< Provérbios 6 >

1 Filho meu, se ficaste por fiador do teu companheiro, se deste a tua mão ao estranho,
Mwana wanga, ngati wamuperekera mnansi wako chikole, ngati walonjeza kumulipirira mlendo,
2 Enredaste-te com as palavras da tua boca: prendeste-te com as palavras da tua boca.
ngati wagwidwa ndi zimene iwe unanena, wakodwa ndi mawu a mʼkamwa mwako.
3 Faze pois isto agora, filho meu, e livra-te, pois já caíste nas mãos do teu companheiro; vai, humilha-te, e aperta com o teu companheiro.
Tsono popeza iwe mwana wanga wadziponya mʼmanja mwa mnansi wako, chita izi kuti udzipulumutse: pita msanga ukamupemphe mnansi wako; kuti akumasule!
4 Não dês sono aos teus olhos, nem adormecimento às tuas pálpebras.
Usagone tulo, usawodzere.
5 Livra-te como o corço da mão do passarinheiro.
Dzipulumutse monga imachitira mphoyo mʼdzanja la mlenje, ndi monga imachitira mbalame mu msampha wa munthu wosaka.
6 Vai-te à formiga, ó preguiçoso: olha para os seus caminhos, e sê sábio.
Pita kwa nyerere, mlesi iwe; kaonetsetse njira zake kuti uphunzirepo kanthu!
7 A qual, não tendo superior, nem oficial, nem dominador,
Zilibe mfumu, zilibe woyangʼanira kapena wolamulira,
8 Prepara no verão o seu pão: na sega ajunta o seu mantimento.
komabe zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe ndipo zimatuta chakudyacho nthawi yokolola.
9 Oh! preguiçoso, até quando ficarás deitado? quando te levantarás do teu sono?
Kodi uzingogonabe pamenepo mpaka liti mlesi iwe? Kodi tulo tako tidzatha liti?
10 Um pouco de sono, um pouco tosquenejando; um pouco encruzando as mãos, para estar deitado.
Ukati ndingogona pangʼono, ndingowodzera pangʼono ndingopinda manjawa pangʼono kuti ndipumule,
11 Assim te sobrevirá a tua pobreza como o caminhante, e a tua necessidade como um homem armado.
umphawi udzakugwira ngati mbala ndipo usiwa udzafika ngati munthu wachifwamba.
12 O homem de Belial, o homem vicioso, anda em perversidade de boca.
Munthu wachabechabe, munthu woyipa, amangoyendayenda ndi kumayankhula zoyipa,
13 Acena com os olhos, fala com os pés, ensina com os dedos.
amatsinzinira maso ake, namakwakwaza mapazi ake ndi kulozaloza ndi zala zake,
14 Perversidade há no seu coração, todo o tempo maquina mal: anda semeando contendas.
amalingalira zoyipa ndi mtima wake wachinyengo ndipo nthawi zonse amangokhalira kuyambitsa mikangano pakati pa anthu.
15 Pelo que a sua destruição virá repentinamente: subitamente será quebrantado, sem que haja cura.
Nʼchifukwa chake tsoka lidzamugwera modzidzimutsa; adzawonongeka msangamsanga popanda chomupulumutsa.
16 Estas seis coisas aborrece o Senhor, e sete a sua alma abomina:
Pali zinthu zisanu ndi chimodzi zimene Yehova amadana nazo, zinthu zisanu ndi ziwiri zimene zimamunyansa:
17 Olhos altivos, língua mentirosa, e mãos que derramam sangue inocente:
maso onyada, pakamwa pabodza, manja akupha munthu wosalakwa,
18 O coração que maquina pensamentos viciosos; pés que se apressam a correr para o mal;
mtima wokonzekera kuchita zoyipa, mapazi othamangira msanga ku zoyipa,
19 A testemunha falsa que respira mentiras: e o que semeia contendas entre irmãos.
mboni yonama yoyankhula mabodza komanso munthu amene amayambitsa mikangano pakati pa abale.
20 Filho meu, guarda o mandamento de teu pai, e não deixes a lei de tua mãe;
Mwana wanga, usunge malamulo a abambo ako; ndipo usataye zimene anakuphunzitsa amayi ako.
21 Ata-os perpetuamente ao teu coração, e pendura-os ao teu pescoço.
Zimenezi uzimatirire pa mtima pako masiku onse, uzimangirire mʼkhosi mwako.
22 Quando caminhares, te guiará; quando te deitares, te guardará; quando acordares, ela falará contigo.
Ukamayenda, zidzakulozera njira; ukugona, zidzakulondera; ukudzuka, zidzakuyankhula.
23 Porque o mandamento é uma lâmpada, e a lei uma luz: e as repreensões da correção são o caminho da vida
Paja malamulo awa ali ngati nyale, malangizowa ali ngati kuwunika, ndipo chidzudzulo cha mwambo ndiwo moyo weniweni,
24 Para te guardarem da má mulher, e das lisonjas da língua estranha.
kukupulumutsa kwa mkazi wadama, zimenezi zidzakutchinjiriza kwa mkazi wadama, ndi kukuthandiza kuti usamvere mawu oshashalika a mkazi wachiwerewere.
25 Não cobices no teu coração a sua formosura, nem te prendas com os seus olhos.
Mu mtima wako usakhumbire kukongola kwake, asakukope ndi zikope zake,
26 Porque por causa de uma mulher prostituta se chega a pedir um bocado de pão; e a mulher dada a homens anda à caça da preciosa alma.
paja mkazi wadama amakusandutsa kukhala ngati nyenyeswa za buledi ndipo mkazi wa mwini wake amasokonezeratu moyo wako wonse.
27 Porventura tomará alguém fogo no seu seio, sem que os seus vestidos se queimem?
Kodi munthu angathe kutenga moto zovala zake osapsa?
28 Ou andará alguém sobre as brazas, sem que se queimem os seus pés?
Kodi munthu angathe kuyenda pa makala amoto mapazi ake osapserera?
29 Assim será o que entrar à mulher do seu próximo: não ficará inocente todo aquele que a tocar.
Ndizo zimachitikira munthu amene amagonana ndi mkazi wa munthu wina. Aliyense wokhudza mkazi wotere adzalangidwa.
30 Não injuriam ao ladrão, quando furta, para saciar a sua alma, tendo fome;
Paja anthu sayinyoza mbala ikaba chifukwa chakuti ili ndi njala.
31 Mas, achado, pagará sete vezes tanto: dará toda a fazenda de sua casa.
Komabe ngati mbalayo igwidwa iyenera kulipira kasanu nʼkawiri, ngakhale kulandidwa katundu wa mʼnyumba mwake.
32 Porém o que adultera com uma mulher é falto de entendimento; destrói a sua alma, o que tal faz.
Munthu wochita chigololo ndi wopanda nzeru. Wochita zimenezi amangodziwononga yekha.
33 Achará castigo e vilipêndio, e o seu opróbrio nunca se apagará.
Adzalandira mabala ndi mʼnyozo, ndipo manyazi ake sadzamuchokera.
34 Porque ciúmes são furores do marido, e de maneira nenhuma perdoará no dia da vingança.
Paja nsanje imachititsa mwini mkaziyo kukalipa, ndipo sadzachita chifundo pobwezera.
35 Nenhum resgate aceitará, nem consentirá, ainda que aumentes os presentes.
Iye savomera dipo lililonse; sangapepeseke ngakhale umupatse mphatso zochuluka motani.

< Provérbios 6 >