< Salmos 44 >
1 Ó Deus, nós ouvimos com os nossos ouvidos, e nossos paes nos teem contado a obra que fizeste em seus dias, nos tempos da antiguidade.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Ife tamva ndi makutu athu, Inu Mulungu; makolo athu atiwuza zimene munachita mʼmasiku awo, masiku akalekalewo.
2 Como expelliste as nações com a tua mão e os plantaste a elles: como affligiste os povos e os derribaste.
Ndi dzanja lanu munathamangitsa mitundu ya anthu ena ndi kudzala makolo athu; Inu munakantha mitundu ya anthu, koma makolo athuwo Inu munawapatsa ufulu.
3 Pois não conquistaram a terra pela sua espada, nem o seu braço os salvou, mas a tua dextra e o teu braço, e a luz da tua face, porquanto te agradaste d'elles.
Sanalande dziko ndi lupanga lawo, si mkono wawo umene unawabweretsera chigonjetso, koma ndi dzanja lanu lamanja, mkono wanu ndi kuwala kwa nkhope yanu, pakuti munawakonda.
4 Tu és o meu Rei, ó Deus: ordena salvações para Jacob.
Inu ndinu Mfumu yanga ndi Mulungu wanga amene mumalamulira chigonjetso cha Yakobo.
5 Por ti escornearemos os nossos inimigos: pelo teu nome pizaremos os que se levantam contra nós:
Kudzera kwa inu ife timabweza adani athu; kudzera mʼdzina lanu timapondereza otiwukirawo.
6 Pois eu não confiarei no meu arco, nem a minha espada me salvará.
Sindidalira uta wanga, lupanga langa silindibweretsera chigonjetso;
7 Mas tu nos salvaste dos nossos inimigos, e confundiste os que nos aborreciam.
koma Inu mumatigonjetsera adani athu, mumachititsa manyazi amene amadana nafe.
8 Em Deus nos gloriamos todo o dia, e louvamos o teu nome eternamente (Selah)
Timanyadira mwa Mulungu wathu tsiku lonse, ndipo tidzatamanda dzina lanu kwamuyaya.
9 Mas agora tu nos rejeitaste e nos confundiste, e não saes com os nossos exercitos.
Koma tsopano mwatikana ndi kutichepetsa; Inu simupitanso ndi ankhondo athu.
10 Faze-nos retirar do inimigo, e aquelles que nos odeiam nos saqueiam para si.
Munachititsa ife kubwerera mʼmbuyo pamaso pa mdani ndipo amene amadana nafe atilanda katundu.
11 Tu nos entregaste como ovelhas para comer, e nos espalhaste entre as nações.
Inu munatipereka kuti tiwonongedwe monga nkhosa ndipo mwatibalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina.
12 Tu vendes por nada o teu povo, e não augmentas a tua riqueza com o seu preço.
Inu munagulitsa anthu anu pa mtengo wotsika, osapindulapo kanthu pa malondawo.
13 Tu nos pões por opprobrio aos nossos visinhos, por escarneo e zombaria de aquelles que estão á roda de nós.
Mwachititsa kuti tikhale chochititsa manyazi kwa anthu a mitundu ina, chonyozeka ndi chothetsa nzeru kwa iwo amene atizungulira.
14 Tu nos pões por proverbio entre as nações, por movimento de cabeça entre os povos.
Mwachititsa kuti tikhale onyozeka pakati pa anthu a mitundu ina; anthu amapukusa mitu yawo akationa.
15 A minha confusão está constantemente diante de mim, e a vergonha do meu rosto me cobre:
Manyazi anga ali pamaso panga tsiku lonse ndipo nkhope yanga yaphimbidwa ndi manyazi
16 Á voz d'aquelle que affronta e blasphema, por causa do inimigo e do vingador.
chifukwa cha mawu otonza a iwo amene amandinyoza ndi kundichita chipongwe, chifukwa cha mdani amene watsimikiza kubwezera.
17 Tudo isto nos sobreveiu: comtudo não nos esquecemos de ti, nem nos houvemos falsamente contra o teu concerto.
Zonsezi zinatichitikira ngakhale kuti ifeyo sitinayiwale Inu kapena kuonetsa kusakhulupirika pa pangano lanu.
18 O nosso coração não voltou atraz, nem os nossos passos se desviaram das tuas veredas;
Mitima yathu sinabwerere mʼmbuyo; mapazi athu sanatayike pa njira yanu.
19 Ainda que nos quebrantaste n'um logar de dragões, e nos cobriste com a sombra da morte.
Koma Inu mwatiphwanya ndi kuchititsa kuti tikhale ozunzidwa ndi ankhandwe ndipo mwatiphimba ndi mdima waukulu.
20 Se nós esquecemos o nome do nosso Deus, e estendemos as nossas mãos para um deus estranho,
Tikanayiwala dzina la Mulungu wathu kapena kutambasulira manja athu kwa mulungu wachilendo,
21 Porventura não esquadrinhará Deus isso? pois elle sabe os segredos do coração.
kodi Mulungu wathu sakanazidziwa zimenezi, pakuti Iye amadziwa zinsinsi zamumtima?
22 Sim, por amor de ti, somos mortos todo o dia: somos tidos na conta de ovelhas para o matadouro.
Komabe chifukwa cha Inu timakumana ndi imfa tsiku lonse, tili ngati nkhosa zoyenera kuti ziphedwe.
23 Desperta, porque dormes, Senhor? acorda, não nos rejeites para sempre.
Dzukani Ambuye! Nʼchifukwa chiyani mukugona! Dziwutseni nokha! Musatikane kwamuyaya.
24 Porque escondes a tua face, e te esqueces da nossa miseria e da nossa oppressão?
Nʼchifukwa chiyani mukubisa nkhope yanu, ndi kuyiwala mavuto athu ndi kuponderezedwa kwathu?
25 Pois a nossa alma está abatida até ao pó; o nosso ventre se apega á terra.
Tatsitsidwa pansi mpaka pa fumbi; matupi athu amatirira pa dothi.
26 Levanta-te em nosso auxilio, e resgata-nos por amor das tuas misericordias.
Imirirani ndi kutithandiza, tiwomboleni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.