< Jeremias 16 >

1 E veiu a mim a palavra do Senhor, dizendo:
Kenaka Yehova anandiwuza kuti,
2 Não tomarás para ti mulher, nem terás filhos nem filhas n'este logar.
“Usadzakwatire ndi kubereka ana aamuna kapena aakazi malo ano
3 Porque assim diz o Senhor, ácerca dos filhos e das filhas que nascerem n'este logar, ácerca de suas mães, que os parirem, e de seus paes que os gerarem n'esta terra:
pakuti ana aamuna ndi ana aakazi obadwira mʼdziko muno, komanso amayi awo ndi abambo awo amene anabereka anawo mʼdziko muno,
4 Morrerão de enfermidades dolorosas, e não serão pranteados nem sepultados: servirão d'esterco sobre a terra; e pela espada e pela fome serão consumidos, e os seus cadaveres servirão de mantimento para as aves do céu e para os animaes da terra.
adzafa ndi nthenda zoopsa. Sadzawalira maliro kapena kuyikidwa mʼmanda koma adzakhala ngati ndowe zotayikira pansi. Ena adzaphedwa ku nkhondo ndipo ena adzafa ndi njala. Mitembo yawo idzakhala chakudya cha mbalame zamlengalenga ndi zirombo zakuthengo.”
5 Porque assim diz o Senhor: Não entres na casa do luto, nem vás a lamentar, nem te compadeças d'elles; porque já d'este povo, diz o Senhor, tirei a minha paz, benignidade e misericordia.
Yehova akuti, “Usalowe mʼnyumba ya maliro; usapite kukalira maliro kapena kukapepesa, chifukwa Ine ndawachotsera madalitso anga, chikondi changa ndi chifundo changa.”
6 E morrerão grandes e pequenos n'esta terra, e não serão sepultados, e não os prantearão nem se farão por elles incisões, nem por elles se raparão os cabellos.
Akuluakulu ndi angʼonoangʼono omwe adzafa mʼdziko muno. Sadzayikidwa mʼmanda kapena kuliridwa, ndipo palibe amene adzaonetse chisoni podzichekacheka kapena kumeta tsitsi lake chifukwa cha iwo.
7 E nada se lhes repartirá por dó, para consolal-os por causa de morte: nem lhes darão a beber do copo de consolação, nem por pae de alguem, nem por mãe de alguem.
Palibe amene adzapereka chakudya kutonthoza amene akulira maliro, ngakhale kuti womwalirayo ndi abambo ake kapena amayi ake.
8 Nem entres na casa do banquete, para te assentares com elles a comer e a beber.
“Ndipo usalowe mʼnyumba mmene muli madyerero, nʼkukhala pansi ndi kudya ndi kumwa nawo.
9 Porque assim diz o Senhor dos Exercitos, o Deus d'Israel: Eis que farei cessar d'este logar perante os vossos olhos, e em vossos dias, a voz de gozo e a voz de alegria, a voz do esposo e a voz da esposa.
Pakuti Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akunena kuti, ‘Pa nthawi yanu, inu mukuona ndidzathetsa mawu achimwemwe ndi achisangalalo ndiponso mawu a mkwati ndi mkwatibwi pa malo ano.’
10 E será que, quando annunciares a este povo todas estas palavras, e elles te disserem: Porque falla o Senhor sobre nós todo este grande mal? e qual é a nossa iniquidade, e qual é o nosso peccado, que peccámos contra o Senhor nosso Deus
“Ukawawuza anthu awa zinthu zonsezi akakufunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani Yehova wanena kuti tsoka lalikulu lotere lidzatigwere? Kodi talakwa chiyani? Kodi tamuchimwira tchimo lotani Yehova Mulungu wathu?’
11 Então lhes dirás: Porquanto vossos paes me deixaram, diz o Senhor, e se foram após deuses alheios, e os serviram, e se inclinaram diante d'elles, e a mim me deixaram, e a minha lei não a guardaram.
Pamenepo ukawawuze kuti, ‘Nʼchifukwa chakuti makolo anu anandisiya Ine,’ akutero Yehova, ‘ndi kutsatira milungu ina, kuyitumikira ndi kuyipembedza. Iwo anandisiya Ine ndipo sanasunge lamulo langa.
