< Amós 5 >

1 Ouvi esta palavra, que levanto sobre vós uma lamentação, ó casa de Israel.
Israeli, imva mawu awa, nyimbo ya maliro imene ndikuyimba za iweyo:
2 A virgem de Israel caiu, nunca mais tornará a levantar-se: desamparada está na sua terra, não há quem a levante.
“Namwali Israeli wagwa, moti sadzadzukanso, wasiyidwa mʼdziko lake lomwe, popanda woti ndi kumudzutsa.”
3 Porque assim diz o Senhor Jehovah: A cidade da qual saem mil conservará cem, e aquela da qual saem cem conservará dez à casa de Israel.
Ambuye Yehova akuti, “Mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 1,000 amphamvu udzatsala ndi anthu 100 okha; mzinda umene udzapite ku nkhondo ndi anthu 100 amphamvu udzatsala ndi anthu khumi okha basi.”
4 Porque assim diz o Senhor à casa de Israel: buscai-me, e vivei.
Zimene Yehova akunena kwa nyumba ya Israeli ndi izi: “Mundifunefune kuti mukhale ndi moyo;
5 Porém não busqueis a bethel, nem venhais a Gilgal, nem passeis a Berseba, porque Gilgal certamente será levado cativo, e bethel será desfeito em nada.
musafunefune Beteli, musapite ku Giligala, musapite ku Beeriseba. Pakuti Giligala adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo, ndipo Beteli adzawonongekeratu.”
6 Buscai ao Senhor, e vivei, para que não acommetta a casa de José como um fogo, e a consuma, e não haja em bethel quem o apague.
Funani Yehova kuti mukhale ndi moyo, mukapanda kutero Iye adzatentha nyumba ya Yosefe ngati moto; motowo udzawononga, ndipo sipadzakhala wina wozimitsa motowo ku Beteli.
7 (Os que pervertem o juízo em alosna, e deitam na terra a justiça.)
Inu amene mumasandutsa chiweruzo cholungama kukhala chowawa ndi kunyoza chilungamo.
8 O que faz o setestrello, e o orion, e torna a sombra da noite em manhã, e escurece o dia como a noite, que chama as águas do mar, e as derrama sobre a terra, o Senhor é o seu nome.
(Iye amene analenga nyenyezi za Nsangwe ndi Akamwiniatsatana, amene amasandutsa mdima kuti ukhale mmawa ndi kudetsa usana kuti ukhale usiku, amene amayitana madzi a mʼnyanja ndi kuwathira pa dziko lapansi, Yehova ndiye dzina lake.
9 O que esforça o despojado contra o forte: assim que venha a assolação contra a fortaleza.
Iyeyo amabweretsa chiwonongeko modzidzimutsa pa anthu amphamvu ndi kuwononga mizinda yotetezedwa),
10 Na porta aborrecem o que os repreende, e abominam o que fala sinceramente.
inu mumadana ndi amene amadzudzula mʼbwalo la milandu ndi kunyoza amene amanena zoona.
11 Portanto, visto que pizais o pobre, e dele tomais um cargo de trigo, edificastes casas de pedras lavradas, mas nelas não habitareis; vinhas desejáveis plantastes, mas não bebereis do seu vinho.
Mumapondereza munthu wosauka ndi kumukakamiza kuti akupatseni tirigu. Nʼchifukwa chake, ngakhale mwamanga nyumba zamiyala yosema, inuyo simudzakhalamo. Ngakhale mwalima minda yabwino ya mphesa, inu simudzamwa vinyo wake.
12 Porque sei que são muitas as vossas transgressões, e grossos os vossos pecados: afligem o justo, tomam resgate, e rejeitam os necessitados na porta.
Pakuti Ine ndikudziwa kuchuluka kwa zolakwa zanu ndi kukula kwa machimo anu. Inu mumapondereza anthu olungama ndi kulandira ziphuphu ndipo anthu osauka simuwaweruza mwachilungamo mʼmabwalo anu amilandu.
13 Portanto, o prudente naquele tempo se calará, porque o tempo será mau.
Nʼchifukwa chake pa nthawi yotere munthu wanzeru sayankhulapo kanthu, popeza ndi nthawi yoyipa.
14 Buscai o bem, e não o mal, para que vivais: e assim o Senhor, o Deus dos exércitos, estará convosco, como dizeis.
Muyike mtima wanu pa zabwino osati pa zoyipa, kuti mukhale ndi moyo. Mukatero Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzakhala nanu, monga mmene mumanenera kuti ali nanu.
