< Jó 10 >
1 Minha alma está cansada de minha vida. Darei liberdade à minha queixa sobre mim; falarei com amargura de minha alma.
“Ine ndatopa nawo moyo wanga; choncho ndidzanena zodandaula zanga momasuka ndipo ndidzayankhula mwa kuwawidwa mtima kwanga.
2 Direi a Deus: Não me condenes; faz-me saber por que brigas comigo.
Ndidzati kwa Mulungu wanga: Musandiweruze kuti ndine wolakwa, koma mundiwuze chifukwa chimene Inu mukukanganira ndi ine.
3 [Parece] -te bem que [me] oprimas, que rejeites o trabalho de tuas mãos, e favoreças o conselho dos perversos?
Kodi mumakondwera mukamandizunza, kunyoza ntchito ya manja anu, chonsecho mukusekerera ndi zochita za anthu oyipa?
4 Tens tu olhos de carne? Vês tu como o ser humano vê?
Kodi maso anu ali ngati a munthu? Kodi mumaona zinthu monga momwe amazionera munthu?
5 São teus dias como os dias do ser humano, ou teus anos como os anos do homem,
Kodi masiku anu ali ngati masiku a munthu, kapena zaka zanu ngati zaka za munthu,
6 Para que investigues minha perversidade, e pesquises meu pecado?
kuti Inu mufufuze zolakwa zanga ndi kulondola tchimo langa,
7 Tu sabes que eu não sou mau; todavia ninguém há que [me] livre de tua mão.
ngakhale mukudziwa kuti sindine wolakwa ndiponso kuti palibe amene angandilanditse mʼdzanja lanu?
8 Tuas mãos me fizeram e me formaram por completo; porém agora tu me destróis.
“Munandiwumba ndi kundipanga ndi manja anu. Kodi tsopano Inu mudzatembenuka ndi kundiwononga?
9 Por favor, lembra-te que me preparaste como o barro; e me farás voltar ao pó da terra.
Kumbukirani kuti munandipanga ndi dothi, kodi tsopano mundibwezeranso ku fumbi?
10 Por acaso não me derramaste como o leite, e como o queijo me coalhaste?
Suja munapatsa abambo anga mphamvu zoti andibale, suja munandikuza bwino mʼmimba mwa amayi anga?
11 De pele e carne tu me vestiste; e de ossos e nervos tu me teceste.
Munandikuta ndi khungu ndi mnofu ndi kundilumikiza pamodzi ndi mafupa ndi mitsempha?
12 Vida e misericórdia me concedeste, e teu cuidado guardou meu espírito.
Munandipatsa moyo ndi kundionetsa chifundo chanu, ndipo munasamalira bwino moyo wanga.
13 Porém estas coisas escondeste em teu coração; eu sei que isto esteve contigo:
“Koma izi ndi zimene munabisa mu mtima mwanu, ndipo ndikudziwa kuti zinali mʼmaganizo anu:
14 Se eu pecar, tu me observarás, e não absolverás minha culpa.
Kuti ngati ndingachimwe mudzakhala mukundipenyetsetsa ndipo kuti simudzalola kuti ndisalangidwe chifukwa cha kulakwa kwanga.
15 Se eu for perverso, ai de mim! Mesmo se eu for justo, não levantarei minha cabeça; estou farto de desonra, e de ver minha aflição.
Ngati ndili wolakwa, tsoka langa! Koma ngakhale ndili wosalakwa sindingathe kutukula mutu wanga, pakuti ndagwidwa ndi manyazi ndipo ndamizidwa mʼmavuto anga.
16 Se [minha cabeça] se exaltar, tu me caças como um leão feroz, e voltas a fazer em coisas extraordinárias contra mim.
Ndipo ndikatukula mutu wanga, Inu mumandisaka ngati mkango ndiponso mumandiopseza ndi mphamvu yanu.
17 Renovas tuas testemunhas contra mim, e multiplicas tua ira sobre mim; combates vêm sucessivamente contra mim.
Mumabweretsa mboni zatsopano potsutsana nane ndipo mkwiyo wanu pa ine umanka nukulirakulira ndi magulu anu olimbana nane amanka nachulukirachulukira.
18 Por que me tiraste da madre? [Bom seria] se eu não tivesse respirado, e nenhum olho me visse!
“Chifukwa chiyani Inu munalola kuti ndibadwe? Ndi bwino ndikanafa diso lililonse lisanandione.
19 Teria sido como se nunca tivesse existido, e desde o ventre [materno] seria levado à sepultura.
Ndikanapanda kubadwa, kapena akanangonditenga nditabadwa kupita nane ku manda!
20 Por acaso não são poucos os meus dias? Cessa [pois] e deixa-me, para que eu tenha um pouco de alívio,
Kodi masiku anga owerengeka sali pafupi kutha? Ndilekeni kuti ndipumule pangʼono pokha
21 Antes que eu me vá para não voltar, à terra da escuridão e da sombra de morte;
ndisanapite ku malo amene munthu sabwererako ku dziko la imfa ndi kwa mdima wandiweyani,
22 Terra escura ao extremo, tenebrosa, sombra de morte, sem ordem alguma, onde a luz é como a escuridão.
ku dziko la mdima wandiweyani ndi chisokonezo, kumene kuwala kumakhala ngati mdima.”