< Salmos 104 >

1 Louva, minha alma, ao SENHOR; ó SENHOR meu Deus, tu és grandioso; de majestade e de glória estás vestido.
Tamanda Yehova, iwe moyo wanga. Inu Yehova Mulungu wanga, ndinu wamkulu kwambiri; mwavala ulemerero ndi ufumu.
2 Tu estás coberto de luz, como que uma roupa; estendes os céus como cortinas.
Iye wadzifunditsa kuwala ngati chovala; watambasula miyamba ngati tenti
3 Ele, que fixou seus cômodos sobre as águas; que faz das nuvens sua carruagem; que se move sobre as asas do vento.
ndipo wayika pa madzi mitanda ya chipinda chake. Iye amasandutsa mitambo kukhala galeta lake, ndi kuwuluka pa mapiko a mphepo.
4 Que faz de seus anjos ventos, e de seus servos fogo flamejante.
Amapanga mphepo kukhala amithenga ake, malawi amoto kukhala atumiki ake.
5 Ele fundou a terra sobre suas bases; ela jamais se abalará.
Anakhazikitsa dziko lapansi pa maziko ake; silingasunthike.
6 Com o abismo, como um vestido, tu a cobriste; sobre os montes estavam as águas.
Munaliphimba ndi nyanja yozama ngati chovala; madzi anayimirira pamwamba pa mapiri.
7 Elas fugiram de tua repreensão; pela voz de teu trovão elas se recolheram apressadamente.
Koma pakudzudzula kwanu madzi anathawa, pa mkokomo wa bingu lanu iwo anamwazika;
8 Os montes subiram [e] os vales desceram ao lugar que tu lhes tinha fundado.
Inu munamiza mapiri, iwo anatsikira ku zigwa kumalo kumene munawakonzera.
9 Tu [lhes] puseste um limite, que não ultrapassarão; não voltarão mais a cobrir a terra.
Inu munayika malire ndipo sangathe kudutsa, iwo sadzamizanso dziko lapansi.
10 Ele envia fontes aos vales, para que corram por entre os montes.
Iye achititsa akasupe kutulutsa madzi kupita ku zigwa; madziwo amayenda pakati pa mapiri.
11 Elas dão de beber a todos os animais do campo; os asnos selvagens matam a sede [com elas].
Iwo amapereka madzi kwa zirombo zonse zakuthengo; abulu akuthengo amapha ludzu lawo.
12 Junto a elas habitam as aves dos céus, que dão [sua] voz dentre os ramos.
Mbalame zamlengalenga zimayika zisa mʼmbali mwa madzi; zimayimba pakati pa thambo.
13 Ele rega os montes desde seus cômodos; a terra se farta do fruto de tuas obras.
Iye amathirira mapiri kuchokera ku zipinda zake zapamwamba; dziko lapansi limakhutitsidwa ndi chipatso cha ntchito yake.
14 Ele faz brotar a erva para os animais, e as plantas para o trabalho do homem, fazendo da terra produzir o pão,
Amameretsa udzu kuti ngʼombe zidye, ndi zomera, kuti munthu azilima kubweretsa chakudya kuchokera mʼdziko lapansi:
15 E o vinho, que alegra o coração do homem, [e] faz o rosto brilhar o rosto com o azeite; com o pão, que fortalece o coração do homem.
vinyo amene amasangalatsa mtima wa munthu, mafuta amene amachititsa nkhope yake kuwala, ndi buledi amene amapereka mphamvu.
16 As árvores do SENHOR são fartamente [nutridas], os cedros do Líbano, que ele plantou.
Mitengo ya Yehova ndi yothiriridwa bwino, mikungudza ya ku Lebanoni imene Iye anadzala.
17 Onde as aves fazem ninhos, e os pinheiros são as casas para as cegonhas.
Mbalame zimamanga zisa zawo; kakowa ali ndi malo ake mʼmikungudzamo.
18 Os altos montes são para as cabras selvagens; as rochas, refúgio para os coelhos.
Mapiri ataliatali ndi a mbalale; mʼmingʼalu ya miyala ndi mobisalamo mbira.
