< Isaías 35 >

1 O deserto e os lugares secos se alegrarão disto; e o ermo exultará e florescerá como a rosa.
Chipululu ndi dziko lopanda madzi zidzasangalala; dziko lowuma lidzakondwa ndi kuchita maluwa.
2 Abundantemente florescerá, e também se alegrará de alegria e exultará; a glória do líbano se lhe deu, o ornato do Carmelo e Saron: eles verão a glória do Senhor, o ornato do nosso Deus.
Dzikolo lidzakhala ndi maluwa ochuluka lidzasangalala kwambiri ndi kufuwula mwachimwemwe. Lidzakhala ndi ulemerero monga wa ku mapiri a ku Lebanoni, maonekedwe ake wokongola adzakhala ngati a ku Karimeli ndi a ku Saroni. Aliyense adzaona ulemerero wa Yehova, ukulu wa Mulungu wathu.
3 Confortai as mãos fracas, e esforçai os joelhos trementes.
Limbitsani manja ofowoka, limbitsani mawondo agwedegwede;
4 Dizei aos turbados de coração: confortai-vos, não temais: eis que o vosso Deus virá a tomar vingança, com pagos de Deus; ele virá, e vos salvará.
nenani kwa a mitima yamantha kuti; “Limbani mtima, musachite mantha; Mulungu wanu akubwera, akubwera kudzalipsira; ndi kudzabwezera chilango adani anu; akubwera kudzakupulumutsani.”
5 Então os olhos dos cegos serão abertos, e os ouvidos dos surdos se abrirão.
Pamenepo maso a anthu osaona adzapenyanso ndipo makutu a anthu osamva adzatsekuka.
6 Então os coxos saltarão como cervos, e a língua dos mudos cantará: porque águas arrebentarão no deserto e ribeiros no ermo.
Anthu olumala adzalumpha ngati mbawala, ndipo osayankhula adzayimba mokondwera. Akasupe adzatumphuka mʼchipululu ndipo mitsinje idzayenda mʼdziko lowuma,
7 E a terra seca se tornará em tanques, e a terra sedenta em mananciais de águas; e nas habitações em que jaziam os dragões haverá erva com canas e juncos.
mchenga wotentha udzasanduka dziwe, nthaka yowuma idzasanduka ya akasupe. Pamene panali mbuto ya ankhandwe padzamera udzu ndi bango.
8 E ali haverá estrada e caminho, que se chamará o caminho Santo; o imundo não passará por ele, mas será para estes: os caminhantes, até mesmo os loucos, não errarão.
Ndipo kumeneko kudzakhala msewu waukulu; ndipo udzatchedwa Msewu Wopatulika. Anthu odetsedwa sadzayendamo mʼmenemo; zitsiru sizidzasochera mʼmenemo.
9 Ali não haverá leão, nem besta fera subirá a ele, nem se achará nele: porém só os remidos andarão por ele.
Kumeneko sikudzakhala mkango, ngakhale nyama yolusa sidzafikako; sidzapezeka konse kumeneko. Koma okhawo amene Yehova anawapulumutsa adzayenda mu msewu umenewu.
10 E os resgatados do Senhor tornarão, e virão a Sião com júbilo: e alegria eterna haverá sobre as suas cabeças: gozo e alegria alcançarão, e deles fugirá a tristeza e o gemido.
Iwo amene Yehova anawawombola adzabwerera. Adzalowa mu mzinda wa Ziyoni akuyimba; kumeneko adzakondwa mpaka muyaya. Adzakutidwa ndi chisangalalo ndi chimwemwe, ndipo chisoni ndi kudandaula zidzatheratu.

< Isaías 35 >