< Oséias 6 >
1 Vinde, e tornemos ao Senhor, porque elle despedaçou, e nos sarará, feriu, e nos atará a ferida.
“Bwerani, tiyeni tibwerere kwa Yehova. Iye watikhadzula, koma adzatichiritsa. Iye wativulaza, koma adzamanga mabala athu.
2 Depois de dois dias nos dará a vida: ao terceiro dia nos resuscitará, e viveremos diante d'elle.
Pakapita masiku awiri adzatitsitsimutsa; pa tsiku lachitatu Iye adzatiukitsa kuti tikhale ndi moyo pamaso pake.
3 Então conheceremos, e proseguiremos em conhecer, ao Senhor: como a alva, está apparelhada a sua saida: e elle a nós virá como a chuva, como chuva serodia que rega a terra.
Tiyeni timudziwe Yehova, tiyeni tilimbike kumudziwa Iye. Adzabwera kwa ife mosakayikira konse ngati kutuluka kwa dzuwa; adzabwera kwa ife ngati mvula ya mʼchilimwe, ngati mvula ya nthawi yamphukira imene imakhathamiritsa nthaka.”
4 Que te farei, ó Ephraim? que te, farei, ó Judah? visto que a vossa beneficencia é como a nuvem da manhã, e como o orvalho da madrugada, que passa.
Iwe Efereimu, kodi ndichite nawe chiyani? Kodi ndichite nawe chiyani, iwe Yuda? Chikondi chanu chili ngati nkhungu yammawa, ngati mame a mmamawa amene amakamuka msanga.
5 Por isso os cortei pelos prophetas: pela palavras da minha bocca os matei; e os teus juizos sairão como a luz.
Choncho ndakuwazani ngati nkhuni kudzera mwa aneneri anga, ndakuphani ndi mawu a pakamwa panga; chigamulo changa chinangʼanima ngati mphenzi pa inu.
6 Porque o que eu quero é a misericordia, e não o sacrificio; e o conhecimento de Deus, mais do que os holocaustos.
Pakuti Ine ndimafuna chifundo osati nsembe, ndi kudziwa Mulungu kulekana ndi nsembe zopsereza.
7 Porém elles traspassaram o concerto, como Adão; ali se portaram aleivosamente contra mim.
Monga Adamu, anthuwa aphwanya pangano langa, iwo sanakhulupirike kwa Ine.
8 Gilead é uma cidade dos que obram iniquidade, calcada de sangue.
Giliyadi ndi mzinda wa anthu ochita zoyipa, okhala ndi zizindikiro za kuphana.
9 Como as tropas dos salteadores a alguns esperam, assim é a companhia dos sacerdotes; matam no caminho para Sichem, porque fazem abominações.
Monga momwe mbala zimadikirira anthu, magulu a ansembe amachitanso motero; iwo amapha anthu pa njira yopita ku Sekemu, kupalamula milandu yochititsa manyazi.
10 Vejo uma coisa horrenda na casa de Israel: ali está a fornicação d'Ephraim; Israel é contaminado.
Ndaona chinthu choopsa kwambiri mʼnyumba ya Israeli. Kumeneko Efereimu akuchita zachiwerewere, ndipo Israeli wadzidetsa.
11 Tambem para ti, ó Judah, foi assignada uma sega; quando eu tornar o captiveiro do meu povo.
“Kunenanso za iwe Yuda, udzakolola chilango. “Pamene ndiwabwezere anthu anga zinthu zabwino.”