< 39 >

1 Sabes tu o tempo em que as cabras montezes parem? ou consideraste as dôres das cervas?
“Kodi iwe umadziwa nthawi imene mbalale yayikazi imaswera? Kodi umaonerera pamene nswala ikubala?
2 Contarás os mezes que cumprem? ou sabes o tempo do seu parto?
Kodi umawerenga miyezi imene zimakhala ndi bere? Kodi nthawi imene zimaswana iwe umayidziwa?
3 Quando se encurvam, produzem seus filhos, e lançam de si as suas dôres.
Zimakhala tsonga ndi kuswa ana awo; pamenepo ululu wobereka nʼkutha.
4 Seus filhos enrijam, crescem com o trigo: saem, e nunca mais tornam a ellas.
Ana a nyamazi amakhala ndi mphamvu ndipo amakulira mʼthengo; kenaka amachoka ndipo sabwereranso.
5 Quem despediu livre o jumento montez? e quem soltou as prisões ao jumento bravo?
“Kodi bulu wakuthengo amamupatsa ndani ufulu wongodziyendera? Ndani amamasula zingwe zake?
6 Ao qual dei o ermo por casa, e a terra salgada por suas moradas.
Ine ndinamupatsa chipululu kuti chikhale mudzi wake, nthaka ya mchere kuti ikhale malo ake okhalamo
7 Ri-se do arroido da cidade: não ouve os muitos gritos do exactor.
Iye amakhala kutali ndi phokoso la mu mzinda; ndipo samva kufuwula kwa oyendetsa nyama zakatundu.
8 O que descobre nos montes é o seu pasto, e anda buscando tudo que está verde.
Amayendayenda mʼmapiri kudya msipu ndipo amafunafuna msipu uliwonse wobiriwira.
9 Ou, querer-te-ha servir o unicornio? ou ficará na tua cavallariça?
“Kodi njati ingavomere kukutumikira? Kodi ingagone mu gome lako usiku?
10 Ou amarrarás o unicornio com a sua corda no rego? ou estorroará apoz ti os valles?
Kodi ungathe kuyimanga ndi zingwe kuti izilima? Kodi ingasalaze nthumbira mʼmunda mwako?
11 Ou confiarás n'elle, por ser grande a sua força? ou deixarás a seu cargo o teu trabalho?
Kodi ungadalire njatiyo chifukwa champhamvu zake? Kodi ungayilekere kuti igwire ntchito zako zolemetsa?
12 Ou fiarás d'elle que te torne o que semeaste e o recolherá na tua eira?
Kodi ungadalire kuti idzakubweretsera tirigu wako ndi kumuyika ku malo opunthira?
13 Vem de ti as alegres azas dos pavões, que teem pennas de cegonha e d'aguia?
“Nthiwatiwa imakupiza mapiko ake monyadira, koma mapikowo sangafanane ndi mapiko ndi nthenga za kakowa.
14 A qual deixa os seus ovos na terra, e os aquenta no pó.
Nthiwatiwa imakwirira mazira ake pansi ndipo amafundidwa ndi nthaka,
15 E se esquece de que algum pé os pise, ou os animaes do campo os calquem.
nthiwatiwayo sidera nkhawa kuti mazira ake angathe kuswanyidwa, ndi kuti nyama zakuthengo zitha kuwaponda.
16 Endurece-se para com seus filhos, como se não fossem seus: debalde é seu trabalho, porquanto está sem temor.
Nthiwatiwa imachitira nkhanza ana ake ngati anawo si ake; Imayiwala zoti inavutika powabala.
17 Porque Deus a privou de sabedoria, e não lhe repartiu entendimento.
Chifukwa Mulungu anayimana nzeru, simvetsa kanthu kalikonse.
18 A seu tempo se levanta ao alto: ri-se do cavallo, e do que vae montado n'elle.
Komatu nthiwatiwa ikadzambatuka ndi kuyamba kuthamanga, imamusiya kutali kavalo ndi wokwerapo wake.
19 Ou darás tu força ao cavallo? ou vestirás o seu pescoço com trovão?
“Kodi ndiwe amene umamupatsa mphamvu kavalo kapena kumuveka chenjerere mʼkhosi mwake?
20 Ou espantal-o-has, como ao gafanhoto? terrivel é o fogoso respirar das suas ventas.
Kodi ndiwe amene umalipatsa dzombe ulemerero wolumphira, ukali wake nʼkumachititsa mantha?
21 Escarva a terra, e folga na sua força, e sae ao encontro dos armados.
Iye amalumphalumpha moopseza, kukondwerera mphamvu zake, ndipo amapita ku nkhondo ndi mphamvu zake zonse.
22 Ri-se do temor, e não se espanta, e não torna atraz por causa da espada.
Iye sachita mantha, saopa chilichonse; sabwerera mʼmbuyo akaona lupanga.
23 Contra elle rangem a aljava, o ferro flammante da lança e do dardo.
Zida zankhondo zimachita kwichikwichi mʼchimake pambali pake pamodzi ndi mkondo wonyezimira ndi nthungo.
24 Sacudindo-se, e removendo-se, escarva a terra, e não faz caso do som da buzina.
Kavaloyo amanjenjemera ndi ukali ndi kulumphalumpha; satha kungoyima pamene wamva kulira kwa lipenga.
25 Na furia do som das buzinas diz: Eia! e de longe cheira a guerra, e o trovão dos principes, e o alarido.
Lipenga likalira amati, ‘Twee!’ Amamva fungo la nkhondo ali patali, kufuwula kwa anthu olamulira nkhondo ndi mfuwu wankhondo.
26 Ou vôa o gavião pela tua intelligencia, e estende as suas azas para o sul?
“Kodi kabawi amawuluka ndi nzeru zako, ndi kutambasula mapiko ake kupita kummwera?
27 Ou se remonta a aguia ao teu mandado, e põe no alto o seu ninho?
Kodi umalamulira chiwombankhanga ndiwe kuti chiziwuluka ndi kumanga chisa chake pamwamba penipeni?
28 Nas penhas mora e habita: no cume das penhas, e nos logares seguros.
Chimakhala pa phiri ndipo chimakhala pamenepo usiku; chimakhala pa msonga penipeni pa mwala.
29 Desde ali descobre a preza: seus olhos a avistam desde longe.
Chili pamenepo chimayangʼanayangʼana choti chigwire kuti chidye; maso ake amachionera patali chinthucho.
30 E seus filhos chupam o sangue, e onde ha mortos ahi está.
Ana ake amayamwa magazi, ndipo kumene kuli mitembo ndiko chimapezeka.”

< 39 >