< 41 >

1 Poderás tirar com anzol o leviathan? ou ligarás a sua língua com a corda?
“Kodi ungathe kukoka ngʼona ndi mbedza ya nsomba kapena kukanikiza lilime lake pansi ndi chingwe?
2 Podes pôr um junco no seu nariz? ou com um espinho furarás a sua queixada?
Kodi ungathe kumanga chingwe mʼmphuno mwake, kapena kubowola nsagwada zake ndi mbedza?
3 Porventura multiplicará muitas suplicações para contigo? ou brandamente falará?
Kodi ngʼonayo idzakupempha kuti uyichitire chifundo? Kodi idzakuyankhula ndi mawu ofatsa?
4 Fará ele concertos contigo? ou o tomarás tu por escravo para sempre?
Kodi idzachita nawe mgwirizano kuti uyisandutse kapolo wako mpaka muyaya?
5 Brincarás com ele, como com um passarinho? ou o atarás para tuas meninas?
Kodi udzasewera nayo ngati mbalame, kapena kuyimangirira kuti atsikana ako asewere nayo?
6 Os teus companheiros farão dele um banquete? ou o repartirão entre os negociantes?
Kodi anthu adzayitsatsa malonda? Nanga amalondawo nʼkugawanagawana nyama yake kuti akagulitse?
7 Encherás a sua pele de ganchos? ou a sua cabeça com arpéos de pescadores?
Kodi chikopa chake ungathe kuchilasa ndi zisonga, kapena kubowola mutu wake ndi nthungo zophera nsomba?
8 Põe a tua mão sobre ele, lembra-te da peleja, e nunca mais tal intentarás.
Ukayiputa udziwe kuti pali nkhondo, ndipo iweyo sudzabwereranso.
9 Eis que a sua esperança falhará: porventura também à sua vista será derribado?
Chiyembekezo choti nʼkuyigonjetsa ndi chabodza; kungoyiona kokha, ndithu iwe kumangodzigwera wekha.
10 Ninguém há tão atrevido, que a desperta-lo se atreva: quem pois é aquele que ousa pôr-se em pé diante de mim
Palibe wolimba mtima kuti ndi kuyiputa. Ndani angalimbe mtima kulimbana ndi Ine?
11 Quem me preveniu, para que eu haja de retribuir-lhe? pois o que está debaixo de todos os céus é meu.
Kodi ndani anandipatsa kanthu kuti ndimubwezere? Zonse za pansi pa thambo ndi zanga.
12 Não calarei os meus membros, nem a relação das suas forças, nem a graça da sua formação.
“Sindidzaleka kuyankhula za ziwalo zake za chirombocho, za mphamvu zake ndiponso za maonekedwe a thupi lake.
13 Quem descobriria a superfície do seu vestido? quem entrará entre as suas queixadas dobradas?
Ndani angasende chikopa chake? Ndani angayiyandikire kuti abowole chikopa chake cholimbacho?
14 Quem abriria as portas do seu rosto? pois em roda dos seus dentes está o terror.
Ndani angatsekule kukamwa kwake, pakamwa pamene pazunguliridwa ndi mano ochititsa mantha?
15 As suas fortes escamas são excelentíssimas, cada uma fechada como com selo apertado.
Kumsana kwake kuli mizere ya mamba onga zishango zolumikizanalumikizana;
16 Uma à outra se chega tão perto, que nem um assopro passa por entre elas.
Mambawo ndi olukanalukana kotero kuti mpweya sungathe kulowa pakati pake.
17 Umas às outras se apegam: tanto se travam entre si, que não se podem separar.
Ndi olumikizanalumikizana; ndi omatirirana kwambiri kotero kuti sangathe kulekana.
18 Cada um dos seus espirros faz resplandecer a luz, e os seus olhos são como as pestanas da alva.
Kuyetsemula kwake kumatulutsa mbaliwali; maso ake amawala ngati kuwala kwa mʼbandakucha.
19 Da sua boca saem tochas: faiscas de fogo arrebentam dela.
Mʼkamwa mwake mumatuluka nsakali zamoto ndipo mumathetheka mbaliwali zamoto.
20 Dos seus narizes procede fumo, como de uma panela fervente, ou de uma grande caldeira.
Mʼmphuno mwake mumatuluka utsi ngati wa mʼnkhali yowira yomwe ili pa moto wa bango.
21 O seu hálito faria incender os carvões: e da sua boca sai chama.
Mpweya wake umayatsa makala, ndipo malawi amoto amatuluka mʼkamwa mwake.
22 No seu pescoço pousa a força: perante ele até a tristeza salta de prazer.
Mphamvu zake zili mʼkhosi mwake; aliyense wokumana nayo amangoti njenjenje ndi mantha.
23 Os músculos da sua carne estão pegados entre si: cada um está firme nele, e nenhum se move.
Minyewa ya thupi lake ndi yolumikizana ndipo ndi yokhwima kwambiri ndi yolimba.
24 O seu coração é firme como uma pedra e firme como parte da mó de baixo.
Pachifuwa pake ndi powuma ngati mwala, ndi pa gwaa, ngati mwala wamphero.
25 Levantando-se ele, tremem os valentes: em razão dos seus abalos se purificam.
Ngʼonayo ikangovuwuka, ndi anthu amphamvu omwe amaopa; amabwerera mʼmbuyo, kuthawa.
26 Se alguém lhe tocar com a espada, essa não poderá penetrar, nem lança, dardo ou couraça.
Ngakhale ikanthidwe ndi lupanga, lupangalo silichita kanthu, ngakhale mkondo, muvi ndi nthungo, zonse zimalephera.
27 Ele reputa o ferro por palha, e o cobre por pau podre.
Chitsulo imachiyesa ngati phesi chabe ndi mkuwa ngati chikuni chowola.
28 A seta o não fará fugir: as pedras das fundas se lhe tornam em rastolho.
Muvi sungathe kuyithawitsa, miyala imene ayilasa nayo imangoyinyenyanyenya.
29 As pedras atiradas estima como arestas, e ri-se do brandir da lança.
Zibonga zimakhala ngati ziputu; imangoseka pamene akuyibaya ndi nthungo.
30 Debaixo de si tem conchas ponteagudas: estende-se sobre coisas ponteagudas como na lama.
Mamba a ku mimba kwake ali ngati chopunthira chakunthwa ndipo imasiya mkukuluzi mʼmatope ngati galeta lopunthira tirigu.
31 As profundezas faz ferver, como uma panela: torna o mar como quando os unguentos fervem.
Imagadutsa madzi ozama ngati madzi a mʼnkhali, imachititsa nyanja kuti iwire ngati mbiya yoyengera mafuta.
32 Após ele alumia o caminho: parece o abismo tornado em brancura de cãs.
Kumbuyo kwake imasiya nthubwitubwi zambee, kotero kuti munthu angaganize kuti nyanja yachita imvi.
33 Na terra não há coisa que se lhe possa comparar, pois foi feito para estar sem pavor.
Pa dziko lapansi palibe china chofanana nacho, nʼcholengedwa chopanda mantha.
34 Todo o alto vê: é rei sobre todos os filhos de animais altivos.
Chimanyoza nyama zina zonse; icho chija ndi mfumu ya nyama zonse.”

< 41 >