< Ezequiel 40 >
1 No ano vinte e cinco do nosso cativeiro, no princípio do ano, no décimo dia do mes, quatorze anos depois que a cidade foi ferida, naquele mesmo dia veio sobre mim a mão do Senhor, e me levou para lá.
Kumayambiriro a chaka cha 25, cha ukapolo wathu, tsiku la khumi lamwezi, patapita zaka khumi ndi zinayi mzinda wa Yerusalemu utawonongedwa, pa tsiku lomwelo dzanja la Yehova linali pa ine ndipo Iye anapita nane ku Yerusalemu.
2 Em visões de Deus me levou à terra de Israel, e me pôs sobre um monte mui alto, e havia sobre ele como edifício de cidade para a banda do sul.
Mʼmasomphenyawo Yehova ananditenga ndi kupita nane ku dziko la Israeli ndipo anandiyika pa phiri lalitali kwambiri, moti ndinaona ngati mzinda.
3 E, havendo-me levado ali, eis que um homem cujo parecer era como o parecer de cobre tinha um cordel de linho na sua mão e uma cana de medir; e ele estava em pé na porta.
Atandifikitsa kumeneko ndinaona munthu wonyezimira ngati mkuwa. Iye anali atayima pa chipata ndipo mʼdzanja lake munali chingwe cha nsalu yabafuta ndi ndodo yoyezera.
4 E disse-me o homem: Filho do homem, vê com os teus olhos, e ouve com os teus ouvidos, e põe no teu coração tudo quanto eu te fizer vêr; porque afim de to mostrar foste tu aqui trazido: anuncia pois à casa de Israel tudo quanto tu vires
Munthuyo anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, penyetsetsa ndipo umvetse bwinobwino. Uyikepo mtima wako pa zonse zimene ndikukuonetsa pakuti anakubweretsa kuno kuti uwone zimenezi. Tsono ukawawuze Aisraeli zonse zimene uzione.”
5 E eis um muro fora da casa em redor, e na mão do homem uma cana de medir, de seis côvados, cada côvado dum côvado e um palmo, e mediu a largura do edifício, de uma cana, e a altura, de uma cana.
Ine ndinaona khoma litazungulira mbali zonse za Nyumba ya Mulungu. Mʼdzanja la munthuyo munali bango lopimira limene kutalika kwake kunali kwa mamita atatu. Atayeza chipupacho anapeza kuti kuchindikira kwake kunali mamita atatu, ndiponso kutalika kwake kunalinso mamita atatu.
6 Então veio à porta que olhava para o caminho do oriente, e subiu pelos seus degraus; mediu o umbral da porta, uma cana de largo, e o outro umbral, de uma cana de largo.
Anapita ku chipata chakummawa. Anakwera pa makwerero a nyumbayo, nayeza chiwundo choyamba cha chipatacho; kutalika kwake kunali mamita atatu.
7 E cada camarinha era uma cana de comprido, e outra cana de largo, e entre as camarinhas havia cinco côvados; e o umbral da porta, ao pé do vestíbulo da porta, era de uma cana, por dentro.
Kudutsa chiwundo choyambachi, panali zipinda za alonda zisanu ndi chimodzi, zitatu kudzanja lamanja, zitatu kudzanja lamanzere. Chilichonse chinali cha mamita atatu mulitali mwake, chimodzimodzinso mulifupi mwake. Mipata ya pakati pa zipindazo inali ya mamita awiri ndi theka. Ndipo chiwundo cha pa chipata pafupi ndi khonde lapachipata, chinali mamita atatu.
8 Também mediu o vestíbulo da porta por dentro, de uma cana.
Ndipo iye anayeza khonde la chipata ndipo chinali cha mamita atatu.
9 Então mediu o outro alpendre da porta, de oito côvados, e os seus pilares, de dois côvados, e o vestíbulo da porta, por dentro.
