< 22 >

1 Então respondeu Eliphaz o temanita, e disse:
Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
2 Porventura o homem será d'algum proveito a Deus? antes a si mesmo o prudente será proveitoso.
“Kodi munthu nʼkukhala waphindu kwa Mulungu? Kodi munthu wanzeru angamupindulire Iye?
3 Ou tem o Todo-poderoso prazer em que tu sejas justo? ou lucro algum que tu faças perfeitos os teus caminhos?
Kodi Wamphamvuzonse akanapeza chabwino chotani iweyo ukanakhala wolungama? Kodi iyeyo akanapeza phindu lanji makhalidwe ako akanakhala angwiro?
4 Ou te reprehende, pelo temor que tem de ti? ou entra comtigo em juizo?
“Kodi nʼchifukwa choti umamuopa, kuti azikudzudzula, kuti azifuna kukukokera ku mlandu?
5 Porventura não é grande a tua malicia? e sem termo as tuas iniquidades?
Kodi osati nʼchifukwa chakuti kuyipa kwako nʼkwakukulu? Kodi machimo ako si opanda malire?
6 Porque penhoraste a teus irmãos sem causa alguma, e aos nus despiste os vestidos.
Iwe unkawumiriza abale ako kuti akupatse chikole popanda chifukwa; umalanda anthu zovala zawo ndi kuwasiya amaliseche.
7 Não déste de beber agua ao cançado, e ao faminto retiveste o pão.
Sunawapatse madzi anthu otopa, ndipo unawamana chakudya anthu anjala,
8 Mas para o violento era a terra, e o homem tido em respeito habitava n'ella.
ngakhale unali munthu wamphamvu, wokhala ndi malo akeake, munthu waulemu wake, wokhala mʼdzikomo.
9 As viuvas despediste vazias, e os braços dos orphãos foram quebrantados.
Ndipo akazi amasiye unawachotsa wopanda kanthu, ndipo unapondereza ana amasiye.
10 Por isso é que estás cercado de laços, e te perturbou um pavor repentino,
Nʼchifukwa chake misampha yakuzungulira, nʼchifukwa chake tsoka ladzidzidzi lakuchititsa mantha,
11 Ou as trevas que não vês, e a abundancia d'agua que te cobre.
nʼchifukwa chake kuli mdima kuti sungathe kuona kanthu, nʼchifukwa chakenso madzi achigumula akumiza.
12 Porventura Deus não está na altura dos céus? olha pois para o cume das estrellas, quão levantadas estão.
“Kodi Mulungu sali kutalitali kumwamba? Ndipo ona nyenyezi zili mmwamba kwambirizo, ona kutalika kwake pamene zililipo!
13 E dizes que sabe Deus d'isto? porventura julgará por entre a escuridão?
Komabe iweyo ukunena kuti, ‘Kodi Mulungu amadziwa chiyani? Kodi Iye amaweruza mu mdima woterewu?
14 As nuvens são escondedura para elle, para que não veja: e passeia pelo circuito dos céus.
Mitambo yakuda yamuphimba, kotero kuti Iye sakutiona pamene akuyendayenda pamwamba pa thambopo.’
15 Porventura consideraste a vereda do seculo passado, que pisaram os homens iniquos?
Kodi iwe udzayendabe mʼnjira yakale imene anthu oyipa ankayendamo?
16 Os quaes foram arrebatados antes do seu tempo: sobre cujo fundamento um diluvio se derramou.
Iwo anachotsedwa nthawi yawo isanakwane, maziko awo anakokoloka ndi madzi achigumula.
17 Diziam a Deus: Retira-te de nós. E que é o que o Todo-poderoso lhes fez?
Anthuwo anati kwa Mulungu, ‘Tichokereni! Kodi Wamphamvuzonse angatichitire chiyani?’
18 Sendo elle o que enchera de bens as suas casas: mas o conselho dos impios esteja longe de mim.
Chonsecho ndi Iye amene anadzaza nyumba zawo ndi zinthu zabwino, choncho ine sindigwirizana ndi uphungu wa anthu oyipa.
19 Os justos o viram, e se alegravam, e o innocente escarneceu d'elles.
“Anthu olungama amaona kuwonongeka kwawo ndipo amakondwera; anthu osalakwa amangoseka, akamuona woyipa akulangidwa.
20 Porquanto o nosso estado não foi destruido, mas o fogo consumiu o resto d'elles.
Amanena kuti, ‘Ndithudi adani athu awonongeka ndipo moto wawononga chuma chawo!’
21 Acostuma-te pois a elle, e tem paz, e assim te sobrevirá o bem.
“Gonjera Mulungu kuti ukhale naye pamtendere; ukatero udzaona zabwino.
22 Acceita, peço-te, a lei da sua bocca, e põe as suas palavras no teu coração.
Landira malangizo a pakamwa pake ndipo usunge mawu ake mu mtima mwako.
23 Se te converteres ao Todo-poderoso, serás edificado: affasta a iniquidade da tua tenda.
Ukabwerera kwa Wamphamvuzonse udzabwezeretsedwa; ukachotsa zoyipa zonse zimene zimachitika mʼnyumba mwako,
24 Então amontoarás oiro como pó, e o oiro d'Ophir como pedras dos ribeiros.
ndipo chuma chamtengowapatali nuchiona ngati fumbi, golide wa ku Ofiri numutaya ku miyala ya ku zigwa.
25 E até o Todo-poderoso te será por oiro, e a tua prata amontoada.
Pamenepo Wamphamvuzonseyo adzakhala golide wako, siliva wako wamtengowapatali.
26 Porque então te deleitarás no Todo-poderoso, e levantarás o teu rosto para Deus.
Pamenepo udzakondwera naye Wamphamvuzonse ndipo udzakweza nkhope yako kwa Mulungu.
27 Devéras orarás, a elle, e elle te ouvirá, e pagarás os teus votos.
Udzamupempha ndipo adzakumvera, ndipo udzapereka zimene unalonjeza.
28 Determinando tu algum negocio, ser-te-ha firme, e a luz brilhará em teus caminhos.
Chimene watsimikiza kuti uchite, chidzachitikadi, kuwala kudzakuwunikira pa njira yako.
29 Quando abaterem, então tu dirás: Haja exaltação: e Deus salvará ao humilde.
Pamene anthu agwetsedwa pansi, iwe nʼkunena kuti, ‘Akwezeni!’ Pamenepo Iye adzapulumutsa anthu oponderezedwa.
30 E livrará até ao que não é innocente; porque fica livre pela pureza de tuas mãos.
Iye adzapulumutsa ngakhale munthu amene ndi wolakwa, ameneyo adzapulumutsidwa kudzera mʼkulungama kwako.”

< 22 >