< 12 >

1 Então Job respondeu, e disse:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 Na verdade, que só vós sois o povo, e comvosco morrerá a sabedoria.
“Ndithudi inuyo ndinu anthu ndipo nzeru zanu zidzafera nanu pamodzi!
3 Tambem eu tenho um coração como vós, e não vos sou inferior: e quem não sabe taes coisas como estas?
Koma inenso ndili nazo nzeru ngati inu; ineyo sindine munthu wamba kwa inu. Ndani amene sadziwa zonse zimene mwanenazi?
4 Eu sou irrisão aos meus amigos; eu, que invoco a Deus, e elle me responde; o justo e o recto servem de irrisão.
“Ndasanduka chinthu choseketsa kwa abwenzi anga, ngakhale ndinkapemphera kwa Mulungu ndipo Iye ankandiyankha. Ine ndasanduka chinthu chongoseketsa, ngakhale ndili wolungama ndi wosalakwa!
5 Tocha desprezivel é na opinião do que está descançado, aquelle que está prompto a tropeçar com os pés.
Anthu amene ali pabwino amanyoza anzawo amene ali pa tsoka. Tsokalo limagwa pa amene wayamba kale kugwa.
6 As tendas dos assoladores teem descanço, e os que provocam a Deus estão seguros; nas suas mãos Deus lhes põe tudo.
Nyumba za anthu achifwamba zimakhala pa mtendere, ndipo anthu amene amaputa Mulungu amakhala pabwino, amene amanyamula milungu yawo mʼmanja.
7 Mas, pergunta agora ás bestas, e cada uma d'ellas t'o ensinará: e ás aves dos céus, e ellas t'o farão saber;
“Koma funsa nyama zakuthengo ndipo zidzakuphunzitsa, kapena mbalame zamumlengalenga ndipo zidzakuwuza;
8 Ou falla com a terra, e ella t'o ensinará: até os peixes do mar t'o contarão.
kapena uyankhule ndi dziko lapansi ndipo lidzakuphunzitsa, kapena ulole nsomba zamʼnyanja kuti zikufotokozere.
9 Quem não entende por todas estas coisas que a mão do Senhor faz isto?
Kodi mwa zonsezi ndi chiti chimene sichidziwa kuti lachita zimenezi ndi dzanja la Yehova?
10 Em cuja mão está a alma de tudo quanto vive, e o espirito de toda a carne humana.
Mʼmanja mwake ndi mʼmene muli moyo wa cholengedwa chilichonse, ndiponso moyo wa anthu a mitundu yonse.
11 Porventura o ouvido não provará as palavras, como o paladar gosta as comidas?
Kodi khutu sindiye limene limamva mawu monga mmene lilime limalawira chakudya?
12 Com os edosos está a sabedoria, e na longura de dias o entendimento.
Kodi nzeru sipezeka pakati pa anthu okalamba? Kodi moyo wautali sumabweretsa nzeru zomvetsa zinthu?
13 Com elle está a sabedoria e a força: conselho e entendimento tem.
“Kwa Mulungu ndiye kuli nzeru ndi mphamvu; uphungu ndi kumvetsa zinthu ndi zake.
14 Eis que elle derriba, e não se reedificará: encerra o homem, e não se lhe abrirá.
Chimene Iye wapasula palibe angachimangenso. Akatsekera munthu mʼndende palibe angamutulutse.
15 Eis que elle retem as aguas, e se seccam; e as larga, e transtornam a terra.
Iyeyo akamanga mvula dziko limawuma; akamasula mvulayo, madzi amasefukira pa dziko.
16 Com elle está a força e a sabedoria: seu é o errante e o que o faz errar.
Kwa Iye kuli mphamvu ndi kupambana; munthu wopusitsidwa ndiponso wopusitsa onse ali mu ulamuliro wake.
17 Aos conselheiros leva despojados, e aos juizes faz desvairar.
Iye amalanda aphungu nzeru zawo ndipo amapusitsa oweruza.
18 Solta a atadura dos reis, e ata o cinto aos seus lombos.
Iye amachotsa zingwe zimene mafumu anawamanga nazo ndipo amawamanga lamba mʼchiwuno mwawo.
19 Aos principes leva despojados, aos poderosos transtorna.
Iye amasocheretsa ansembe atawalanda nzeru zawo ndipo amagonjetsa anthu amphamvu amene ndi okhazikika.
20 Aos acreditados tira a falla, e toma o entendimento aos velhos.
Iye amakhalitsa chete aphungu odalirika ndipo amalanda chidziwitso cha anthu akuluakulu.
21 Derrama desprezo sobre os principes, e affrouxa o cinto dos violentos.
Iye amanyoza anthu otchuka ndipo anthu anyonga amawatha mphamvu.
22 As profundezas das trevas manifesta, e a sombra da morte traz á luz.
Iye amatulutsira poyera zinthu zozama za mu mdima ndipo mdima wandiweyaniwo amawusandutsa kuwala.
23 Multiplica as gentes e as faz perecer; espalha as gentes, e as guia.
Iye amakuza mitundu ya anthu ndipo amayiwononganso; amachulukitsa mitundu ya anthu ndipo amayimwazanso.
24 Tira o coração aos chefes das gentes da terra, e os faz vaguear pelos desertos, sem caminho.
Iye amalanda nzeru za atsogoleri a dziko lapansi; amawayendetsa mʼthengo mopanda njira.
25 Nas trevas andam ás apalpadelas, sem terem luz, e os faz desatinar como ebrios.
Iwo amafufuzafufuza njira mu mdima wopanda chowunikira; Iye amawayendetsa dzandidzandi ngati oledzera.

< 12 >