< Salmos 119 >
1 Bemaventurados os rectos em seus caminhos, que andam na lei do Senhor.
Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
2 Bemaventurados os que guardam os seus testemunhos, e que o buscam com todo o coração,
Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
3 E não obram iniquidade: andam nos seus caminhos.
Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
4 Tu ordenaste os teus mandamentos, para que diligentemente os observassemos.
Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
5 Oxalá que os meus caminhos fossem dirigidos a observar os teus estatutos.
Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
6 Então não serei envergonhado, quando tiver respeito a todos os teus mandamentos.
Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
7 Louvar-te-hei com rectidão de coração, quando tiver aprendido os teus justos juizos.
Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
8 Observarei os teus estatutos: não me desampares totalmente.
Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
9 Com que purificará o mancebo o seu caminho? observando-o conforme a tua palavra.
Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
10 Com todo o meu coração te busquei: não me deixes desviar dos meus mandamentos.
Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
11 A tua palavra tenho eu escondido no meu coração, para não peccar contra ti
Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
12 Bemdito és tu, ó Senhor; ensina-me os teus estatutos.
Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
13 Com os meus labios declarei todos os juizos da tua bocca.
Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
14 Folguei tanto no caminho dos teus testemunhos, como em todas as riquezas.
Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
15 Meditarei nos teus preceitos, e terei respeito aos teus caminhos.
Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
16 Recrear-me-hei nos teus estatutos: não me esquecerei da tua palavra.
Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
17 Faze bem ao teu servo, para que viva e observe a tua palavra.
Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
18 Abre tu os meus olhos, para que veja as maravilhas da tua lei.
Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
19 Sou peregrino na terra: não escondas de mim os teus mandamentos.
Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
20 A minha alma está quebrantada de desejar os teus juizos em todo o tempo.
Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
21 Tu reprehendeste asperamente os soberbos que são amaldiçoados, que se desviam dos teus mandamentos.
Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
22 Tira de sobre mim o opprobrio e o desprezo, pois guardei os teus testemunhos.
Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
23 Principes tambem se assentaram, e fallaram contra mim, mas o teu servo meditou nos teus estatutos.
Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
24 Tambem os teus testemunhos são o meu prazer e os meus conselheiros.
Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
25 A minha alma está pegada ao pó: vivifica-me segundo a tua palavra.
Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
26 Eu te contei os meus caminhos, e tu me ouviste: ensina-me os teus estatutos.
Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
27 Faze-me entender os caminhos dos teus preceitos: assim fallarei das tuas maravilhas.
Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
28 A minha alma se derrete de tristeza: fortalece-me segundo a tua palavra.
Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
29 Desvia de mim o caminho da falsidade, e concede-me piedosamente a tua lei.
Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
30 Tenho escolhido o caminho da verdade: os teus juizos tenho posto diante de mim.
Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
31 Tenho-me apegado aos teus testemunhos: ó Senhor, não me confundas.
Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
32 Percorrerei o caminho dos teus mandamentos, quando dilatares o meu coração.
Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
33 Ensina-me, ó Senhor, o caminho dos teus estatutos, e guardal-o-hei até ao fim.
Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
34 Dá-me entendimento, e guardarei a tua lei, e observal-a-hei de todo o meu coração.
Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
35 Faze-me andar na vereda dos teus mandamentos, porque n'ella tenho prazer.
Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
36 Inclina o meu coração aos teus testemunhos, e não á cubiça.
Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
37 Desvia os meus olhos de contemplarem a vaidade, e vivifica-me no teu caminho.
Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
38 Confirma a tua palavra ao teu servo, que é dedicado ao teu temor.
Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
39 Desvia de mim o opprobrio que temo, pois os teus juizos são bons.
Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
40 Eis que tenho desejado os teus preceitos; vivifica-me na tua justiça.
Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
41 Venham sobre mim tambem as tuas misericordias, ó Senhor, e a tua salvação segundo a tua palavra.
Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
42 Assim terei que responder ao que me affronta, pois confio na tua palavra.
ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
43 E não tires totalmente a palavra de verdade da minha bocca, pois tenho esperado nos teus juizos.
Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
44 Assim observarei de continuo a tua lei para sempre e eternamente.
Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
45 E andarei em liberdade; pois busco os teus preceitos.
Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
46 Tambem fallarei dos teus testemunhos perante os reis, e não me envergonharei.
Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
47 E recrear-me-hei em teus mandamentos, que tenho amado.
popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
48 Tambem levantarei as minhas mãos para os teus mandamentos, que amei, e meditarei nos teus estatutos.
Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
49 Lembra-te da palavra dada ao teu servo, na qual me fizeste esperar.
Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
50 Isto é a minha consolação na minha afflicção, porque a tua palavra me vivificou.
Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
51 Os soberbos zombaram grandemente de mim; comtudo não me desviei da tua lei.
Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
52 Lembrei-me dos teus juizos antiquissimos, ó Senhor, e assim me consolei.
Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
53 Grande indignação se apoderou de mim por causa dos impios que desamparam a tua lei.
Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
54 Os teus estatutos teem sido os meus canticos, na casa da minha peregrinação.
Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
55 Lembrei-me do teu nome, ó Senhor, de noite, e observei a tua lei.
Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
56 Isto fiz eu, porque guardei os teus mandamentos.
Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
57 O Senhor é a minha porção: eu disse que observaria as tuas palavras.
Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
58 Roguei devéras o teu favor com todo o meu coração: tem piedade de mim, segundo a tua palavra.
Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
59 Considerei os meus caminhos, e voltei os meus pés para os teus testemunhos.
Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
60 Apressei-me, e não me detive, a observar os teus mandamentos.
Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
61 Bandos de impios me despojaram, mas eu não me esqueci da tua lei.
Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
62 Á meia noite me levantarei para te louvar, pelos teus justos juizos.
Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
63 Companheiro sou de todos os que te temem e dos que guardam os teus preceitos.
Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
64 A terra, ó Senhor, está cheia da tua benignidade: ensina-me os teus estatutos.
Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
65 Fizeste bem ao teu servo, Senhor, segundo a tua palavra.
Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
66 Ensina-me bom juizo e sciencia, pois cri nos teus mandamentos.
Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
67 Antes de ser afflicto andava errado; mas agora tenho guardado a tua palavra.
Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
68 Tu és bom e fazes bem: ensina-me os teus estatutos.
Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
69 Os soberbos forjaram mentiras contra mim; mas eu com todo o meu coração guardarei os teus preceitos.
Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
70 Engrossa-se-lhes o coração como gordura, mas eu me recreio na tua lei.
Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
71 Foi-me bom ter sido afflicto, para que aprendesse os teus estatutos.
Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
72 Melhor é para mim a lei da tua bocca do que milhares de oiro ou prata.
Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
73 As tuas mãos me fizeram e me formaram; dá-me intelligencia para entender os teus mandamentos.
Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
74 Os que te temem alegraram-se quando me viram, porque tenho esperado na tua palavra.
Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
75 Bem sei eu, ó Senhor, que os teus juizos são justos, e que segundo a tua fidelidade me affligiste.
Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
76 Sirva pois a tua benignidade para me consolar, segundo a palavra que déste ao teu servo.
Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
77 Venham sobre mim as tuas misericordias, para que viva, pois a tua lei é as minhas delicias.
Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
78 Confundam-se os soberbos, pois me trataram d'uma maneira perversa, sem causa; mas eu meditarei nos teus preceitos.
Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
79 Voltem-se para mim os que te temem, e aquelles que teem conhecido os teus testemunhos.
Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
80 Seja recto o meu coração nos teus estatutos, para que não seja confundido.
Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
81 Desfallece a minha alma pela tua salvação, mas espero na tua palavra.
Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
82 Os meus olhos desfallecem pela tua palavra; entretanto dizia: Quando me consolarás tu?
Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
83 Pois estou como odre no fumo; comtudo não me esqueço dos teus estatutos.
Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
84 Quantos serão os dias do teu servo? Quando me farás justiça contra os que me perseguem?
Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
85 Os soberbos me cavaram covas, o que não é conforme á tua lei.
Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
86 Todos os teus mandamentos são verdade: com mentiras me perseguem; ajuda-me.
Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
87 Quasi que me teem consumido sobre a terra, mas eu não deixei os teus preceitos.
Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
88 Vivifica-me segundo a tua benignidade; assim guardarei o testemunho da tua bocca.
Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
89 Para sempre, ó Senhor, a tua palavra permanece no céu.
Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
90 A tua fidelidade dura de geração em geração: tu firmaste a terra, e ella permanece firme.
Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
91 Elles continuam até ao dia d'hoje, segundo as tuas ordenações; porque todos são teus servos.
Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
92 Se a tua lei não fôra toda a minha recreação, ha muito que pereceria na minha afflicção.
Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
93 Nunca me esquecerei dos teus preceitos; pois por elles me tens vivificado.
Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
94 Sou teu, salva-me; pois tenho buscado os teus preceitos.
Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
95 Os impios me esperam para me destruirem, mas eu considerarei os teus testemunhos.
Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
96 Tenho visto fim a toda a perfeição, mas o teu mandamento é amplicissimo.
Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
97 Oh! quanto amo a tua lei! é a minha meditação em todo o dia.
Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
98 Tu pelos teus mandamentos me fazes mais sabio do que os meus inimigos, pois estão sempre comigo.
Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
99 Tenho mais entendimento do que todos os meus mestres, porque os teus testemunhos são a minha meditação.
Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
