< Salmos 3 >
1 Senhor, como se teem multiplicado os meus adversarios! são muitos os que se levantam contra mim.
Salimo la Davide. Atathawa mwana wake Abisalomu. Inu Yehova, achulukadi adani anga! Achulukadi amene andiwukira!
2 Muitos dizem da minha alma: Não ha salvação para elle em Deus (Selah)
Ambiri akunena za ine kuti, “Mulungu sadzamupulumutsa.” (Sela)
3 Porém tu, Senhor, és um escudo para mim, a minha gloria, e o que exalta a minha cabeça.
Koma Inu Yehova, ndinu chishango chonditeteza, Inu mwandiveka ulemerero ndipo mwanditukula.
4 Com a minha voz clamei ao Senhor, e ouviu-me desde o seu sancto monte (Selah)
Kwa Yehova, Ine ndilira mofuwula ndipo Iye amandiyankha kuchokera ku phiri lake loyera. (Sela)
5 Eu me deitei e dormi: acordei; porque o Senhor me sustentou.
Ine ndimagona ndi kupeza tulo; ndimadzukanso chifukwa Yehova amandichirikiza.
6 Não temerei os milhares de povo que se pozeram contra mim e me cercam.
Sindidzaopa adani anga osawerengeka amene abwera kulimbana nane kuchokera ku madera onse.
7 Levanta-te, Senhor; salva-me, Deus meu; pois feriste a todos os meus inimigos nos queixos; quebraste os dentes aos impios.
Dzukani, Inu Yehova! Pulumutseni, Inu Mulungu wanga. Akantheni adani anga onse pa msagwada; gululani mano a anthu oyipa.
8 A salvação vem do Senhor; sobre o teu povo seja a tua benção. (Selah)
Chipulumutso chimachokera kwa Yehova. Madalitso akhale pa anthu anu. (Sela)