< Oséias 12 >
1 Ephraim se apascenta de vento, e segue o vento leste: todo o dia multiplica a mentira e a destruição; e fazem alliança com a Assyria, e o azeite se leva ao Egypto.
Efereimu amadya mpweya; tsiku lonse amasaka mphepo ya kummawa ndipo amachulukitsa mabodza ndi chiwawa. Amachita mgwirizano ndi Asiriya ndipo amatumiza mphatso za mafuta a olivi ku Igupto.
2 O Senhor tambem com Judah tem contenda, e fará visitação sobre Jacob segundo os seus caminhos; segundo as suas obras lhe recompensará.
Yehova akuyimba mlandu Yuda; Iye adzalanga Yakobo molingana ndi makhalidwe ake, adzamulanga molingana ndi ntchito zake.
3 No ventre pegou do calcanhar de seu irmão, e pela sua força como principe se houve com Deus.
Akali mʼmimba mwa amayi ake, Yakobo anagwira chidendene cha mʼbale wake; iye atakula analimbana ndi Mulungu.
4 Como principe se houve com o anjo, e prevaleceu; chorou, e lhe supplicou: em Beth-el o achou, e ali fallou comnosco,
Yakobo analimbana ndi mngelo ndipo anapambana; analira napempha kuti amukomere mtima. Mulungu anakumana naye ku Beteli ndipo anayankhula naye kumeneko,
5 A saber, o Senhor, o Deus dos Exercitos: o Senhor é o seu memorial.
Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Yehova ndiye dzina lake lotchuka!
6 Tu, pois, converte-te a teu Deus: guarda a beneficencia e o juizo, e em teu Deus espera sempre.
Koma inu muyenera kubwerera kwa Mulungu wanu; pitirizani chikondi ndi chiweruzo cholungama, ndipo muzidikira Mulungu wanu nthawi zonse.
7 Na mão do mercador está uma balança enganosa; ama a oppressão.
Munthu wamalonda amagwiritsa ntchito masikelo achinyengo; iyeyo amakonda kubera anthu.
8 Ainda diz Ephraim: Comtudo eu estou enriquecido, e tenho adquirido para mim grandes bens: em todo o meu trabalho não acharão em mim iniquidade alguma que seja peccado.
Efereimu amadzitama ponena kuti, “Ndine wolemera kwambiri; ndili ndi chuma chambiri. Palibe amene angandiloze chala chifukwa cha kulemera kwanga.”
9 Mas eu sou o Senhor teu Deus desde a terra do Egypto: eu ainda te farei habitar em tendas, como nos dias do ajuntamento.
“Ine ndine Yehova Mulungu wako amene ndinakutulutsa mu Igupto. Ndidzakukhazikaninso mʼmatenti, monga munkachitira masiku aja pa nthawi ya zikondwerero zanu.
10 E fallarei aos prophetas, e multiplicarei a visão; e pelo ministerio dos prophetas proporei similes.
Ndinayankhula ndi aneneri, ndinawaonetsa masomphenya ambiri, ndipo ndinawawuza mafanizo kudzera mwa iwo.”
11 Porventura não é Gilead iniquidade? pura vaidade são: em Gilgal sacrificam bois: os seus altares como montões de pedras são nos regos dos campos.
Kodi Giliyadi ndi woyipa? Anthu ake ndi achabechabe! Kodi amapereka nsembe za ngʼombe zazimuna ku Giligala? Maguwa awo ansembe adzakhala ngati milu ya miyala mʼmunda molimidwa.
12 Jacob fugiu para o campo da Syria, e Israel serviu por sua mulher, e por sua mulher guardou o gado.
Yakobo anathawira ku dziko la Aramu, Israeli anagwira ntchito kuti apeze mkazi, ndipo anaweta nkhosa kuti akwatire mkaziyo.
13 Mas o Senhor por um propheta fez subir a Israel do Egypto, e por um propheta foi elle guardado.
Yehova anagwiritsa ntchito mneneri kuti atulutse Israeli mu Igupto; kudzera mwa mneneriyo Iye anawasamalira.
14 Ephraim porém mui amargosamente o irou: portanto deixará ficar sobre elle o seu sangue, e o seu Senhor lhe recompensará o seu opprobrio.
Koma Efereimu wamukwiyitsa kwambiri. Nʼchifukwa chake Yehova adzawalanga ndi imfa. Adzawalanga chifukwa anamuchititsa manyazi kwambiri.