< Provérbios 25 >

1 Tambem estes são proverbios de Salomão, os quaes transcreveram os homens d'Ezequias, rei de Judah.
Iyi ndi miyambo inanso ya Solomoni, imene anthu a Hezekiya mfumu ya ku Yuda analemba.
2 A gloria de Deus é encobrir o negocio; mas a gloria dos reis esquadrinhar o negocio.
Ulemerero wa Mulungu uli pa kubisa zinthu; ulemerero wa mafumu uli pa kufufuza zinthuzo.
3 Para a altura dos céus, e para a profundeza da terra, e para o coração dos reis, não ha investigação.
Monga momwe kwatalikira kumwamba ndi momwe kulili kuzama kwa dziko lapansi, ndi momwemonso alili maganizo a mfumu kusadziwika kwake.
4 Tira da prata as escorias, e sairá vaso para o fundidor.
Chotsa zoyipa mʼsiliva ndipo wosula adzapanga naye ziwiya.
5 Tira o impio da presença do rei, e o seu throno se affirmará na justiça.
Chotsa munthu woyipa pamaso pa mfumu; ndipo ufumu wake udzakhazikika mu chilungamo.
6 Não te glories na presença do rei, nem te ponhas no logar dos grandes;
Usamadzikuze ukakhala pamaso pa mfumu, ndipo usamakhale pamalo pa anthu apamwamba;
7 Porque melhor é que te digam: Sobe aqui; do que seres humilhado diante do principe que já viram os teus olhos.
paja ndi bwino kuti mfumu ichite kukuwuza kuti, “Bwera pamwamba pano,” kulekana ndi kuti ikuchititse manyazi chifukwa cha wina wokuposa. Chimene wachiona ndi maso ako,
8 Não saias depressa a litigar, para que depois ao fim não saibas que fazer, podendo-te confundir o teu proximo.
usafulumire kupita nacho ku bwalo la milandu nanga udzachita chiyani pa mapeto pake ngati mnansi wako adzakuchititsa manyazi?
9 Pleiteia o teu pleito com o teu proximo, e não descubras o segredo d'ontro:
Kamba mlandu ndi mnansi wako, koma osawulula chinsinsi cha munthu wina
10 Para que não te deshonre o que o ouvir, e a tua infamia se não aparte de ti.
kuopa kuti wina akamva mawu ako adzakuchititsa manyazi ndipo mbiri yako yoyipa sidzatha.
11 Como maçãs d'oiro em salvas de prata, assim é a palavra dita a seu tempo.
Mawu amodzi woyankhulidwa moyenera ali ngati zokongoletsera zagolide mʼzotengera zasiliva.
12 Como pendentes d'oiro e gargantilhas d'oiro fino, assim é o sabio reprehensor para o ouvido ouvinte.
Kwa munthu womvetsa bwino, kudzudzula kwa munthu wanzeru kuli ngati ndolo zagolide kapena chodzikongoletsera china cha golide wabwino kwambiri.
13 Como frieza de neve no tempo da sega, assim é o mensageiro fiel para com os que o enviam; porque recreia a alma de seu senhor.
Wamthenga wodalirika ali ngati madzi ozizira pa nthawi yokolola kwa anthu amene amutuma; iye amaziziritsa mtima bwana wake.
14 Como nuvens e ventos que não trazem chuva, assim é o homem que se gaba falsamente de dadivas.
Munthu wonyadira mphatso imene sayipereka ali ngati mitambo ndi mphepo yopanda mvula.
15 Pela longanimidade se persuade o principe, e a lingua branda quebranta os ossos.
Kupirira ndiye kumagonjetsa mfumu, ndipo kufewa mʼkamwa kutha kumafatsitsa munthu wowuma mtima.
16 Achaste mel? come o que te basta; para que porventura não te fartes d'elle, e o venhas a vomitar.
Ngati upeza uchi, ingodya okukwanira, kuopa ungakoledwe nawo ndi kuyamba kusanza.
17 Retira o teu pé da casa do teu proximo; para que se não enfade de ti, e te aborreça.
Uzipita kamodzikamodzi ku nyumba ya mnzako ukawirikiza kupita, udzadana naye.
18 Martello, e espada, e frecha aguda é o homem que diz falso testemunho contra o seu proximo.
Munthu wochitira mnzake umboni wonama, ali ngati chibonga kapena lupanga kapena muvi wakuthwa.
19 Como dente quebrado, e pé desengonçado, é a confiança no desleal, no tempo da angustia.
Kudalira munthu wosankhulupirika pa nthawi ya mavuto, kuli ngati dzino lobowoka kapena phazi lolumala.
20 O que canta canções ao coração afflicto é como aquelle que despe o vestido n'um dia de frio, e como vinagre sobre salitre.
Kuyimbira nyimbo munthu wachisoni kuli ngati kuvula zovala pa nyengo yozizira kapena kuthira mchere pa chilonda.
21 Se o que te aborrece tiver fome, dá-lhe pão para comer; e se tiver sêde, dá-lhe agua para beber;
Ngati mdani wako ali ndi njala, mupatse chakudya kuti adye; ngati ali ndi ludzu mupatse madzi kuti amwe.
22 Porque assim brazas lhe amontoarás sobre a cabeça; e o Senhor t'o pagará.
Pochita izi, udzamusenzetsa makala a moto pa mutu pake, ndipo Yehova adzakupatsa mphotho.
23 O vento norte afugenta a chuva, e a face irada a lingua fingida.
Monga momwe mphepo yampoto imabweretsera mvula, chonchonso mjedu umadzetsa mkwiyo.
24 Melhor é morar n'um canto do terraço, do que com a mulher contenciosa, e isso em casa em que mais companhia haja.
Nʼkwabwino kukhala pa ngodya ya denga kuposa kukhala mʼnyumba ndi mkazi wolongolola.
25 Como agua fria á alma cançada, taes são as boas novas de terra remota.
Mthenga wabwino wochokera ku dziko lakutali ali ngati madzi ozizira kwa munthu waludzu.
26 Como fonte turva, e manancial corrupto, assim é o justo que cae diante do impio.
Munthu wolungama amene amagonjera munthu woyipa ali ngati kasupe wodzaza ndi matope kapena chitsime cha madzi oyipa.
27 Comer muito mel não é bom; assim a pesquiza da propria gloria não é gloria.
Sibwino kudya uchi wambiri, sibwinonso kudzifunira wekha ulemu.
28 Como a cidade derribada, sem muro, assim é o homem que não pode conter o seu espirito.
Munthu amene samatha kudziretsa ali ngati mzinda umene adani awuthyola ndi kuwusiya wopanda malinga.

< Provérbios 25 >