< Jó 33 >
1 Assim, na verdade, ó Job, ouve as minhas razões, e dá ouvidos a todas as minhas palavras.
“Koma tsopano, inu abambo Yobu chonde mverani mawu anga; mutcherere khutu zonse zimene ndinene.
2 Eis que já abri a minha boca: já falou a minha língua debaixo do meu paladar.
Tsopano ndiyamba kuyankhula; mawu anga ali pa msonga ya lilime langa.
3 As minhas razões sairão da sinceridade do meu coração, e a pura ciência dos meus lábios.
Mawu anga akuchokera mu mtima wolungama; pakamwa panga pakuyankhula zoonadi zimene ndikuzidziwa.
4 O espírito de Deus me fez: e a inspiração do Todo-poderoso me deu vida.
Mzimu wa Mulungu wandiwumba, mpweya wa Wamphamvuzonse umandipatsa moyo.
5 Se podes responde-me, põe por ordem diante de mim a tua causa, e levanta-te.
Mundiyankhe ngati mungathe; konzekani tsopano kuti munditsutse.
6 Eis que sou de Deus, como tu: do lodo também eu fui cortado.
Ine ndili monga inu pamaso pa Mulungu; nanenso ndinachokera ku dothi.
7 Eis que não te perturbará o meu terror, nem será pesada sobre ti a minha mão.
Musachite mantha ndipo musandiope ayi, Ine sindikupanikizani kwambiri ayi.
8 Na verdade que disseste aos meus ouvidos; e eu ouvi a voz das palavras, dizendo:
“Koma inu mwayankhula ine ndikumva, ndamva mawu anuwo onena kuti,
9 Limpo estou, sem transgressão: puro sou; e não tenho culpa.
‘Ndine wolungama mtima ndi wopanda tchimo; ndine woyera mtima ndipo ndilibe cholakwa.
10 Eis que acha contra mim achaques, e me considerou como seu inimigo.
Komatu Mulungu wapeza zifukwa zoti anditsutsire nazo; Iye akundiyesa ngati mdani wake.
11 Põe no tronco os meus pés, e observa todas as minhas veredas.
Iyeyo wamanga mapazi anga mʼzigologolo, akulonda mayendedwe anga onse.’
12 Eis que nisto te respondo: Não foste justo; porque maior é Deus do que o homem.
“Koma ine ndi kuti kwa inu, inuyo simukukhoza pa zimenezi, pakuti Mulungu ndi wamkulu kupambana munthu.
13 Por que razão contendeste com ele? porque não responde acerca de todos os seus feitos.
Chifukwa chiyani mukudandaula kwa Iye kuti sayankha mawu ena aliwonse a munthu?
14 Antes Deus fala uma e duas vezes; porém ninguém atenta para isso.
Pajatu Mulungu amayankhula mwa njira zosiyanasiyana, ngakhale munthu sazindikira zimenezi.
15 Em sonho ou em visão de noite, quando cai sono profundo sobre os homens, e adormecem na cama,
Mʼmaloto, mʼmasomphenya usiku, pamene anthu ali mʼtulo tofa nato pamene akungosinza chabe pa bedi,
16 Então o revela ao ouvido dos homens, e lhes sela a sua instrução.
amawanongʼoneza mʼmakutu ndi kuwaopseza ndi machenjezo ake,
17 Para apartar o homem daquilo que faz, e esconder do homem a soberba.
kumuchotsa munthu ku zoyipa, ndi kuthetseratu kunyada kwake,
18 Para desviar a sua alma da cova, e a sua vida de passar pela espada.
kumulanditsa munthu ku manda, kuti moyo wake usawonongeke ndi lupanga.
19 Também na sua cama é com dores castigado; como também a multidão de seus ossos com fortes dores.
“Mwina Mulungu amalanga munthu ndi matenda ndi ululu ali pa bedi pake, nthawiyo thupi lake lonse limangophwanya,
20 De modo que a sua vida abomina até o pão, e a sua alma a comida apetecível.
kuti asakhalenso ndi chilakolako cha chakudya, ndipo amanyansidwa ndi chakudya chabwino chomwe.
21 Desaparece a sua carne à vista de olhos, e os seus ossos, que se não viam, agora aparecem:
Thupi lake limawonda ndipo mafupa ake, omwe anali obisika, tsopano amaonekera poyera.
22 E a sua alma se vai chegando à cova, e a sua vida ao que traz morte.
Munthuyo amayandikira ku manda, moyo wake umayandikira kwa amene amabweretsa imfa.
23 Se com ele pois houver um mensageiro, um intérprete, um entre milhares, para declarar ao homem a sua retidão,
“Koma patakhala mngelo ngati mthandizi, mmodzi mwa ambirimbiri oterewa, adzafotokoza zimene zili zoyenera,
24 Então terá misericórdia dele, e lhe dirá: Livra-o, que não desça à cova; já achei resgate.
kudzamukomera mtima ndi kunena kuti, ‘Mupulumutseni kuti asapite ku manda; ine ndapeza cholowa mʼmalo mwa moyo wake,’
25 Sua carne se reverdecerá mais do que era na mocidade, e tornará aos dias da sua juventude.
pamenepo thupi lake lidzasanduka lasee ngati la mwana; ndipo adzabwezeretsedwanso kukhala ngati mʼmasiku a unyamata wake.
26 Deveras orará a Deus, o qual se agradará dele, e verá a sua face com júbilo, e restituirá ao homem a sua justiça.
Akapemphera kwa Mulungu, iyeyo adzalandiridwa. Mulungu adzamulandira mwa chimwemwe ndipo adzamubwezeretsa pamalo ake oyamba.
27 Olhará para os homens, e dirá: Pequei, e perverti o direito, o que de nada me aproveitou.
Ndipo adzabwera kwa anzake ndi kunena kuti, ‘Ndinachimwa ndipo sindinachite zolungama, koma sindinalangidwe koyenerana ndi kuchimwa kwanga.
28 Porém Deus livrou a minha alma de que não passasse a cova; assim que a minha vida vê a luz.
Iye anapulumutsa moyo wanga kuti usapite ku manda, ndipo ndidzakhala ndi moyo ndi kuonanso kuwala kwa dzuwa.’
29 Eis que tudo isto obra Deus, duas e três vezes para com o homem;
“Mulungu amachita zonsezi kwa munthu kawirikawiri,
30 Para desviar a sua alma da perdição, e o alumiar com a luz dos viventes.
kupulumutsa moyo wa munthuyo ku manda, kuti athe kuonanso kuwala kwa moyo.
31 Escuta pois, ó Job, ouve-me: cala-te, e eu falarei.
“Abambo Yobu, tcherani khutu ndipo mundimvere; khalani chete kuti ndiyankhule.
32 Se tens alguma coisa que dizer, responde-me: fala, porque desejo justificar-te.
Ngati muli nʼchoti munene, ndiyankheni; yankhulani, pakuti ine ndikufuna mupezeke wolungama.
33 Se não, escuta-me tu: cala-te, e ensinar-te-ei a sabedoria.
Koma ngati sichoncho, mundimvere; khalani chete ndipo ine ndidzakuphunzitsani nzeru.”