< Números 28 >

1 Falou mais o Senhor a Moisés, dizendo:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Dá ordem aos filhos de Israel, e dize-lhes: Da minha oferta, do meu manjar para as minhas ofertas queimadas, do meu cheiro suave, tereis cuidado, para mas oferecer ao seu tempo determinado.
“Lamula Aisraeli kuti, ‘Onetsetsani kuti mukupereka kwa Ine pa nthawi yoyikika, chopereka cha chakudya chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Ine.’
3 E dir-lhes-ás: Esta é a oferta queimada que oferecereis ao Senhor: dois cordeiros dum ano, sem mancha, cada dia, em contínuo holocausto:
Awuze kuti, ‘Nsembe ya chakudya imene muzipereka pa moto kwa Yehova tsiku ndi tsiku ndi iyi: Ana ankhosa a chaka chimodzi awiri, wopanda chilema.
4 Um cordeiro sacrificarás pela manhã, e o outro cordeiro sacrificarás de tarde:
Mmawa muzipereka mwana wankhosa mmodzi ndipo winayo madzulo.
5 E a décima parte dum epha de flor de farinha em oferta de manjares, misturada com a quarta parte dum hin de azeite moído.
Muziperekanso kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi lita imodzi ya mafuta a olivi.
6 Este é o holocausto contínuo, instituído no monte Sinai, em cheiro suave, oferta queimada ao Senhor.
Iyi ndi nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku imene analamula pa phiri la Sinai kuti ikhale fungo lokoma, nsembe yopsereza pa moto yopereka kwa Yehova.
7 E a sua libação será a quarta parte dum hin para um cordeiro: no santuário oferecerás a libação de bebida forte ao Senhor.
Chopereka chachakumwa chikhale lita imodzi yachakumwa chaukali pa nkhosa iliyonse. Muzithira pamalo opatulika, kupereka kwa Yehova.
8 E o outro cordeiro sacrificarás de tarde, como a oferta de manjares da manhã, e como a sua libação o aparelharás em oferta queimada de cheiro suave ao Senhor.
Muzipereka mwana wankhosa winayo madzulo, pamodzi ndi chopereka chachakudya monga poyamba paja ndi chopereka chachakumwa monga mmawa. Ichi ndi chopereka chachakudya, fungo lokoma kwa Yehova.’”
9 Porém no dia de sábado dois cordeiros dum ano, sem mancha, e duas dácimas de flor de farinha, misturada com azeite, em oferta de manjares, com a sua libação.
“‘Pa tsiku la Sabata, muzipereka nsembe ana ankhosa awiri a chaka chimodzi wopanda chilema, pamodzi ndi chopereka chachakumwa ndi chopereka chachakudya chokwana makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta.
10 Holocausto é do sábado em cada sábado, além do holocausto contínuo, e a sua libação.
Iyi ndi nsembe yopsereza ya pa Sabata iliyonse, kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake chachakumwa.’”
11 E nos princípios dos vossos meses oferecereis, em holocausto ao Senhor, dois bezerros e um carneiro, sete cordeiros dum ano, sem mancha;
“Pa tsiku loyamba la mwezi uliwonse muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi, ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, onse wopanda chilema.
12 E três dácimas de flor de farinha misturada com azeite, em oferta de manjares, para um bezerro; e duas dácimas de flor de farinha misturada com azeite, em oferta de manjares, para um carneiro.
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; ndi nkhosa yayimuna, chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta;
13 E uma décima de flor de farinha misturada com azeite, em oferta de manjares, para um cordeiro: holocausto é de cheiro suave, oferta queimada ao Senhor.
ndipo pa mwana wankhosa aliyense, chopereka cha ufa wa kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, izi ndi za nsembe yopsereza, fungo lokoma, nsembe yotentha pa moto ya kwa Yehova.