Anayeza khonde ndipo linali mamita anayi. Mphuthu zake zinali mita imodzi kuchindikira kwake. Khonde lamʼkati lapachipata linali kumapeto kwenikweni pafupi ndi Nyumba ya Mulungu.
10 E as camarinhas da porta do caminho para o oriente eram três desta e três da outra banda, uma mesma medida era a das três: também os pilares desta e da outra banda tinham a mesma medida.
Mʼkati mwa chipata chakummawa munali zipinda za alonda zitatu mbali iliyonse. Zitatu zonsezo zinali zofanana, ndipo khonde la pakati pa zipindazo linali lofanana.
11 Mediu mais a largura da entrada da porta, de dez côvados; e o comprimento da porta, treze côvados.
Kenaka anayeza chipata cholowera; mulifupi mwake munali mamita asanu ndipo mulitali mwake munali mamita asanu ndi limodzi ndi theka.
12 E o espaço de diante das camarinhas era de um côvado, e de um côvado o espaço da outra banda: e cada camarinha tinha seis côvados de uma e seis côvados da outra banda.
Kutsogolo kwa chipinda chilichonse cha alonda kunali khoma lalifupi lotalika theka la mita, ndipo mbali iliyonse ya zipinda za alondazo inali yotalika mamita atatu.
13 Então mediu a porta desde o telhado de uma camarinha até ao telhado da outra, vinte e cinco côvados de largo, porta contra porta.
Ndipo anayeza kutalika kwa mulifupi mwa chipata cholowera, kuchokera ku khoma lakumbuyo la chipinda chimodzi mpaka ku khoma la chipinda china; kuchokera ku chitseko mpaka ku chitseko china. Kutalika kwake kunali mamita khumi ndi awiri ndi theka.
14 Também fez pilares de sessenta côvados, a saber, para o pilar do átrio, em roda da porta.
Anayezanso khonde lamʼkati ndipo linali la mamita makumi atatu. Ndipo mozungulira khondelo munali bwalo. Muyesowu sukuphatikiza khonde loyangʼanana ndi bwalo.
15 E, desde a dianteira da porta da entrada até à dianteira do vestíbulo da porta interior, havia cincoênta côvados.
Kuchokera pa chipata cholowera mpaka ku mapeto a khonde la chipata, kutalika kwake kunali mamita 27.
16 Fez também janelas de fechar nas camarinhas, e nos seus pilares, dentro da porta ao redor, e da mesma sorte nos vestíbulos: e as janelas estavam à roda pela parte de dentro, e nos pilares havia palmas.
Makoma a zipinda ndiponso makoma a pakati pa zipindazo anali ndi mazenera. Khonde lamʼkati linalinso ndi mazenera mʼkati mwake. Pa makoma onsewo anajambulapo zithunzi za kanjedza.
17 E ele me levou ao átrio exterior; e eis que havia nele câmaras, e um solhado que estava feito no átrio em redor: trinta câmaras havia naquele solhado.
Kenaka munthuyo anandilowetsa mʼbwalo lakunja, ndipo ndinaona zipinda zina ndi msewu wa miyala wozungulira bwalo lonse. Zipinda zonse zinali makumi atatu ndipo zinkayangʼana msewuwo.
18 E o solhado da banda das portas era a par do comprimento das portas: o solhado estava debaixo.
Utali wa mulifupi mwa msewuwo unkayenda mamita 27 kufanana ndi utali wa chipata cholowera. Uwu unali msewu wa mʼmunsi.
19 E mediu a largura da dianteira do átrio interior, por fora, cem côvados, da banda do oriente e do norte.
Tsono, anayeza kutalika kwa bwalo kuyambira chipata cholowera choyamba mpaka polowera pa chipata chakunja cha bwalo la mʼkati. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.
20 E, quanto à porta que olhava para o caminho do norte, no átrio exterior, ele mediu o seu comprimento e a sua largura.
Kenaka munthuyo anayeza mulitali ndi mulifupi mwa chipata chimene chimayangʼana kumpoto, chotulukira kunja.
