< 1 Coríntios 13 >
1 Ainda que eu falasse as línguas dos seres humanos e dos anjos, e não tivesse amor, seria como o metal que soa, ou como o sino que retine.
Ngakhale nditamayankhula mʼmalilime a anthu ndi a angelo, koma ngati ndilibe chikondi, ndili ngati chinganga chaphokoso kapena ngati chitsulo chosokosera.
2 E ainda que tivesse [o dom] de profecia, e soubesse todos os mistérios, e todo o conhecimento; e ainda que tivesse toda a fé, de tal maneira que movesse os montes de lugar, e não tivesse amor, nada seria.
Ngati ndili ndi mphatso ya uneneri, nʼkumazindikira zinsinsi ndi kudziwa zonse, ndipo ngati ndili ndi chikhulupiriro chosuntha mapiri, koma wopanda chikondi, ine sindili kanthu.
3 E ainda que eu distribuísse todos os meus bens para alimentar [aos pobres], e ainda que entregasse meu corpo para ser queimado, e não tivesse amor, nada me aproveitaria.
Ngati ndipereka zanga zonse kwa osauka ndi kupereka thupi langa kuti alitenthe, koma ngati ndilibe chikondi, ine sindipindula kanthu.
4 O amor é paciente, é bondoso; o amor não é invejoso; o amor não é orgulhoso, não é arrogante.
Chikondi nʼcholeza mtima, chikondi nʼchokoma mtima, chilibe nsanje, sichidzikuza, sichidzitamandira.
5 O amor não trata mal; não busca os próprios [interesses], não se ira, não é rancoroso.
Chikondi chilibe mwano, sichodzikonda, sichipsa mtima msanga, sichisunga mangawa.
6 Não se alegra com a injustiça, mas se alegra com a verdade.
Chikondi sichikondwera ndi zoyipa koma chimakondwera ndi choonadi.
7 Tudo aguenta, tudo crê, tudo espera, tudo suporta.
Chimatchinjiriza nthawi zonse, chimakhulupirika nthawi zonse, chimakhala ndi chiyembekezo nthawi zonse, chimapirira nthawi zonse.
8 O amor nunca falha. Porém as profecias serão aniquiladas; as línguas acabarão, e o conhecimento será aniquilado.
Chikondi ndi chosatha. Koma mphatso ya uneneri idzatha, pamene pali kuyankhula malilime adzatha, pamene pali chidziwitso chidzatha.
9 Porque em parte conhecemos, e em parte profetizamos;
Pakuti timadziwa zinthu pangʼono chabe ndipo timanenera pangʼono chabe.
10 Mas quando vier o [que é] completo, [Ou: perfeito] então o que é em parte será aniquilado.
Koma changwiro chikadzaoneka ndipo chopereweracho chidzatha.
11 Quando eu era menino, falava como menino, sentia como menino, pensava como menino; mas quando me tornei homem, aniquilei as coisas de menino.
Pamene ndinali mwana ndinkayankhula ngati mwana, ndinkaganiza ngati mwana, ndinkalingalira ngati mwana. Koma nditakula, zonse zachibwana ndinazisiya.
12 Porque agora vemos por espelho em enigma, mas então [veremos] face a face; agora conheço em parte, mas então conhecerei assim como sou conhecido.
Pakuti tsopano tiona zinthu mosaoneka bwino ngati mʼgalasi loonera; kenaka tidzaziona maso ndi maso. Tsopano ndidziwa mosakwanira koma kenaka ndidzadziwa mokwanira, monga mmene Mulungu akundidziwira ine.
13 E agora continuam a fé, a esperança, [e] o amor, estes três; porém o maior destes é o amor.
Ndipo tsopano zatsala zinthu zitatu: chikhulupiriro, chiyembekezo ndi chikondi. Koma chachikulu pa zonsezi ndi chikondi.