< 19 >

1 Porém Jó respondeu dizendo:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 Até quando atormentareis minha alma, e me quebrantareis com palavras?
“Kodi mudzakhala mukundizunza mpaka liti, ndi kundilasa ndi mawu anuwo?
3 Já dez vezes me humilhastes; não tendes vergonha em me maltratar.
Inuyo mwandinyoza kwambiri; mwanditsutsa mopanda manyazi.
4 Mesmo se eu tiver errado, meu erro cabe apenas a mim.
Ngati ndi zoona kuti ine ndasochera, cholakwachotu nʼchanga.
5 Visto que vos exaltais contra mim, e contra mim usais minha desgraça,
Ngati ndithudi mukudziyika nokha pamwamba panga, ndi kugwiritsa ntchito kunyozedwa kwanga polimbana nane,
6 Sabei, pois, que foi Deus que me transtornou, e [com] sua rede me cercou.
pamenepa dziwani kuti Mulungu wandilakwira ndipo wandizinga ukonde wake.
7 Eis que eu clamo: Violência! Porém não sou respondido; grito, porém não há justiça.
“Ngakhale ndifuwule kuti, ‘Akundizunza!’ Palibe wondiyankha; ngakhale ndipemphe thandizo, palibe wondichitira zolungama.
8 Ele entrincheirou meu caminho, de modo que não consigo passar; e pôs trevas sobre minhas veredas.
Mulungu wanditsekera njira yanga kotero sindingathe kudutsa; waphimba njira zanga ndi mdima.
9 Ele me despojou de minha honra, e tirou a coroa de minha cabeça.
Iye wandilanda ulemu wanga ndipo wandivula chipewa chaufumu pamutu panga.
10 Ele me derrubou por todos os lados, e pereço; e arrancou minha esperança como a uma árvore.
Wandiphwanyaphwanya mbali zonse ndipo ndatheratu; Iye wazula chiyembekezo changa ngati mtengo.
11 E fez inflamar contra mim sua ira, e me considerou para consigo como a [um de] seus inimigos.
Wandikwiyira ndipo akundiyesa mmodzi mwa adani ake.
12 Juntas vieram suas tropas; prepararam contra mim seu caminho, e se acamparam ao redor de minha tenda.
Ankhondo ake akubwera kwa ine mwamphamvu, akonzekera zodzalimbana nane ndipo azungulira nyumba yanga.
13 Ele afastou meus irmãos para longe de mim; e os que me conheciam agora me estranham.
“Mulungu wandisiyanitsa ndi abale anga; wasandutsa odziwana nane kukhala achilendo kwa ine.
14 Meus parentes [me] deixaram, e meus conhecidos se esqueceram de mim.
Abale anga andithawa; abwenzi anga andiyiwala.
15 Os moradores de minha casa e minhas servas me tiveram por estranho; estrangeiro me tornei em seus olhos.
Anthu odzacheza ku nyumba kwanga ndiponso antchito anga aakazi andisandutsa mlendo; ndasanduka mlendo mʼmaso mwawo.
16 Chamei a meu servo, e ele não respondeu; de minha própria boca eu lhe suplicava.
Ndikayitana wa ntchito wanga, iye sandiyankha, ngakhale ndikapempha ndi pakamwa panga sandichitira kanthu.
17 Meu hálito é estranho à minha mulher, e sou repugnante aos filhos de minha mãe.
Mpweya wanga umamunyansa mkazi wanga; ndine chinthu chonyansa kwa abale anga a mimba imodzi.
18 Até os meninos me desprezam; quando eu me levanto, falam contra mim.
Inde, ngakhale ana amandinyoza; akandiona amandinyodola.
19 Todos os meus amigos próximos me abominam; e [até] aqueles que eu amava se viraram contra mim.
Anzanga onse apamtima amanyansidwa nane; iwo amene ndinkawakonda andiwukira.
20 Meus ossos se grudaram à minha pele e à minha carne; e escapei [só] com a pele de meus dentes.
Ndangotsala khungu ndi mafupa okhaokha; ndapulumuka lokumbakumba.
21 Compadecei-vos de mim, meus amigos, compadecei-vos de mim; pois a mão de Deus me tocou.
“Mvereni chisoni, inu abwenzi anga, mvereni chisoni, pakuti dzanja la Mulungu landikantha.
22 Por que vós me perseguis como Deus, e não vos fartais de minhas carne?
Chifukwa chiyani mukundilondola ngati Mulungu? Kodi simunatope nalo thupi langa?
23 Ah se minhas palavras fossem escritas! Ah se fossem escritas em um livro!
“Aa, achikhala mawu anga analembedwa, achikhala analembedwa mʼbuku,
24 Que com ponta de ferro e com chumbo fossem esculpidas em pedra para sempre!
akanalembedwa pa mwala ndi chitsulo, akanalembedwa pa thanthwe kuti sangathe kufufutidwa!
25 Pois eu sei que meu Redentor vive, e ao fim se levantará sobre a terra;
Koma ndikudziwa kuti mpulumutsi wanga ali ndi moyo, ndipo pa nthawi yomaliza adzabwera kudzanditeteza.
26 E mesmo depois de consumida minha pele, então em minha carne verei a Deus;
Ndipo khungu langa litatha nʼkuwonongeka, mʼthupi langa lomweli ndidzamuona Mulungu.
27 Ao qual eu verei para mim, e meus olhos [o] verão, e não outro. [Isto é o que] minhas entranhas anseiam dentro de mim.
Ine ndemwe ndidzamuona Iye ndi maso angawa, ineyo, osati wina ayi. Ndithu mtima wanga ukufunitsitsadi!
28 Se disserdes: Como o perseguiremos? Pois a raiz do problema se acha em mim,
“Koma inu mukuti, ‘Haa! Tingamuzunze bwanji, popeza kuti zonsezi zaoneka chifukwa cha iye yemweyo?’
29 Temei vós mesmos a espada; pois furor [há nos] castigos pela espada; para que [assim] saibais que [haverá] julgamento.
Inu muyenera kuopa lupanga; pakuti mkwiyo wake umalangadi ndi lupanga; zikadzatero muzadziwa kuti chiweruzo chilipo ndithu.”

< 19 >