21 E as suas camarinhas, três de uma banda, e três da outra, e os seus pilares e os seus vestíbulos eram da medida da primeira porta: cincoênta côvados era o seu comprimento, e a largura vinte e cinco côvados.
Zipinda za alonda zimene zinalipo zitatu mbali iliyonse, makoma ake ndi khonde zinali ndi muyeso wofanana ndi wachipata choyamba chija. Kutalika kwake kunali mamita 27 ndipo mulifupi mwake munali mamita 13.
22 E as suas janelas, e os seus vestíbulos, e as suas palmas, eram da medida da porta que olhava para o caminho do oriente; e subiam a ela por sete degraus, e os seus vestíbulos estavam diante delas.
Mipata yake, khonde lake ndi zojambula za kanjedza zinali ndi miyeso yofanana ndi za chipata chakummawa. Chipatacho chinali ndi makwerero asanu ndi awiri ndipo kotsirizira kwa chipatacho kunali khonde.
23 E estava a porta do átrio interior defronte da porta do norte e do oriente; e mediu de porta a porta cem côvados.
Panalinso chipata cholowera ku bwalo lamʼkati chofanana ndi chakummawa chimene chimayangʼanana ndi chipata chakumpoto, chofanana ndi cha mbali ya kummawa. Anachiyeza kuchokera ku chipata china mpaka ku chipata china. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.
24 Então ele me levou ao caminho do sul, e eis uma porta que olhava para o caminho do sul, e mediu os seus pilares e os seus vestíbulos conforme estas medidas.
Ndipo munthuyo anapita nane ku mbali yakummwera ndipo ndinaona chipata chakummwera. Iye anayeza mphuthu zake ndi khonde ndipo zinali ndi miyeso yofanana ndi ya zina zija.
25 E tinha também janelas em redor dos seus vestíbulos, como estas janelas: cincoênta côvados o comprimento, e a largura vinte e cinco côvados.
Mʼzipinda za chipata cholowera chimenechi ndi mʼkhonde lake munali mipata yofanana ndi ya mʼzipinda zina. Mulitali mwake munali mamita 27, mulifupi mwake munali mamita 13.
26 E de sete degraus eram as suas subidas, e os seus vestíbulos diante delas; e tinha umas palmas, uma de uma banda e outra da outra banda, nos seus pilares.
Chipatacho chinali ndi makwerero asanu ndi awiri ndi khonde kotsirizira kwake. Chipindacho chinali ndi zojambula za kanjedza ku mbali zonse za makoma.
27 Também havia uma porta no átrio interior para o caminho do sul; e mediu de porta a porta, para o caminho do sul, cem côvados.
Bwalo lamʼkati linalinso ndi chipata kummwera. Munthuyo analiyeza kuchokera ku chipata chimenechi mpaka ku chipata chakunja. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.
28 Então me levou ao átrio interior pela porta do sul; e mediu a porta do sul, conforme estas medidas.
Ndipo munthu uja anandilowetsa mʼbwalo lamʼkati kudzera ku chipata chakummwera. Anayeza chipatachi ndipo chinali chofanana ndi zinzake zija.
29 E as suas camarinhas, e os seus pilares, e os seus vestíbulos eram conforme estas medidas; e tinham também janelas ao redor dos seus vestíbulos: o comprimento era de cincoênta côvados, e a largura de vinte e cinco côvados.
Zipinda zake za alonda, makoma ake ndi khonde lake zinali zofanana ndi zina zija. Chipata cholowera ndi khonde lake zinali ndi mipata mʼmbali zonse. Mulitali mwake munali mamita 27 ndipo mulifupi munali mamita 13.
30 E havia vestíbulos em redor: o comprimento era de vinte e cinco côvados, e a largura de cinco côvados.
(Khonde lililonse la makonde atatu a zipata zolowera bwalo lamʼkati aja linali la mamita ozungulira mʼbwalo lamʼkati anali mamita 13 mulitali mwake, mamita awiri ndi theka mulifupi mwake).
