< Provérbios 4 >
1 Ouvi, filhos, a correção do pai; e prestai atenção, para que conheçais o entendimento.
Ananu, mverani malangizo a abambo anu; tcherani khutu kuti mupeze nzeru zodziwira zinthu.
2 Pois eu vos dou boa doutrina; não deixeis a minha lei.
Zimene ndikukuphunzitsani ndi zabwino. Choncho musasiye malangizo anga.
3 Porque eu era filho do meu pai; tenro, e único perante a face de minha mãe.
Paja ndinalinso mwana mʼnyumba mwa abambo anga; mwana mmodzi yekha wapamtima pa amayi anga.
4 E ele me ensinava, e me dizia: Que teu coração retenha minhas palavras; guarda meus mandamentos, e vive.
Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti, “Ugwiritse mawu anga pa mtima pako, usunge malamulo anga kuti ukhale ndi moyo.
5 Adquire sabedoria, adquire entendimento; [e] não te esqueças nem te desvies das palavras de minha boca.
Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu; usayiwale mawu anga kapena kutayana nawo.
6 Não a abandones, e ela te guardará; ama-a, e ela te conservará.
Usasiye nzeru ndipo idzakusunga. Uziyikonda ndipo idzakuteteza.
7 O principal é a sabedoria; adquire sabedoria, e acima de tudo o que adquirires, adquire entendimento.
Fundo yayikulu pa za nzeru ndi iyi: upeze nzeru. Kaya pali china chilichonse chimene ungapeze, koma upeze nzeru yomvetsa bwino zinthu.
8 Exalta-a, e ela te exaltará; quando tu a abraçares, ela te honrará.
Uyilemekeze nzeruyo ndipo idzakukweza; ikumbatire nzeruyo ndipo idzakupatsa ulemu.
9 Ela dará a tua cabeça um ornamento gracioso; ela te entregará uma bela coroa.
Idzayika sangamutu yokongola yamaluwa pamutu pako; idzakupatsa chipewa chaufumu chaulemu.”
10 Ouve, filho meu, e recebe minhas palavras; e elas te acrescentarão anos de vida.
Mwana wanga, umvere ndi kuvomereza zimene ndikunena, ndipo zaka za moyo wako zidzakhala zochuluka.
11 Eu te ensino no caminho da sabedoria; [e] te faço andar pelos percursos direitos.
Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru. Ndakutsogolera mʼnjira zolungama.
12 Quando tu andares, teus passos não se estreitarão; e se tu correres, não tropeçarás.
Pamene ukuyenda, mapazi ako sadzawombana; ukamadzathamanga, sudzapunthwa.
13 Toma a correção para si, e não [a] largues; guarda-a, porque ela [é] tua vida.
Ugwiritse zimene ndikukuphunzitsazi osazitaya ayi. Uwasamale bwino pakuti moyo wako wagona pamenepa.
14 Não entres pela vereda dos perversos, nem andes pelo caminho dos maus.
Usayende mʼnjira za anthu oyipa kapena kuyenda mʼnjira ya anthu ochimwa.
15 Rejeita-o! Não passes por ele; desvia-te dele, e passa longe.
Pewa njira zawo, usayende mʼmenemo; uzilambalala nʼkumangopita.
16 Pois eles não dormem se não fizerem o mal; e ficam sem sono, se não fizerem tropeçar [a alguém].
Pakuti iwo sagona mpaka atachita zoyipa; tulo salipeza mpaka atapunthwitsa munthu wina.
17 Porque comem pão da maldade, e bebem vinho de violências.
Paja chakudya chawo ndicho kuchita zoyipa basi ndipo chakumwa chawo ndi chiwawa.
18 Mas o caminho dos justos é como a luz brilhante, que vai, e ilumina até o dia [ficar claro] por completo.
Koma njira ya anthu olungama ili ngati kuwala kwa mʼbandakucha kumene kumanka kuwalirawalira mpaka dzuwa litafika pa mutu.
19 O caminho dos perversos é como a escuridão; não sabem nem em que tropeçam.
Koma njira ya anthu oyipa ili ngati mdima wandiweyani; iwo sadziwa chomwe chimawapunthwitsa.
20 Filho meu, presta atenção às minhas palavras; e ouve as minhas instruções.
Mwana wanga, mvetsetsa zimene ndikunena; tchera khutu ku mawu anga.
21 Não as deixes ficarem longe de teus olhos; guarda-as no meio de teu coração.
Usayiwale malangizo angawa, koma uwasunge mu mtima mwako.
22 Porque são vida para aqueles que as encontram; e saúde para todo o seu corpo.
Pakuti amapatsa moyo kwa aliyense amene awapeza ndipo amachiritsa thupi lake lonse.
23 Acima de tudo o que se deve guardar, guarda o teu coração; porque dele [procedem] as saídas da vida.
Ndipotu mtima wako uziwuyangʼanira bwino ndithu pakuti ndiwo magwero a moyo.
24 Afasta de ti a perversidade da boca; e põe longe de ti a corrupção dos lábios.
Usiyiretu kuyankhula zokhotakhota; ndipo ulekeretu kuyankhula zinthu zonyansa.
25 Teus olhos olhem direito; tuas pálpebras estejam corretas diante de ti.
Maso ako ayangʼane patsogolo; uziyangʼana kutsogolo molunjika.
26 Pondera o curso de teus pés; e todos os teus caminhos sejam bem ordenados.
Uzilingalira bwino kumene kupita mapazi ako ndipo njira zako zonse zidzakhala zosakayikitsa.
27 Não te desvies nem para a direita, nem para a esquerda; afasta teus pés do mal.
Usapatukire kumanja kapena kumanzere; usapite kumene kuli zoyipa.