15 Aborrecei o mal, e amai o bem, e estabelecei o juízo na porta: porventura o Senhor, o Deus dos exércitos, terá piedade do resto de José.
Mudane ndi zoyipa, mukonde zabwino; mukhazikitse chiweruzo cholungama mʼmabwalo anu amilandu. Mwina mwake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse adzachitira chifundo anthu otsala a mʼbanja la Yosefe.
16 Portanto, assim diz o Senhor Deus dos exércitos, o Senhor: Em todas as ruas haverá pranto, e em todos os bairros dirão: Ai! ai! E ao lavrador chamarão a choro, e ao pranto aos que souberem prantear.
Choncho izi ndi zimene Ambuye, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, akunena: “Mʼmisewu monse mudzakhala kulira mofuwula, ndi kulira chifukwa cha kuwawa kwa masautso kudzakhala paliponse. Adzayitana alimi kuti adzalire, ndipo anthu odziwa maliridwe anthetemya adzalira mofuwula.
17 E em todas as vinhas haverá pranto; porque passarei pelo meio de ti, diz o Senhor.
Mʼminda yonse ya mpesa mudzakhala kulira kokhakokha, pakuti Ine ndidzadutsa pakati panu,” akutero Yehova.
18 Ai daqueles que desejam o dia do Senhor! para que pois vos será este dia do Senhor? trevas será e não luz.
Tsoka kwa inu amene mumalakalaka tsiku la Yehova! Chifukwa chiyani mumalakalaka tsiku la Yehova? Tsikulo kudzakhala mdima osati kuwala.
19 Como o que foge de diante do leão, e se encontra com ele o urso, ou como se entrasse numa casa, e a sua mão encostasse à parede, e fosse mordido de uma cobra.
Lidzakhala ngati tsiku limene munthu pothawa mkango amakumana ndi chimbalangondo, ngati pamene munthu walowa mʼnyumba, natsamira dzanja lake pa khoma ndipo njoka nʼkuluma.
20 Não será pois o dia do Senhor trevas e não luz? e escuridade, sem que haja resplandor?
Kodi tsiku la Yehova silidzakhala mdima osati kuwala, mdima wandiweyani, popanda powala pena paliponse?
21 Aborreço, desprezo as vossas festas, e os vossos dias de proibição não me darão bom cheiro.
“Ndimadana nawo masiku anu achikondwerero ndipo ndimawanyoza; sindikondwera nayo misonkhano yanu.
22 Porque ainda que me ofereceis holocaustos, como também as vossas ofertas de manjares, não me agrado delas: nem atentarei para as ofertas pacíficas de vossos animais gordos.
Ngakhale mupereke nsembe zopsereza ndi nsembe zachakudya, Ine sindidzazilandira. Ngakhale mupereke nsembe zabwino zachiyanjano, Ine sindidzaziyangʼana nʼkomwe.
23 Afasta de mim o estrépito dos teus cânticos; porque não ouvirei as salmodias dos teus instrumentos.
Musandisokose nazo nyimbo zanu! Sindidzamvetsera kulira kwa azeze anu.
24 Corra porém o juízo como as águas, e a justiça como o ribeiro impetuoso.
Koma chiweruzo cholungama chiyende ngati madzi, chilungamo ngati mtsinje wosaphwa!
25 Haveis-me porventura oferecido sacrifícios e ofertas no deserto por quarenta anos, ó casa de Israel?
“Kodi pa zaka makumi anayi zimene munakhala mʼchipululu muja munkandibweretsera nsembe ndi zopereka, inu nyumba ya Israeli?
26 Antes levastes a tenda de vosso Moloch, e a estátua das vossas imagens, a estrela do vosso deus, que fizestes para vós mesmos.
Inu mwanyamula kachisi wa mfumu yanu, ndi nyenyezi ija Kaiwani, mulungu wanu, mafano amene munadzipangira.
27 Portanto vos levarei cativos, para além de Damasco, diz o Senhor, cujo nome é o Deus dos exércitos.
Nʼchifukwa chake Ine ndidzakupititsani ku ukapolo, kutali kupitirira ku Damasiko,” akutero Yehova, amene dzina lake ndi Mulungu Wamphamvuzonse.

< Amós 5 >