< Provérbios 22 >
1 Mais digno de ser escolhido é o bom nome do que as muitas riquezas; e a graça é melhor do que a riqueza e o oiro.
Mbiri yabwino ndi yofunika kuposa chuma chambiri; kupeza kuyanja nʼkwabwino kuposa siliva kapena golide.
2 O rico e o pobre se encontraram: a todos os fez o Senhor.
Wolemera ndi wosauka ndi ofanana; onsewa anawalenga ndi Yehova.
3 O avisado vê o mal, e esconde-se; mas os simples passam, e pagam a pena.
Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amadzanongʼoneza bondo.
4 O galardão da humildade com o temor do Senhor são riquezas, a honra e a vida.
Mphotho ya munthu wodzichepetsa ndi woopa Yehova ndi chuma, ulemu ndi moyo.
5 Espinhos e laços ha no caminho do perverso: o que guarda a sua alma retira-se para longe d'elle.
Mʼnjira za anthu oyipa muli minga ndi misampha, koma amene amasala moyo wake adzazipewa zonsezo.
6 Instrue ao menino conforme o seu caminho; e até quando envelhecer não se desviará d'elle.
Mwana muzimuphunzitsa njira yake, ndipo akadzakalamba sadzachokamo.
7 O rico domina sobre os pobres, e o que toma emprestado servo é do que empresta.
Wolemera amalamulira wosauka, ndipo wokongola zinthu amakhala kapolo wa womukongozayo.
8 O que semear a perversidade segará males; e a vara da sua indignação se acabará.
Amene amafesa zoyipa amakolola mavuto, ndipo ndodo yaukali wake idzathyoka.
9 O que é de bons olhos será abençoado, porque deu do seu pão ao pobre.
Amene ali ndi diso lachifundo adzadalitsika, pakuti iye amagawana chakudya chake ndi anthu osauka.
10 Lança fóra ao escarnecedor, e se irá a contenda; e cessará o pleito e a vergonha.
Chotsani munthu wonyoza, ndipo kukangana kudzatha; mapokoso ndi zonyoza zidzaleka.
11 O que ama a pureza do coração, e tem graça nos seus labios, seu amigo será o rei
Amene amakonda kukhala woyera mtima ndi kumayankhula mawu abwino, adzakhala bwenzi la mfumu.
12 Os olhos do Senhor conservam o conhecimento, mas as palavras do iniquo transtornará.
Maso a Yehova amakhala pa anthu odziwa bwino zinthu, koma Iye adzalepheretsa mawu a anthu osakhulupirika.
13 Diz o preguiçoso: Um leão está lá fóra; serei morto no meio das ruas
Munthu waulesi amati, “Kunjaku kuli mkango. Ine ndidzaphedwa mʼmisewu!”
14 Cova profunda é a bocca das mulheres estranhas; aquelle contra quem o Senhor se irar, cairá n'ella.
Pakamwa pa mkazi wachigololo pali ngati dzenje lozama; amene Yehova wamukwiyira adzagwamo.
15 A estulticia está ligada no coração do menino, mas a vara da correcção a afugentará d'elle.
Uchitsiru umakhala mu mtima mwa mwana, koma ndodo yomulangira mwanayo idzachotsa uchitsiruwo.
16 O que opprime ao pobre para se engrandecer a si, ou o que dá ao rico, certamente empobrecerá.
Amene amapondereza anthu osauka kuti awonjezere chuma chake, ndiponso amene amapereka mphatso kwa anthu olemera onsewa adzasauka.
17 Inclina a tua orelha, e ouve as palavras dos sabios, e applica o teu coração á minha sciencia.
Utchere khutu lako ndipo umvere mawu anzeru; uyike mtima wako pa zimene ndikukuphunzitsa kuti udziwe.
18 Porque é coisa suave, se as guardares nas tuas entranhas, se applicares todas ellas aos teus labios.
Zidzakhala zokondweretsa ngati uzisunga mu mtima mwako ndi wokonzeka kuziyankhula.
19 Para que a tua confiança esteja no Senhor: a ti t'as faço saber hoje; tu tambem a outros as faze saber.
Ndakuphunzitsa zimenezi lero koma makamaka uziopa Yehova.
20 Porventura não te escrevi excellentes coisas, ácerca de todo o conselho e conhecimento?
Kodi suja ndinakulembera malangizo makumi atatu okuchenjeza ndi okupatsa nzeru,
21 Para fazer-te saber a certeza das palavras da verdade, para que possas responder palavras de verdade aos que te enviarem.
malangizo okudziwitsa zolungama ndi zoona ndi kuti ukawayankhe zoona amene akutumawo?
22 Não roubes ao pobre, porque é pobre, nem atropelles na porta ao afflicto.
Mʼmphawi usamubere chifukwa ndi osauka, ndipo usawapondereze anthu osowa mʼbwalo la milandu,
23 Porque o Senhor defenderá a sua causa em juizo, e aos que os roubam lhes roubará a alma.
pakuti Yehova adzawateteza pa mlandu wawo ndipo adzalanda moyo onse amene amawalanda iwo.
24 Não acompanhes com o iracundo, nem andes com o homem colerico.
Usapalane naye ubwenzi munthu wosachedwa kupsa mtima ndipo usayanjane ndi munthu amene sachedwa kukwiya
25 Para que não aprendas as suas veredas, e tomes um laço para a tua alma.
kuopa kuti iwe ungadzaphunzire njira zake ndi kukodwa mu msampha.
26 Não estejas entre os que dão a mão, e entre os que ficam por fiadores de dividas.
Usakhale munthu wopereka chikole kapena kukhala mboni pa ngongole;
27 Se não tens com que pagar, porque tirariam a tua cama de debaixo de ti?
ngati ulephera kupeza njira yolipirira adzakulanda ngakhale bedi lako lomwe.
28 Não removas os limites antigos que fizeram teus paes.
Usasunthe mwala wamʼmalire akalekale amene anayikidwa ndi makolo ako.
29 Viste a um homem ligeiro na sua obra? perante reis será posto: não será posto perante os de baixa sorte.
Kodi ukumuona munthu waluso pa ntchito yake? Iye adzatumikira mafumu; sadzatumikira anthu wamba.