< Provérbios 18 >
1 Busca coisas desejáveis aquele que se separa e se entremete em toda a sabedoria.
Munthu wokonda kukhala yekha amafunafuna zomukomera yekha; iye amatsutsana ndi malangizo onse anzeru.
2 Não toma prazer o tolo na inteligência, senão em que se descubra o seu coração.
Chitsiru chilibe chidwi chomvetsa zinthu, koma chimakondwera ndi kuyankhula maganizo ake okha.
3 Vindo o ímpio, vem também o desprezo, e com a vergonha a ignomínia.
Kuyipa mtima kukabwera, manyozonso amabwera. Manyazi amabwera pamodzi ndi kunyozeka.
4 águas profundas são as palavras da boca do homem, e ribeiro trasbordante é a fonte da sabedoria.
Mawu a munthu ali ngati madzi akuya, kasupe wa nzeru ndiye mtsinje wotumphuka.
5 Não é bom ter respeito à pessoa do ímpio para derribar o justo em juízo.
Si kwabwino kukondera munthu woyipa pa milandu; kapena kupondereza munthu wosalakwa.
6 Os beiços do tolo entram na contenda, e a sua boca por acoites brada.
Mawu a chitsiru amautsa mkangano; pakamwa pake pamayitana mkwapulo.
7 A boca do tolo é a sua própria destruição, e os seus lábios um laço para a sua alma.
Pakamwa pa chitsiru ndipo pamabweretsa chiwonongeko chake, ndipo milomo yake ili ngati msampha wa moyo wake.
8 As palavras do assoprador são como doces bocados; e elas descem ao intimo do ventre.
Mawu a miseche ali ngati chakudya chokoma; amalowa mʼmimba mwa munthu.
9 Também o negligente na sua obra é irmão do desperdiçador.
Munthu waulesi pa ntchito yake ali pachibale ndi munthu amene amawononga zinthu.
10 Torre forte é o nome do Senhor; a ele correrá o justo, e estará em alto retiro.
Dzina la Yehova lili ngati nsanja yolimba; wolungama amathawiramo napulumuka.
11 A fazenda do rico é a cidade da sua fortaleza, e como um muro alto na sua imaginação.
Chuma cha anthu olemera chili ngati mzinda wake wolimba; chili ngati khoma lalitali limene amaganiza kuti limutchinjiriza.
12 Antes de ser quebrantado eleva-se o coração do homem; e diante da honra vai a humildade.
Chiwonongeko chisanafike, mtima wa munthu umakhala wonyada, koma ulemu umatsatira kudzichepetsa.
13 O que responde antes de ouvir, estultícia lhe é, e vergonha.
Ukayankha usanamvetse bwino nkhani, umenewo ndi uchitsiru ndipo umachita manyazi.
14 O espírito do homem sosterá a sua enfermidade, mas ao espírito abatido quem levantará?
Mtima wa munthu utha kupirira pa matenda, koma munthu akataya mtima ndani angathe kumulimbitsanso.
15 O coração do entendido adquire o conhecimento, e o ouvido dos sábios busca o conhecimento.
Munthu wanzeru amawonjezera nzeru zina; amafunafuna kudziwa bwino zinthu.
16 O presente do homem lhe alarga o caminho e o leva diante dos grandes.
Mphatso ya munthu imamutsekulira njira yomufikitsa pamaso pa anthu akuluakulu.
17 O que primeiro começa o seu pleito justo é; porém vem o seu companheiro, e o examina.
Amene amayamba kufotokoza mlandu wake amaoneka ngati wolungama ndiye mpaka mnzake atabwera ndi kumufunsa bwino.
18 A sorte faz cessar os pleitos, e faz separação entre os poderosos.
Kuchita maere kumathetsa mikangano; amalekanitsa okangana amphamvu.
19 O irmão ofendido é mais difícil de conquistar do que uma cidade forte; e as contendas são como os ferrolhos dum palácio.
Mʼbale amene wamuthandiza amakhala ngati mzinda wolimba, koma kukangana naye kumatsekereza thandizo.
20 Do fruto da boca de cada um se fartará o seu ventre: dos renovos dos seus lábios se fartará.
Munthu amapeza bwino malingana ndi zoyankhula zake. Adzakhuta ndi zipatso za pakamwa pake.
21 A morte e a vida estão no poder da língua; e aquele que a ama comerá do seu fruto.
Mawu ako angathe kukuphetsa kapena kukukhalitsa moyo. Wokonda kuyankhulayankhula adzadya zipatso zake.
22 O que acha mulher acha o bem e alcança a benevolência do Senhor.
Wapeza mkazi wapeza chinthu chabwino ndipo Yehova amamukomera mtima.
23 O pobre fala com rogos, mas o rico responde com durezas.
Munthu wosauka amapempha koma munthu wolemera amayankha mwaukali.
24 O homem que tem amigos haja-se amigavelmente, e há amigo mais chegado do que um irmão.
Pali abwenzi amene chibwenzi chawo nʼchapamaso, koma pali bwenzi limene limakukangamira kuposa mʼbale wako.