< Salmos 20 >

1 O Senhor te oiça no dia da angustia, o nome do Deus de Jacob te proteja.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Yehova akuyankhe pamene uli pa msautso; dzina la Mulungu wa Yakobo likuteteze.
2 Envie-te soccorro desde o seu sanctuario, e te sustenha desde Sião.
Iye atumize thandizo kuchokera ku malo ake opatulika; akugwirizize kuchokera ku Ziyoni.
3 Lembre-se de todas as tuas offertas, e acceite os teus holocaustos (Selah)
Iye akumbukire nsembe zako zonse ndipo alandire nsembe zako zopsereza. (Sela)
4 Conceda-te conforme ao teu coração, e cumpra todo o teu conselho.
Akupatse chokhumba cha mtima wako ndipo akuthandize kuti zonse wakonza zichitike.
5 Nós nos alegraremos pela tua salvação, e em nome do nosso Deus arvoraremos pendões; cumpra o Senhor todas as tuas petições.
Ife tidzafuwula ndi chimwemwe pamene iwe wapambana ndipo tidzanyamula mbendera zathu mʼdzina la Mulungu wathu, Yehova ayankhe zopempha zako zonse.
6 Agora sei que o Senhor salva ao seu ungido: elle o ouvirá desde o seu sancto céu, com a força salvadora da sua mão direita.
Tsopano ndadziwa kuti Yehova amapulumutsa wodzozedwa wake; Iye amamuyankha kuchokera kumwamba ku malo ake opatulika ndi mphamvu yopulumutsa ya dzanja lake lamanja.
7 Uns confiam em carros e outros em cavallos, mas nós faremos menção do nome do Senhor nosso Deus.
Ena amadalira magaleta ndipo ena akavalo koma ife tidzadalira dzina la Yehova Mulungu wathu.
8 Uns encurvam-se e caem, mas nós nos levantamos e estamos de pé.
Iwo amagonjetsedwa ndi kugwa, koma ife timadzuka ndi kuyima chilili.
9 Salva-nos, Senhor, oiça-nos o Rei quando clamarmos.
Inu Yehova, pulumutsani mfumu! Tiyankheni pamene tikuyitanani!

< Salmos 20 >