< Oséias 14 >
1 Converte-te, ó Israel, ao Senhor teu Deus; porque pelos teus peccados tens caido.
Iwe Israeli bwerera kwa Yehova Mulungu wako. Machimo anu ndi amene akugwetsani!
2 Tomae comvosco palavras, e convertei-vos ao Senhor: dizei-lhe: Tira toda a iniquidade, e recebe o bem; e pagaremos os bezerros dos nossos labios.
Bweretsani zopempha zanu ndipo bwererani kwa Yehova. Munene kwa Iye kuti, “Tikhululukireni machimo athu onse ndi kutilandira mokoma mtima, kuti tithe kukuyamikani ndi mawu a pakamwa pathu.
3 Não nos salvará a Assyria, não iremos montados em cavallos, e á obra das nossas mãos não diremos mais: Tu és o nosso Deus; porque por ti o orphão alcançará misericordia.
Asiriya sangatipulumutse; ife sitidzakwera pa akavalo ankhondo, sitidzanenanso kuti, ‘Milungu yathu’ kwa zimene manja athu omwe anazipanga, pakuti ndinu amene mumachitira chifundo ana amasiye.”
4 Eu sararei a sua perversão, eu voluntariamente os amarei; porque a minha ira se apartou d'elles.
Ine ndidzachiza kusakhulupirika kwawo ndipo ndidzawakonda mwaufulu pakuti ndaleka kuwakwiyira.
5 Eu serei a Israel como orvalho, elle florescerá como o lirio, e espalhará as suas raizes como o Libano.
Ndidzakhala ngati mame kwa Israeli Ndipo iye adzachita maluwa ngati kakombo. Adzazika mizu yake pansi ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
6 Estender-se-hão as suas vergonteas, e a sua gloria será como a da oliveira, e cheirará como o Libano.
mphukira zake zidzakula. Kukongola kwake kudzakhala ngati mtengo wa olivi, kununkhira kwake ngati mkungudza wa ku Lebanoni.
7 Voltarão os que se assentarem debaixo da sua sombra; serão vivificados como o trigo, e florescerão como a vide; a sua memoria será como o vinho do Libano.
Anthu adzakhalanso mu mthunzi wake. Iye adzakula bwino ngati tirigu. Adzachita maluwa ngati mphesa ndipo kutchuka kwake kudzakhala ngati vinyo wochokera ku Lebanoni.
8 Ephraim então dirá: Que mais tenho eu com os idolos? eu o tenho ouvido, e olharei para elle: ser-lhe-hei como a faia verde: de mim é achado o teu fructo.
Efereimu adzati, “Ndidzachita nawonso chiyani mafano? Ine ndidzamuyankha ndi kumusamalira. Ine ndili ngati mtengo wa payini wobiriwira; zipatso zako zimachokera kwa Ine.”
9 Quem é sabio, para que entenda estas coisas; quem é prudente, para que as saiba? porque os caminhos do Senhor são rectos, e os justos andarão n'elles, mas os transgressores cairão n'elles.
Ndani ali ndi nzeru? Adzazindikire zinthu izi. Ndani amene amamvetsa zinthu? Adzamvetse izi. Njira za Yehova ndi zolungama; anthu olungama amayenda mʼmenemo, koma anthu owukira amapunthwamo.