19 Ele fez a lua para [marcar] os tempos, e o sol sobre seu poente.
Mwezi umasiyanitsa nyengo ndipo dzuwa limadziwa nthawi yake yolowera.
20 Ele dá ordens à escuridão, e faz haver noite, quando saem todos os animais do mato.
Inu mumabweretsa mdima nukhala usiku, ndipo zirombo zonse za ku nkhalango zimatuluka.
21 Os filhos dos leões, rugindo pela presa, e para buscar de Deus sua comida.
Mikango imabangula kufuna nyama, ndi kufunafuna chakudya chawo kuchokera kwa Mulungu.
22 Quando o sol volta a brilhar, [logo] se recolhem, e vão se deitar em suas tocas.
Dzuwa limatuluka ndipo iyo imapita kukabisala; imabwerera kukagona pansi mʼmapanga awo.
23 Então o homem sai para seu trabalho e sua obra até o entardecer.
Pamenepo munthu amapita ku ntchito yake, kukagwira ntchito yake mpaka madzulo.
24 Como são muitas as suas obras, SENHOR! Tu fizeste todas com sabedoria; a terra está cheia de teus bens.
Ntchito zanu ndi zochulukadi Inu Yehova! Munazipanga zonse mwanzeru, dziko lapansi ladzaza ndi zolengedwa zanu.
25 Este grande e vasto mar, nele há inúmeros seres, animais pequenos e grandes.
Kuli nyanja yayikulu ndi yotambalala, yodzaza ndi zolengedwa zosawerengeka, zamoyo zanu zazikulu ndi zazingʼono zomwe.
26 Por ali andam os navios e o Leviatã que formastes, para que te alegrasses nele.
Kumeneko sitima zapamadzi zimayenda uku ndi uku, ndiponso Leviyatani amene munamulenga kuti asewere kumeneko.
27 Todos eles aguardam por ti, que [lhes] dês seu alimento a seu tempo [devido].
Zonsezi zimayangʼana kwa Inu kuti muzipatse chakudya chawo pa nthawi yake yoyenera.
28 O que tu dás, eles recolhem; tu abres tua mão, [e] eles se fartam de coisas boas.
Mukazipatsa, zimachisonkhanitsa pamodzi; mukatsekula dzanja lanu, izo zimakhutitsidwa ndi zinthu zabwino.
29 [Quando] tu escondes teu rosto, eles ficam perturbados; [quando] tu tiras o fôlego deles, [logo] eles morrem, e voltam ao seu pó.
Mukabisa nkhope yanu, izo zimachita mantha aakulu; mukachotsa mpweya wawo, zimafa ndi kubwerera ku fumbi.
30 Tu envias o teu fôlego, e logo são criados; e [assim] tu renovas a face da terra.
Mukatumiza mzimu wanu, izo zimalengedwa ndipo mumakozanso maonekedwe a dziko lapansi.
31 A glória do SENHOR será para sempre; alegre-se o SENHOR em suas obras.
Ulemerero wa Yehova ukhalebe mpaka muyaya; Yehova akondwere ndi ntchito ya manja ake;
32 [Quando] ele olha para a terra, [logo] ela treme; [quando] ele toca nos montes, eles soltam fumaça.
Iye amene amayangʼana dziko lapansi ndipo limanjenjemera, amene amakhudza mapiri ndipo amatuluka utsi.
33 Cantarei ao SENHOR em [toda] a minha vida; tocarei música ao meu Deus enquanto eu existir.
Ine ndidzayimbira Yehova moyo wanga wonse; ndidzayimbira matamando Mulungu wanga nthawi yonse imene ndili ndi moyo.
34 Meus pensamentos lhe serão agradáveis; eu me alegrarei no SENHOR.
Zolingalira zanga zikhale zomukomera Iye, pamene ndikusangalala mwa Yehova.
35 Os pecadores serão consumidos da terra, e os maus não existirão mais. Bendizei, ó minha alma, ao SENHOR! Aleluia!
Koma anthu ochimwa awonongeke pa dziko lapansi ndipo anthu oyipa asapezekenso. Tamanda Yehova, Iwe moyo wanga. Tamandani Yehova.

< Salmos 104 >