31 E os seus vestíbulos estavam no átrio exterior, e tinham palmas nos seus pilares; e de oito degraus eram as suas subidas.
Khonde lake linayangʼanana ndi bwalo lakunja. Pa mphuthu pake anajambulapo zithunzi za kanjedza mbali zonse ziwiri, ndipo linali ndi makwerero asanu ndi atatu.
32 Depois me levou ao átrio interior, para o caminho do oriente, e mediu a porta conforme estas medidas;
Kenaka munthuyo anapita nane ku bwalo la mʼkati mbali ya kummawa, ndipo anayeza chipata cholowera; chinali chofanana ndi zinzake zina zija.
33 Como também as suas camarinhas, e os seus pilares, e os seus vestíbulos, conforme estas medidas; e tinha também janelas em redor dos seus vestíbulos: o comprimento de cincoênta côvados, e a largura de vinte e cinco côvados.
Zipinda zake za alonda, makoma ake ndi khonde lake zinali zofanana ndi zina zija. Chipata cholowera ndi khonde lake chinali ndi mipata mʼmbali zonse. Mulitali mwake munali mamita 27 ndipo mulifupi mwake munali mamita 13.
34 E os seus vestíbulos estavam no átrio de fora: também havia palmas nos seus pilares de uma e de outra banda; e eram as suas subidas de oito degraus.
Khonde lake linayangʼanana ndi bwalo lakunja. Pa mphuthu pake anajambulapo zithunzi za kanjedza mbali zonse ziwiri, ndipo linali ndi makwerero asanu ndi atatu.
35 Então me levou à porta do norte, e mediu conforme estas medidas;
Kenaka anapita nane ku chipata chakumpoto ndipo anachiyeza. Chinali chofanana ndi zina zija.
36 As suas camarinhas, os seus pilares, e os seus vestíbulos; também tinha janelas em redor: o comprimento era de cincoênta côvados, e a largura de vinte e cinco côvados.
Zipinda zake za alonda, makoma ake ndiponso khonde lake zinali zofanana ndi zina zija, ndipo chinalinso ndi mipata mbali zonse ziwiri. Mulitali mwake munali mamita 27 ndipo mulifupi mwake munali mamita 13.
37 E os seus pilares estavam no átrio exterior: também havia palmas nos seus pilares de uma e de outra banda; e eram as suas subidas de oito degraus.
Khonde lake limayangʼanana ndi bwalo lakunja. Pa mphuthu zake anajambulapo zithunzi za kanjedza mbali zonse ziwiri, ndipo linali ndi makwerero asanu ndi atatu.
38 E a sua câmara e a sua porta estavam junto aos pilares das portas onde levavam o holocausto.
Panali chipinda ndipo khomo lake linali pafupi ndi khonde la chipata cholowera chamʼkati. Mʼchipinda mʼmenemo ankatsukira nyama ya nsembe yopsereza.
39 E no vestíbulo da porta havia duas mesas de uma banda, e duas mesas da outra, para nelas se degolar o holocausto e o sacrifício pelo pecado e pela culpa.
Pa khonde la chipatacho panali matebulo awiri, lina kuno lina uko. Ankapherapo nsembe zopsereza, nsembe zopepesera machimo ndi nsembe zopepesera kupalamula.
40 Também da banda de fora da subida para a entrada da porta do norte havia duas mesas; e da outra banda, que estava no vestíbulo da porta, havia duas mesas.
Panali matebulo anayi, awiri a iwo anali kunja kwa khoma la khonde pafupi ndi makwerero olowera pa chipata chakumpoto ndi awiri enawo anali mbali inayo ya makwerero.