14 E as suas libações serão a metade dum hin de vinho para um bezerro, e a terça parte dum hin para um carneiro, e a quarta parte dum hin para um cordeiro: este é o holocausto da lua nova de cada mes, segundo os meses do ano
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakumwa cha malita awiri a vinyo; ndipo pa nkhosa yayimuna, lita limodzi ndi theka, ndipo pa mwana wankhosa, lita limodzi. Iyi ndi nsembe yopsereza ya mwezi ndi mwezi yoperekedwa pa mwezi watsopano mʼkati mwa chaka.
15 Também um bode para expiação do pecado ao Senhor, além do holocausto contínuo, com a sua libação se oferecerá.
Powonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake cha chakumwa, mbuzi yayimuna imodzi iperekedwe kwa Yehova ngati nsembe yopepesera machimo.
16 Porém no mês primeiro, aos quatorze dias do mes, é a pascoa do Senhor.
“‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita Paska wa Yehova.
17 E aos quinze dias do mesmo mês haverá festa: sete dias se comerão pães asmos.
Pa tsiku la 15 la mwezi womwewo pazikhala chikondwerero. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri.
18 No primeiro dia haverá santa convocação: nenhuma obra servil fareis:
Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
19 Mas oferecereis oferta queimada em holocausto ao Senhor, dois bezerros e um carneiro, e sete cordeiros dum ano: servos-ão eles sem mancha.
Koma muzipereka kwa Yehova nsembe yotentha pa moto, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri aamuna a chaka chimodzi, onsewo wopanda chilema.
20 E a sua oferta de manjares será de flor de farinha misturada com azeite: oferecereis três dácimas para um bezerro, e duas dácimas para um carneiro.
Pamodzi ndi ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; makilogalamu awiri pa nkhosa yayimuna iliyonse.
21 Para cada cordeiro oferecereis uma décima, para cada um dos sete cordeiros;
Kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa asanu ndi awiri aja.
22 E um bode para expiação do pecado, para fazer expiação por vós
Muziphatikizapo mbuzi yayimuna monga nsembe yopepesera machimo anu.
23 Estas coisas oferecereis, além do holocausto da manhã, que é o holocausto contínuo.
Muzikonza zimenezi nthawi zonse, powonjezera pa nsembe yopsereza ya mmawa.
24 Segundo este modo, cada dia oferecereis por sete dias o manjar da oferta queimada em cheiro suave ao Senhor: além do holocausto contínuo se oferecerá com a sua libação.
Motere muzikonza chakudya cha nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pa masiku asanu ndi awiri ngati fungo lokomera Yehova. Zimenezi ziziperekedwa kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse pamodzi ndi nsembe yachakumwa.
25 E no sétimo dia tereis santa convocação: nenhuma obra servil fareis.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
26 Semelhantemente, tereis santa convocação no dia das primícias, quando oferecerdes oferta nova de manjares ao Senhor, segundo as vossas semanas; nenhuma obra servil fareis.
“‘Pa tsiku la zipatso zoyambirira kucha, pamene mukupereka chopereka cha chakudya chatsopano kwa Yehova, pa nthawi ya chikondwerero cha Masabata, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa.
27 Então oferecereis ao Senhor por holocausto, em cheiro suave, dois bezerros, um carneiro e sete cordeiros dum ano:
Muzipereka nsembe zopsereza za ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa imodzi yayimuna ndi ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi monga fungo lokomera Yehova.
28 E a sua oferta de manjares de flor de farinha misturada com azeite: três dácimas para um bezerro, duas dácimas para um carneiro;
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pazikhala chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri.
29 Para cada cordeiro uma décima, para cada um dos sete cordeiros;
Ndipo pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja, kilogalamu imodzi.
30 Um bode para fazer expiação por vós.
Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
31 Além do holocausto contínuo, e a sua oferta de manjares, os oferecereis (ser-vos-ão eles sem mancha) com as suas libações.
Muzipereka zimenezi pamodzi ndi zopereka za zakumwa ndi nsembe yake ya chakudya. Onetsetsani kuti nyamazo zilibe chilema.

< Números 28 >