12 E vós fizestes peior do que vossos paes; porque, eis que cada um de vós anda após o proposito do seu malvado coração, para me não dar ouvidos a mim
Komanso inu munachimwa kwambiri kupambana makolo anu. Aliyense wa inu akutsatira zoyipa ndi mtima wake wokanikawo mʼmalo mondimvera Ine.
13 E lançar-vos-hei fóra d'esta terra, para uma terra que não conhecestes, nem vós nem vossos paes; e ali servireis a deuses alheios de dia e de noite, porque não usarei de misericordia comvosco.
Choncho Ine ndidzakubalalitsani mʼdziko muno ndi kukulowetsani mʼdziko limene inu ndi makolo anu simunalidziwe. Kumeneko mukatumikira milungu ina usana ndi usiku, ndipo sadzakuchitirani chifundo.’”
14 Portanto, eis que dias veem, diz o Senhor, em que nunca mais se dirá: Vive o Senhor, que fez subir os filhos d'Israel da terra do Egypto.
Yehova akuti, “Komabe masiku akubwera pamene anthu polumbira sadzatinso, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto,’
15 Mas: Vive o Senhor, que fez subir os filhos d'Israel da terra do norte, e de todas as terras para onde os tinha lançado; porque fal-os-hei voltar á sua terra, a qual dei a seus paes.
koma adzanena kuti, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa Aisraeli ku dziko lakumpoto, ndi ku mayiko onse kumene anawabalalitsirako.’ Pakuti ndidzawabwezera ku dziko limene ndinalipereka kwa makolo awo.”
16 Eis que mandarei muitos pescadores, diz o Senhor, os quaes os pescarão, e depois enviarei muitos caçadores, os quaes os caçarão de sobre todo o monte, e de sobre todo o outeiro, e até das fendas das rochas.
Yehova akuti, “Koma tsopano ndidzayitana adani okhala ngati asodzi ambiri, ndipo adzawagwira ngati nsomba. Izi zitatha adani enanso okhala ngati alenje ambiri, adzawasaka pa phiri lililonse, pa chitunda chilichonse ndiponso mʼmapanga onse a mʼmatanthwe.
17 Porque os meus olhos estão sobre todos os seus caminhos; não se escondem perante a minha face, nem a sua maldade se encobre de diante dos meus olhos.
Maso anga akuona makhalidwe awo onse; sanabisike pamaso panga. Palibe tchimo limene sindikulidziwa.
18 E primeiramente pagarei em dobro a sua maldade e o seu peccado, porque profanaram a minha terra com os cadaveres das suas coisas detestaveis, e das suas abominações encheram a minha herança.
Ndidzawalanga mowirikiza chifukwa cha kuyipa kwawo ndi tchimo lawo. Ndidzatero chifukwa ayipitsa dziko langa ndi mafano awo amene ali ngati mitembo, ndiponso adzaza cholowa changa ndi mafano awo onyansa.”
19 Ó Senhor, fortaleza minha, e força minha, e refugio meu no dia da angustia: a ti virão as nações desde os fins da terra, e dirão: Nossos paes herdaram só mentiras, e vaidade, em que não havia proveito.
Inu Yehova, ndinu mphamvu yanga ndi linga langa, pothawirapo panga nthawi ya masautso, anthu a mitundu yonse adzabwera kwa Inu kuchokera ku mathero onse a dziko lapansi ndipo adzanena kuti, “Makolo anthu anali ndi milungu yonama, anali ndi mafano achabechabe amene sanawathandize.
20 Porventura fará um homem deuses para si, quando elles não são deuses?
Kodi anthu nʼkudzipangira milungu? Atati atero ndiye kuti imeneyo ikhala milungu yachabechabe.”
21 Portanto, eis que os farei conhecer; d'esta vez os farei conhecer a minha mão e o meu poder; e saberão que o meu nome é o Senhor.
“Choncho Ine ndidzawaphunzitsa, kokha kano kuti adziwe za mphamvu yanga ndi za nyonga zanga. Pamenepo adzadziwa kuti dzina langa ndi Yehova.

< Jeremias 16 >