< Provérbios 4 >

1 Ouvi, filhos, a correcção do pae, e estae attentos para conhecerdes a prudencia.
Ananu, mverani malangizo a abambo anu; tcherani khutu kuti mupeze nzeru zodziwira zinthu.
2 Pois dou-vos boa doutrina: não deixeis a minha lei.
Zimene ndikukuphunzitsani ndi zabwino. Choncho musasiye malangizo anga.
3 Porque eu era filho de meu pae: tenro, e unico diante de minha mãe.
Paja ndinalinso mwana mʼnyumba mwa abambo anga; mwana mmodzi yekha wapamtima pa amayi anga.
4 E elle ensinava-me, e dizia-me: Retenha as minhas palavras o teu coração: guarda os meus mandamentos, e vive.
Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti, “Ugwiritse mawu anga pa mtima pako, usunge malamulo anga kuti ukhale ndi moyo.
5 Adquire a sabedoria, adquire a intelligencia, e não te esqueças nem te apartes das palavras da minha bocca.
Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu; usayiwale mawu anga kapena kutayana nawo.
6 Não a desampares, e ella te guardará: ama-a, e ella se te conservará.
Usasiye nzeru ndipo idzakusunga. Uziyikonda ndipo idzakuteteza.
7 O principio da sabedoria é adquirir a sabedoria: adquire pois a sabedoria, e com toda a tua possessão adquire o entendimento.
Fundo yayikulu pa za nzeru ndi iyi: upeze nzeru. Kaya pali china chilichonse chimene ungapeze, koma upeze nzeru yomvetsa bwino zinthu.
8 Exalta-a, e ella te exaltará; e, abraçando-a tu, ella te honrará.
Uyilemekeze nzeruyo ndipo idzakukweza; ikumbatire nzeruyo ndipo idzakupatsa ulemu.
9 Dará á tua cabeça um diadema de graça e uma corôa de gloria te entregará.
Idzayika sangamutu yokongola yamaluwa pamutu pako; idzakupatsa chipewa chaufumu chaulemu.”
10 Ouve, filho meu, e acceita as minhas palavras, e se te multiplicarão os annos de vida.
Mwana wanga, umvere ndi kuvomereza zimene ndikunena, ndipo zaka za moyo wako zidzakhala zochuluka.
11 No caminho da sabedoria te ensinei, e pelas carreiras direitas te fiz andar.
Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru. Ndakutsogolera mʼnjira zolungama.
12 Por ellas andando, não se estreitarão os teus passos; e, se correres, não tropeçarás.
Pamene ukuyenda, mapazi ako sadzawombana; ukamadzathamanga, sudzapunthwa.
13 Pega-te á correcção e não a largues: guarda-a, porque ella é a tua vida
Ugwiritse zimene ndikukuphunzitsazi osazitaya ayi. Uwasamale bwino pakuti moyo wako wagona pamenepa.
14 Não entres na vereda dos impios, nem andes pelo caminho dos maus.
Usayende mʼnjira za anthu oyipa kapena kuyenda mʼnjira ya anthu ochimwa.
15 Rejeita-o; não passes por elle: desvia-te d'elle e passa de largo.
Pewa njira zawo, usayende mʼmenemo; uzilambalala nʼkumangopita.
16 Pois não dormem, se não fizerem mal, e foge d'elles o somno se não fizerem tropeçar alguem.
Pakuti iwo sagona mpaka atachita zoyipa; tulo salipeza mpaka atapunthwitsa munthu wina.
17 Porque comem o pão da impiedade, e bebem o vinho das violencias.
Paja chakudya chawo ndicho kuchita zoyipa basi ndipo chakumwa chawo ndi chiwawa.
18 Porém a vereda dos justos é como a luz resplandecente que vae adiante e alumia até ao dia perfeito.
Koma njira ya anthu olungama ili ngati kuwala kwa mʼbandakucha kumene kumanka kuwalirawalira mpaka dzuwa litafika pa mutu.
19 O caminho dos impios é como a escuridão: nem sabem em que tropeçarão.
Koma njira ya anthu oyipa ili ngati mdima wandiweyani; iwo sadziwa chomwe chimawapunthwitsa.
20 Filho meu, attenta para as minhas palavras: ás minhas razões inclina o teu ouvido.
Mwana wanga, mvetsetsa zimene ndikunena; tchera khutu ku mawu anga.
21 Não as deixes apartar-se dos teus olhos: guarda-as no meio do teu coração.
Usayiwale malangizo angawa, koma uwasunge mu mtima mwako.
22 Porque são vida para os que as acham, e saude para todo o seu corpo.
Pakuti amapatsa moyo kwa aliyense amene awapeza ndipo amachiritsa thupi lake lonse.
23 Sobre tudo o que se deve guardar, guarda o teu coração, porque d'elle procedem as saidas da vida.
Ndipotu mtima wako uziwuyangʼanira bwino ndithu pakuti ndiwo magwero a moyo.
24 Desvia de ti a tortuosidade da bocca, e alonga de ti a perversidade dos beiços.
Usiyiretu kuyankhula zokhotakhota; ndipo ulekeretu kuyankhula zinthu zonyansa.
25 Os teus olhos olhem direitos, e as tuas palpebras olhem directamente diante de ti.
Maso ako ayangʼane patsogolo; uziyangʼana kutsogolo molunjika.
26 Pondera a vereda de teus pés, e todos os teus caminhos sejam bem ordenados!
Uzilingalira bwino kumene kupita mapazi ako ndipo njira zako zonse zidzakhala zosakayikitsa.
27 Não declines nem para a direita nem para a esquerda: retira o teu pé do mal.
Usapatukire kumanja kapena kumanzere; usapite kumene kuli zoyipa.

< Provérbios 4 >