100 Entendo mais do que os antigos; porque guardo os teus preceitos.
Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
101 Desviei os meus pés de todo o caminho mau, para guardar a tua palavra.
Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
102 Não me apartei dos teus juizos, pois tu me ensinaste.
Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
103 Oh! quão doces são as tuas palavras ao meu paladar, mais doces do que o mel á minha bocca.
Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
104 Pelos teus mandamentos alcancei entendimento; pelo que aborreço todo o falso caminho.
Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
105 A tua palavra é uma lampada para os meus pés e uma luz para o meu caminho.
Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
106 Jurei, e o cumprirei, que guardarei os teus justos juizos.
Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
107 Estou afflictissimo; vivifica-me, ó Senhor, segundo a tua palavra.
Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
108 Acceita, eu te rogo, as offerendas voluntarias da minha bocca, ó Senhor; ensina-me os teus juizos.
Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
109 A minha alma está de continuo nas minhas mãos; todavia não me esqueço da tua lei
Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
110 Os impios me armaram laço; comtudo não me desviei dos teus preceitos.
Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
111 Os teus testemunhos tenho eu tomado por herança para sempre, pois são o gozo do meu coração.
Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
112 Inclinei o meu coração a guardar os teus estatutos, para sempre, até ao fim.
Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
113 Aborreço a duplicidade, mas amo a tua lei.
Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
114 Tu és o meu refugio e o meu escudo; espero na tua palavra.
Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
115 Apartae-vos de mim, malfeitores, pois guardarei os mandamentos do meu Deus.
Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
116 Sustenta-me conforme a tua palavra, para que viva, e não me deixes envergonhado da minha esperança.
Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
117 Sustenta-me, e serei salvo, e de continuo terei respeito aos teus estatutos.
Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
118 Tu tens pisado aos pés todos os que se desviam dos teus estatutos, pois o engano d'elles é falsidade.
Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
119 Tu tiraste da terra todos os impios, como a escoria, pelo que amo os teus testemunhos.
Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
120 O meu corpo se arrepiou com temor de ti, e temi os teus juizos.
Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
121 Fiz juizo e justiça: não me entregues aos meus oppressores.
Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
122 Fica por fiador do teu servo para o bem; não deixes que os soberbos me opprimam.
Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
123 Os meus olhos desfalleceram pela tua salvação e pela promessa da tua justiça.
Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
124 Usa com o teu servo segundo a tua benignidade, e ensina-me os teus estatutos.
Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
125 Sou teu servo: dá-me intelligencia, para entender os teus testemunhos.
Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
126 Já é tempo de operares ó Senhor, pois elles teem quebrantado a tua lei.
Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
127 Pelo que amo os teus mandamentos mais do que o oiro, e ainda mais do que o oiro fino.
Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
128 Por isso estimo todos os teus preceitos ácerca de tudo, como rectos, e aborreço toda a falsa vereda.
ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
129 Maravilhosos são os teus testemunhos; portanto a minha alma os guarda.
Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
130 A entrada das tuas palavras dá luz, dá entendimento aos simplices.
Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
131 Abri a minha bocca, e respirei, pois que desejei os teus mandamentos.
Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
132 Olha para mim, e tem piedade de mim, conforme usas com os que amam o teu nome.
Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
133 Ordena os meus passos na tua palavra, e não se apodere de mim iniquidade alguma.
Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
134 Livra-me da oppressão do homem; assim guardarei os teus preceitos.
Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
135 Faze resplandecer o teu rosto sobre o teu servo, e ensina-me os teus estatutos.
Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
136 Rios d'aguas correm dos meus olhos, porque não guardam a tua lei.
Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
137 Justo és, ó Senhor, e rectos são os teus juizos.
Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
138 Os teus testemunhos que ordenaste são rectos e muito fieis.
Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
139 O meu zelo me consumiu, porque os meus inimigos se esqueceram da tua palavra.
Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
140 A tua palavra é muito pura; portanto o teu servo a ama.
Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
141 Pequeno sou e desprezado, porém não me esqueço dos teus mandamentos.
Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
142 A tua justiça é uma justiça eterna, e a tua lei é a verdade.
Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
143 Aperto e angustia se apoderam de mim; comtudo os teus mandamentos são o meu prazer.
Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
144 A justiça dos teus testemunhos é eterna; dá-me intelligencia, e viverei.
Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
145 Clamei de todo o meu coração; escuta-me, Senhor, e guardarei os teus estatutos.
Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
146 A ti te invoquei; salva-me, e guardarei os teus testemunhos.
Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
147 Preveni a alva da manhã, e clamei: esperei na tua palavra.
Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
148 Os meus olhos preveniram as vigilias da noite, para meditar na tua palavra.
Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
149 Ouve a minha voz, segundo a tua benignidade: vivifica-me, ó Senhor, segundo o teu juizo.
Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
150 Approximam-se os que se dão a maus tratos: affastam-se da tua lei.
Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
151 Tu estás perto ó Senhor, e todos os teus mandamentos são a verdade.
Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
152 Ácerca dos teus testemunhos soube, desde a antiguidade, que tu os fundaste para sempre.
Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
153 Olha para a minha afflicção, e livra-me, pois não me esqueci da tua lei.
Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
154 Pleiteia a minha causa, e livra-me: vivifica-me segundo a tua palavra.
Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
155 A salvação está longe dos impios, pois não buscam os teus estatutos.
Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
156 Muitas são, ó Senhor, as tuas misericordias: vivifica-me segundo os teus juizos.
Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
157 Muitos são os meus perseguidores e os meus inimigos; porém não me desvio dos teus testemunhos.
Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
158 Vi os transgressores, e me affligi, porque não observam a tua palavra.
Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
159 Considera como amo os teus preceitos: vivifica-me, ó Senhor, segundo a tua benignidade.
Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
160 A tua palavra é a verdade desde o principio, e cada um dos teus juizos dura para sempre.
Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
161 Principes me perseguiram sem causa, mas o meu coração temeu a tua palavra.
Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
162 Folgo com a tua palavra, como aquelle que acha um grande despojo.
Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
163 Abomino e aborreço a falsidade, porém amo a tua lei.
Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
164 Sete vezes no dia te louvo pelos juizos da tua justiça.
Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
165 Muita paz teem os que amam a tua lei, e para elles não ha tropeço.
Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
166 Senhor, tenho esperado na tua salvação, e tenho cumprido os teus mandamentos.
Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
167 A minha alma tem observado os teus testemunhos; amo-os excessivamente.
Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
168 Tenho observado os teus preceitos e os teus testemunhos, porque todos os meus caminhos estão diante de ti.
Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
169 Chegue a ti o meu clamor, ó Senhor: dá-me entendimento conforme a tua palavra.
Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
170 Chegue a minha supplica perante a tua face: livra-me segundo a tua palavra.
Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
171 Os meus labios proferiram o louvor, quando me ensinaste os teus estatutos.
Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
172 A minha lingua fallará da tua palavra, pois todos os teus mandamentos são justiça.
Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
173 Venha a tua mão soccorrer-me, pois elegi os teus preceitos.
Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
174 Tenho desejado a tua salvação, ó Senhor, a tua lei é todo o meu prazer.
Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
175 Viva a minha alma, e louvar-te-ha: ajudem-me os teus juizos.
Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
176 Desgarrei-me como a ovelha perdida; busca o teu servo, pois não me esqueci dos teus mandamentos.
Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.