< Provérbios 31 >

1 Palavras do rei Lemuel, a profecia que sua mãe o ensinava.
Nawa mawu a mfumu Lemueli wa ku Massa amene anamuphunzitsa amayi ake:
2 O que [posso te dizer], meu filho, ó filho do meu ventre? O que [te direi], filho de minhas promessas?
Nʼchiyani mwana wanga? Nʼchiyani mwana wa mʼmimba mwanga? Nʼchiyani iwe mwana wanga amene ndinachita kupempha ndi malumbiro?
3 Não dês tua força às mulheres, nem teus caminhos para [coisas] que destroem reis.
Usapereke mphamvu yako kwa akazi. Usamayenda nawo amenewa popeza amawononga ngakhale mafumu.
4 Lemuel, não convém aos reis beber vinho; nem aos príncipes [desejar] bebida alcoólica.
Iwe Lemueli si choyenera kwa mafumu, mafumu sayenera kumwa vinyo. Olamulira asamalakalake chakumwa choledzeretsa
5 Para não acontecer de que bebam, e se esqueçam da lei, e pervertam o direito de todos os aflitos.
kuopa kuti akamwa adzayiwala malamulo a dziko, nayamba kukhotetsa zinthu zoyenera anthu osauka.
6 Dai bebida alcoólica aos que estão a ponto de morrer, e vinho que têm amargura na alma,
Perekani chakumwa choledzeretsa kwa amene ali pafupi kufa, vinyo kwa amene ali pa mavuto woopsa;
7 Para que bebam, e se esqueçam de sua pobreza, e não se lembrem mais de sua miséria.
amwe kuti ayiwale umphawi wawo asakumbukirenso kuvutika kwawo.
8 Abre tua boca no lugar do mudo pela causa judicial de todos os que estão morrendo.
Yankhula mʼmalo mwa amene sangathe kudziyankhulira okha. Uwayankhulire anthu onse osiyidwa pa zonse zowayenera.
9 Abre tua boca, julga corretamente, e faze justiça aos oprimidos e necessitados.
Yankhula ndi kuweruza mwachilungamo. Uwateteze amphawi ndi osauka.
10 Mulher virtuosa, quem a encontrará? Pois seu valor é muito maior que o de rubis.
Kodi mkazi wangwiro angathe kumupeza ndani? Ndi wokwera mtengo kuposa miyala yamtengowapatali.
11 O coração de seu marido confia nela, e ele não terá falta de bens.
Mtima wa mwamuna wake umamukhulupirira ndipo mwamunayo sasowa phindu.
12 Ela lhe faz bem, e não o mal, todos os dias de sua vida.
Masiku onse a moyo wake mkaziyo amachitira mwamuna wake zabwino zokhazokha osati zoyipa.
13 Ela busca lã e linho, e com prazer trabalha com suas mãos.
Iye amafunafuna ubweya ndi thonje; amagwira ntchito ndi manja ake mwaufulu.
14 Ela é como um navio mercante; de longe traz a sua comida.
Iye ali ngati sitima zapamadzi za anthu amalonda, amakatenga chakudya chake kutali.
15 Ainda de noite ela se levanta, e dá alimento a sua casa; e ordens às suas servas.
Iye amadzuka kusanache kwenikweni; ndi kuyamba kukonzera a pa banja pake chakudya ndi kuwagawira ntchito atsikana ake antchito.
16 Ela avalia um campo, e o compra; do fruto de suas mãos planta uma vinha.
Iye amalingalira za munda ndi kuwugula; ndi ndalama zimene wazipeza amalima munda wamphesa.
17 Ela prepara seus lombos com vigor, e fortalece seus braços.
Iye amavala zilimbe nagwira ntchito mwamphamvu ndi manja ake.
18 Ela prova que suas mercadorias são boas, [e] sua lâmpada não se apaga de noite.
Iye amaona kuti malonda ake ndi aphindu, choncho nyale yake sizima usiku wonse.
19 Ela estende suas mãos ao rolo de linha, e com suas mãos prepara os fios.
Iye amadzilukira thonje ndipo yekha amagwira chowombera nsalu.
20 Ela estende sua mão ao aflito, e estica os braços aos necessitados.
Iye amachitira chifundo anthu osauka ndipo amapereka chithandizo kwa anthu osowa.
21 Ela não terá medo da neve por sua casa, pois todos os de sua casa estão agasalhados.
Iye saopa kuti banja lake lifa ndi kuzizira pa nyengo yachisanu; pakuti onse amakhala atavala zovala zofunda.
22 Ela faz cobertas para sua cama; de linho fino e de púrpura é o seu vestido.
Iye amadzipangira yekha zoyala pa bedi pake; amavala zovala zabafuta ndi zapepo.
23 Seu marido é famoso às portas [da cidade], quando ele se senta com os anciãos da terra.
Mwamuna wake ndi wodziwika pa chipata cha mzinda, ndipo amakhala pakati pa akuluakulu a mʼdzikomo.
24 Ela faz panos de linho fino, e os vende; e fornece cintos aos comerciantes.
Iye amasoka nsalu zabafuta nazigulitsa; amaperekanso mipango kwa anthu amalonda.
25 Força e glória são suas roupas, e ela sorri pelo seu futuro.
Mphamvu ndi ulemu zimakhala ngati chovala chake; ndipo amaseka osaopa zamʼtsogolo.
26 Ela abre sua boca com sabedoria; e o ensinamento bondoso está em sua língua.
Iye amayankhula mwanzeru, amaphunzitsa anthu mwachikondi.
27 Ela presta atenção aos rumos de sua casa, e não come pão da preguiça.
Iye amayangʼanira makhalidwe a anthu a pa banja lake ndipo sachita ulesi ndi pangʼono pomwe.
28 Seus filhos se levantam e a chamam de bem-aventurada; seu marido também a elogia, [dizendo]:
Ana ake amamunyadira ndipo amamutcha kuti wodala; ndipo mwamuna wake, amamuyamikira nʼkumati,
29 Muitas mulheres agem com virtude, mas tu és melhor que todas elas.
“Pali akazi ambiri amene achita zinthu zopambana koma iwe umawaposa onsewa.”
30 A beleza é enganosa, e a formosura é passageira; [mas] a mulher que teme ao SENHOR, essa será louvada.
Nkhope yachikoka ndi yonyenga, ndipo kukongola nʼkosakhalitsa; koma mkazi amene amaopa Yehova ayenera kutamandidwa.
31 Dai a ela conforme o fruto de suas mãos, e que suas obras a louvem às portas [da cidade].
Mupatseni mphotho chifukwa cha zimene iye wachita ndipo ntchito zake zimutamande ku mabwalo.

< Provérbios 31 >