41 Quatro mesas de uma, e quatro mesas da outra banda; aos lados da porta oito mesas, sobre as quais imolavam.
Choncho ku mbali imodzi ya chipata kunali matebulo anayi, ndiponso ku mbali inayo kunali matebulo anayi. Onse pamodzi anali matebulo asanu ndi atatu. Pa matebulopo ankapherapo nyama za nsembe zopsereza.
42 E as quatro mesas para o holocausto eram de pedras lavradas: o comprimento era de um côvado e meio, e a largura de um côvado e meio, e a altura de um côvado: e sobre elas se punham os instrumentos com que imolavam o holocausto e o sacrifício.
Matebulo anayiwa anali a miyala yosema. Lililonse mulitali mwake linali la masentimita 75, mulifupi mwake linali la masentimita 75, ndipo msinkhu wake unali wa masentimita makumi asanu. Pa matebulopo amayikapo zipangizo zophera nsembe zopsereza ndi nsembe zina.
43 E as pedras do lar eram de um palmo de grossura, postas na casa em redor, e sobre as mesas a carne da oferta.
Choncho pa matebulopo ankayikapo nyama za nsembe zopsereza. Mbedza zitatu zazitali ngati chikhatho amazikoleka pa makoma pozungulira ponse.
44 E fora da porta interior estavam as câmaras dos cantores, no átrio de dentro, que estava da banda da porta do norte e olhava para o caminho do sul: uma estava à banda da porta do oriente, a qual olhava para o caminho do norte.
Munthu uja anapita nane mʼkati mwa bwalo ndipo ndinaona zipinda ziwiri. Chimodzi chinali pafupi ndi chipata chakumpoto kuyangʼana kummwera ndi china chinali pafupi ndi chipata chakummwera kuyangʼana kumpoto.
45 E ele me disse: Esta câmara que olha para o caminho do sul é para os sacerdotes que tem a guarda do templo.
Munthuyo anandiwuza kuti, “Chipinda chimene chikuyangʼana kummwera ndi cha ansembe amene amayangʼanira Nyumba ya Mulungu,
46 Mas a câmara que olha para o caminho do norte é para os sacerdotes que tem a guarda do altar: estes são os filhos de Zadoc, que se chegam ao Senhor, dentre os filhos de Levi, para o servir.
ndipo chipinda chimene chikuyangʼana kumpoto ndi cha ansembe amene amayangʼanira guwa lansembe. Amenewa ndiwo ana a Zadoki, ndipo ndi okhawo mwa zidzukulu za Levi amene ayenera kutumikira pamaso pa Yehova mʼNyumba ya Mulungu.”
47 E mediu o átrio: o comprimento de cem côvados e a largura de cem côvados, quadrado; e o altar estava diante do templo.
Kenaka munthuyo anayeza bwalo; linali lofanana mbali zonse kutalika kwake, mulitali mwake munali mamita 53, ndipo mulifupi mwake munali mamita 53. Ndipo guwa lansembe linali kutsogolo kwa Nyumba ya Mulungu.
48 Então me levou ao vestíbulo do templo, e mediu a cada pilar do vestíbulo, cinco côvados de uma banda, e cinco côvados da outra; e a largura da porta, três côvados de uma banda, e três côvados da outra.
Munthuyo anapita nane pa khonde la Nyumba ya Mulunguyo. Anayeza mphuthu za khondelo ndipo zinali mamita awiri ndi theka mbali zonse. Mulifupi mwa chipatacho munali mamita asanu ndi awiri ndipo mulifupi mwa makoma ake munali mamita awiri mbali zonse.
49 O comprimento do vestíbulo era de vinte côvados, e a largura de onze côvados, e com degraus, pelos quais se subia; e havia colunas junto aos pilares, uma de uma banda e outra da outra.
Mulitali mwa khonde munali mamita khumi, mulifupi mwake munali mamita asanu ndi limodzi kuchokera kutsogolo mpaka kumbuyo. Panali makwerero khumi, ndipo mbali zonse kunali nsanamira.