< Marcos 16 >
1 E, passado o sabbado, Maria Magdalena, e Maria, mãe de Thiago, e Salomé, compraram aromas para irem ungil-o.
Litapita tsiku la Sabata, Mariya Magadalena, ndi amayi ake a Yakobo, ndi Salome anagula zonunkhiritsa ndi cholinga chakuti apite akadzoze thupi la Yesu.
2 E, no primeiro dia da semana, foram ao sepulchro, de manhã cedo, ao nascer do sol;
Mmamawa, tsiku loyamba la Sabata, dzuwa litangotuluka kumene, anali pa ulendo wopita ku manda
3 E diziam umas ás outras: Quem nos revolverá a pedra da porta do sepulchro?
ndipo anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Kodi akatikugudubuzira mwala pa khomo la manda ndani?”
4 E, olhando, viram que já a pedra estava revolvida; porque era muito grande.
Koma atakweza maso awo, anaona kuti mwala umene unali waukulu kwambiri wagubuduzidwa kale.
5 E, entrando no sepulchro, viram um mancebo assentado á direita, vestido de uma roupa comprida, branca; e ficaram espantadas.
Atalowa mʼmanda, anaona mnyamata atavala mwinjiro woyera atakhala ku mbali ya kumanja, ndipo iwo anachita mantha.
6 Porém elle disse-lhes: Não vos assusteis; buscaes a Jesus Nazareno, que foi crucificado; já resuscitou, não está aqui; eis aqui o logar onde o pozeram.
Iye anati, “Musaope. Kodi mukufuna Yesu wa ku Nazareti, amene anapachikidwa? Wauka! Sali muno. Onani malo amene anamugonekapo.
7 Porém ide, dizei a seus discipulos, e a Pedro, que elle vae adiante de vós para a Galilea; ali o vereis, como elle vos disse.
Koma pitani, kawuzeni ophunzira ake ndi Petro kuti, ‘Iye watsogola kupita ku Galileya. Kumeneko mukamuona Iye monga momwe anakuwuzirani.’”
8 E, saindo ellas apressadamente, fugiram do sepulchro, porque estavam possuidas de temor e assombro; e nada diziam a ninguem, porque temiam.
Akunjenjemera ndi kudabwa, amayiwo anatuluka ndipo anathawa ku mandako. Sananene china chilichonse kwa aliyense, chifukwa anachita mantha.
9 (note: The most reliable and earliest manuscripts do not include Mark 16:9-20.) E Jesus, tendo resuscitado na manhã do primeiro dia da semana, appareceu primeiramente a Maria Magdalena, da qual tinha expulsado sete demonios.
(note: The most reliable and earliest manuscripts do not include Mark 16:9-20.) Yesu atauka kwa akufa mmawa pa tsiku loyamba la Sabata, anayamba kuonekera kwa Mariya Magadalena, amene anatulutsa mwa iye ziwanda zisanu ndi ziwiri.
10 E, partindo ella, annunciou-o áquelles que tinham estado com elle, os quaes estavam tristes, e chorando.
Iye anapita ndi kukawawuza amene anali ndi Yesu, amene ankakhuza maliro ndi kulira.
11 E, ouvindo elles que vivia, e que tinha sido visto por ella, não o creram.
Atamva kuti Yesu ali moyo ndikuti amuona, iwo sanakhulupirire.
12 E depois manifestou-se n'outra fórma a dois d'elles, que iam de caminho para o campo.
Zitatha izi Yesu anaonekera mʼmaonekedwe ena kwa awiri a iwo amene anali ku dera la ku mudzi.
13 E, indo estes, annunciaram-n'o aos outros, mas nem ainda estes creram.
Iwo anabwerera ndi kudzawawuza enawo; koma iwo sanakhulupirirebe.
14 Finalmente appareceu aos onze, estando elles assentados juntamente, e lançou-lhes em rosto a sua incredulidade e dureza de coração, por não haverem crido nos que o tinham visto já resuscitado.
Pambuyo pake Yesu anaonekera kwa khumi ndi mmodziwo pamene ankadya; anawadzudzula chifukwa chopanda chikhulupiriro ndi kukanitsitsa kwawo kuti akhulupirire amene anamuona Iye atauka.
15 E disse-lhes: Ide por todo o mundo, prégae o evangelho a toda a creatura:
Anati kwa iwo, “Pitani mʼdziko lonse lapansi ndipo mukalalikire Uthenga Wabwino kwa zolengedwa zonse.
16 Quem crêr e fôr baptizado será salvo; mas quem não crêr será condemnado.
Aliyense amene akakhulupirire nabatizidwa adzapulumuka, koma amene sakakhulupirira adzalangidwa.
17 E estes signaes seguirão aos que crêrem: Em meu nome expulsarão os demonios; fallarão novas linguas:
Tsono zizindikiro izi zidzawatsata amene adzakhulupirira: Mʼdzina langa adzatulutsa ziwanda; adzayankhula malilime atsopano;
18 Pegarão nas serpentes; e, se beberem alguma coisa mortifera, não lhes fará damno algum; e porão as mãos sobre os enfermos, e os sararão.
adzanyamula njoka ndi manja awo; ndipo pamene adzamwa mankhwala akupha, sadzawapweteka nʼpangʼonongʼono pomwe; adzasanjika manja awo pa anthu odwala ndipo odwalawo adzachira.”
19 Ora o Senhor, depois de lhes ter fallado, foi recebido acima no céu, e assentou-se á direita de Deus.
Ambuye Yesu atatha kuyankhulana nawo, anatengedwa kupita kumwamba ndipo anakhala kudzanja lamanja la Mulungu.
20 E elles, tendo partido, prégaram por todas as partes, cooperando com elles o Senhor, e confirmando a palavra com os signaes que se seguiram. Amen.
Pamenepo ophunzira aja anapita ndi kukalalikira ponseponse, ndipo Ambuye anagwira nawo ntchito pamodzi, ndipo anatsimikizira mawuwo ndi zizindikiro zimene ankachita.