< Isaías 8 >
1 Disse-me também o Senhor: Toma um grande volume, e escreve nele em estilo de homem: Apressando-se ao despojo, apressurou-se à preza.
Yehova anati kwa ine, “Tenga cholembapo chachikulu ndipo ulembepo malemba odziwika bwino: Kusakaza-Kwamsanga Kufunkha-Kofulumira.
2 Então tomei comigo fieis testemunhas, a Urias sacerdote, e a Zacarias, filho de Jeberechias,
Ndipo ndidzayitana wansembe Uriya ndi Zekariya mwana wa Yeberekiya kuti akhale mboni zanga zodalirika.”
3 E cheguei-me à profetiza, a qual concebeu, e pariu um filho; e o Senhor me disse: Chama o seu nome Maher-shalal-hash-baz.
Ndipo ine ndinapita kwa mneneri wamkazi, ndipo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna. Ndipo Yehova anati kwa ine, “Umutche dzina lakuti, ‘Kusakaza-Kwamsanga Kufunkha-Kofulumira.’
4 Porque antes que o menino saiba chamar pai meu, ou mãe minha, se levarão as riquezas de Damasco, e os despojos de Samaria, diante do rei da Assyria.
Mwanayo asanayambe kudziwa kuyitana kuti, ‘Ababa’ kapena ‘Amama’ chuma cha Damasiko ndi zofunkha za Samariya zidzatengedwa ndi mfumu ya ku Asiriya.”
5 E continuou o Senhor a falar ainda comigo, dizendo:
Yehova anayankhulanso ndi Ine;
6 Porquanto este povo desprezou as águas de Siloé que correm brandamente, e com Resin e com o filho de Remalias se alegrou:
“Popeza anthu a dziko ili akana madzi anga oyenda mwachifatse a ku Siloamu, ndipo akukondwerera Rezini ndi mwana wa Remaliya,
7 Portanto eis que o Senhor fará subir sobre eles as águas do rio, fortes e impetuosas, ao rei da Assyria, com toda a sua glória, e subirá acima sobre todos os seus leitos, e trasbordará por todas as suas ribanceiras.
nʼchifukwa chake Ambuye ali pafupi kubweretsa madzi amkokomo a mtsinje wa Yufurate kudzalimbana nawo; mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lake lonse lankhondo. Madziwo adzasefukira mʼngalande zake zonse ndi mʼmagombe ake onse.
8 E passará a Judá, inundando-a, e irá passando por ele e chegará até ao pescoço: e a extensão de suas asas encherá a largura da tua terra, ó Emanuel.
Ndipo adzalowa mwamphamvu mʼdziko la Yuda, adzasefukira, adzapitirira mpaka kumuyesa mʼkhosi. Mapiko ake otambasuka adzaphimba dziko lako lonse, iwe Imanueli!”
9 Ajuntai-vos em companhia, ó povos, e quebrantai-vos; e dai ouvidos, todos os que sois de longes terras, cingi-vos e sede feitos em pedaços, cingi-vos e sede feitos em pedaços.
Chitani phokoso lankhondo, inu mitundu ya anthu, ndipo munjenjemere! Tamverani, inu mayiko onse akutali. Konzekerani nkhondo ndipo munjenjemere! Konzekerani nkhondo ndipo munjenjemere!
10 Tomai juntamente conselho, e será dissipado: dizei a palavra, porém não subsistirá, porque Deus é conosco.
Konzani kachitidwe kanu kankhondo, koma simudzaphula kanthu, kambiranani zochita, koma zidzalephereka, pakuti Mulungu ali nafe.
11 Porque assim me disse o Senhor com mão forte, e me ensinou que não andasse pelo caminho deste povo, dizendo:
Yehova anandiyankhula ine mwamphamvu, ndipo anandichenjeza kuti ndisamayende mʼnjira za anthuwa. Iye anati:
12 Não chameis conjuração, a tudo quanto este povo chama conjuração: e não temais o seu temor, nem tão pouco vos assombreis.
“Usamanene kuti ndi chiwembu, chilichonse chimene anthuwa amati ndi chiwembu usamaope zimene anthuwa amaziopa, ndipo usamachite nazo mantha.
13 Ao Senhor dos exércitos, a ele santificai: e seja ele o vosso temor e seja ele o vosso assombro.
Yehova Wamphamvuzonse ndiye amene uyenera kumuona kuti ndi woyera, ndiye amene uyenera kumuopa, ndiye amene uyenera kuchita naye mantha,
14 Então ele vos será por santuário, mas por pedra de escândalo, e por penha de tropeço, às duas casas de Israel, por laço e rede aos moradores de Jerusalém.
ndipo ndiye amene adzakhala malo opatulika; koma kwa anthu a ku Yuda ndi kwa anthu a ku Israeli adzakhala mwala wopunthwitsa, mwala umene umapunthwitsa anthu, thanthwe limene limagwetsa anthu. Ndipo kwa anthu a mu Yerusalemu adzakhala ngati msampha ndi khwekhwe.
15 E muitos tropeçarão entre eles, e cairão, e serão quebrantados, e enlaçados, e presos.
Anthu ambiri adzapunthwapo adzagwa ndi kuthyokathyoka, adzakodwa ndi kugwidwa.”
16 Liga o testemunho, sela a lei entre os meus discípulos.
Manga umboniwu ndipo umate malamulowa pamaso pa ophunzira anga.
17 E esperarei ao Senhor, que esconde o seu rosto da casa de Jacob, e a ele aguardarei.
Ndidzayembekezera Yehova, amene akubisira nkhope yake nyumba ya Yakobo. Ine ndidzakhulupirira Iyeyo.
18 Eis-me aqui e os filhos que me deu o Senhor, por sinais e por maravilhas em Israel, da parte do Senhor dos exércitos, que habita no monte de Sião.
Onani, ine ndili pano pamodzi ndi ana amene Yehova wandipatsa, ndife zizindikiro ndi zodabwitsa kwa Aisraeli zochokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, amene amakhala pa Phiri la Ziyoni.
19 Quando pois vos disserem: consultai os adivinhos e os encantadores, e que, chilrando entre dentes, murmuram: Porventura não perguntará o povo a seu Deus? ou perguntar-se-á pelos vivos aos mortos?
Anthu akakuwuza kuti kafunsire kwa oyankhula ndi mizimu, amene amayankhula monongʼona ndi mongʼungʼudza, kodi anthu sayenera kukafunsira kwa Mulungu wawo? Chifukwa chiyani amafunsira kwa anthu akufa mʼmalo mwa kwa anthu amoyo,
20 Á Lei e ao Testemunho, que se eles não falarem segundo esta palavra, nunca verão a alva.
kuti akalandireko mawu enieni ndi malangizo? Ngati anthuwo sayankhula monga mwa mawu awa, mwa iwo mulibe kuwala.
21 E passarão pela terra duramente oprimidos e famintos: e será que, tendo fome, e enfurecendo-se, então amaldiçoarão ao seu rei e ao seu Deus, olhando para cima
Anthu adzayendayenda mʼdziko movutika kwambiri ali ndi njala; pamene afowokeratu ndi njala, iwo adzakwiya kwambiri ndipo adzayangʼana kumwamba ndi kutemberera mfumu yawo ndi Mulungu wawo.
22 E, olhando para a terra, eis que haverá angústia e escuridão, e serão entenebrecidos com ancia, e empuxados com escuridão.
Ndipo akadzayangʼana pa dziko lapansi adzangoona mavuto okhaokha ndi mdima woopsa ndi wodetsa nkhawa, ndipo adzaponyedwa mu mdima wandiweyani.