< 35 >

1 Eliú respondeu mais, dizendo:
Ndipo Elihu anawonjeza kunena kuti,
2 Pensas tu ser direito dizeres: Maior é a minha justiça do que a de Deus?
“Kodi mukuganiza kuti mukukhoza? Mukunena kuti, ‘Ndine wolungama pamaso pa Mulungu.’
3 Porque disseste: Para que ela te serve? [Ou]: Que proveito terei dela mais que meu pecado?
Komanso inu mukufunsa kuti, ‘Kodi phindu langa nʼchiyani, ndipo ndimapeza chiyani ndikapanda kuchimwa?’
4 Eu darei reposta a ti, e a teus amigos contigo.
“Ine ndikufuna ndikuyankheni inu pamodzi ndi abwenzi anu omwe.
5 Olha para os céus, e vê; e observa as nuvens, [que] são mais altas que tu.
Yangʼanani kumwamba ndipo muone mitambo imene ili kutali ndi inuyo.
6 Se tu pecares, que [mal] farás contra ele? Se tuas transgressões se multiplicarem, que [mal] lhe farás?
Inuyo mukachimwa, Iye zimamukhudza motani? Ngati machimo anu ndi ochuluka, zimenezo zimachita chiyani kwa Iye?
7 Se fores justo, que lhe darás? Ou o que ele receberá de tua mão?
Ngati inu ndinu wolungama, mumamupatsa Iyeyo chiyani? Kapena Iye amalandira chiyani chochokera mʼdzanja lanu?
8 Tua perversidade [poderia afetar] a outro homem como tu; e tua justiça [poderia ser proveitosa] a [algum] filho do homem.
Kuyipa kwanu kumangokhudza anthu ngati inuyo, ndipo chilungamo chanu chimakhudza anthu anzanu.
9 [Os aflitos] clamam por causa da grande opressão; eles gritam por causa do poder dos grandes.
“Anthu akufuwula chifukwa cha kuzunzidwa; akufuna chithandizo kuti achoke pansi pa ulamuliro wa anthu amphamvu.
10 Porém ninguém diz: Onde está Deus, meu Criador, que dá canções na noite,
Koma palibe amene akunena kuti, ‘Kodi ali kuti Mulungu, Mlengi wanga, amene amatisangalatsa nthawi ya usiku,
11 Que nos ensina mais que aos animais da terra, e nos faz sábios mais que as aves do céu?
amene amatiphunzitsa kupambana nyama za dziko lapansi ndipo amatipatsa nzeru kupambana mbalame zowuluka?’
12 Ali clamam, porém ele não responde, por causa da arrogância dos maus.
Iye sayankha pamene anthu akufuwulira kwa Iye chifukwa cha kudzikuza kwa anthu oyipa.
13 Certamente Deus não ouvirá a súplica vazia, nem o Todo-Poderoso dará atenção a ela.
Ndithu, Mulungu samva kupempha kwawo kopanda pake; Wamphamvuzonse sasamalira zimenezi.
14 Quanto menos ao que disseste: que tu não o vês! Porém o juízo está diante dele; portanto espera nele.
Ndipo ndi bodza lalikulu kunena kuti Iye saona zimene zikuchitika. Iye adzaweruza molungama ngati inu mutamudikira
15 Mas agora, já que a ira dele [ainda] não está castigando, e ele não deu completa atenção à arrogância,
ndiye tsono popeza kuti ukali wake sukupereka chilango, zoyipa zambiri zimene anthu amachita,
16 Por isso Jó abriu sua boca em vão, e multiplicou palavras sem conhecimento.
abambo Yobu mumangoyankhula zopandapake, mukungochulukitsa mawu opanda nzeru.”

< 35 >