru zanga, ndi zapamwamba kuti ine ndizipeze.
7 Para onde eu escaparia de teu Espírito? E para onde fugiria de tua presença?
Kodi ndingapite kuti kufuna kuzemba Mzimu wanu? Kodi ndingathawire kuti kuchoka pamaso panu?
8 Se eu subisse até os céus, lá tu [estás]; se eu fizer meu leito no Xeol, eis que tu [também ali estás]. (Sheol h7585)
Ndikakwera kumwamba, Inu muli komweko; ndikakagona ku malo a anthu akufa, Inu muli komweko. (Sheol h7585)
9 Se eu tomasse as asas do amanhecer, e morasse nas extremidades do mar,
Ngati ndiwulukira kotulukira dzuwa, ngati ndikakhala ku malekezero a nyanja,
10 Até ali tua mão me guiaria, e tua mão direita me seguraria.
kumenekonso dzanja lanu lidzanditsogolera, dzanja lanu lamanja lidzandigwiriziza.
11 Se eu dissesse: Certamente as trevas me encobrirão; e a luz ao redor de mim [será como] a noite.
Ndikanena kuti, “Zoonadi, mdima udzandibisa ndithu ndipo kuwunika kukhale mdima mondizungulira,”
12 Porém nem mesmo as trevas [me] esconderão de ti; ao invés disso, [pois] a noite é tão clara quanto o dia, [e aos teus olhos] as trevas são como a luz.
komabe mdimawo sudzakhala mdima kwa Inu; usiku udzawala ngati masana, pakuti mdima uli ngati kuwunika kwa Inu.
13 Porque tu és dono do meu ser, e me cobriste no ventre da minha mãe.
Pakuti Inu munalenga za mʼkati mwanga; munandiwumba pamodzi mʼmimba mwa amayi anga.
14 Eu te louvarei porque de um [jeito] assombroso e maravilhoso eu fui feito; maravilhosas [são] tuas obras; e minha alma sabe muito bem.
Ndimakuyamikani chifukwa ndinapangidwa mochititsa mantha ndi modabwitsa; ntchito zanu ndi zodabwitsa, zimenezi ndimazidziwa bwino lomwe.
15 Meus ossos não estavam escondidos de ti quando eu fui feito em oculto, e formado como tramas de tecido nas profundezas da terra.
Mapangidwe anga sanabisike pamaso panu pamene ndimapangidwa mʼmalo achinsinsi, pamene ndinkawumbidwa mwaluso mʼmimba ya amayi anga.
16 Teus olhos viram meu corpo [ainda] sem forma, e tudo estava escrito em teu livro; [até] os dias estavam determinados quando nenhum deles [ainda] havia.
Maso anu anaona thupi langa lisanawumbidwe. Masiku onse amene anapatsidwa kwa ine, analembedwa mʼbuku lanu asanayambe nʼkuwerengedwa komwe.
17 Como são preciosos para mim os teus pensamentos, Deus! Como é grande a quantidade deles!
Zolingalira zanu pa ine ndi zamtengowapatali, Inu Mulungu, ndi zosawerengeka ndithu!
18 Se eu os contasse, seriam muito mais [numerosos] que a areia; [quando] acordo, ainda estou contigo.
Ndikanaziwerenga, zikanakhala zochuluka kuposa mchenga; pamene ndadzuka, ndili nanube.
19 Ah, Deus, tomara que mates ao perverso! E vós, homens sanguinários, afastai-vos de mim;
Ndi bwino mukanangopha anthu oyipa, Inu Mulungu! Chokereni inu anthu owononga anzanu!
20 Porque eles falam de ti com maldade, [e] teus inimigos [se] exaltam em vão.
Amayankhula za Inu ndi zolinga zoyipa; adani anu amagwiritsa ntchito dzina lanu molakwika.
21 Por acaso, SENHOR, eu não odiaria aos que te odeiam? E não detestaria os que se levantam contra ti?
Kodi ine sindidana nawo amene amakudani, Inu Yehova? Kodi sindinyansidwa nawo amene amakuwukirani?
22 Eu os odeio com ódio completo; eu os considero como inimigos.
Ndimadana nawo kwathunthu; ndi adani anga.
23 Examina-me, Deus, e conhece meu coração; prova-me, e conhece meus pensamentos.
Santhuleni, Inu Mulungu ndipo mudziwe mtima wanga; Yeseni ndipo mudziwe zolingalira zanga.
24 E vê se em mim [há algum] mau caminho; e guia-me pelo caminho eterno.
Onani ngati muli mayendedwe aliwonse oyipa mwa ine, ndipo munditsogolere mʼnjira yanu yamuyaya.

< Salmos 139 >