< Zachariasza 13 >
1 W tym dniu zostanie otwarte źródło dla domu Dawida i mieszkańców Jerozolimy dla [obmycia] grzechu i nieczystości.
“Pa tsiku limenelo nyumba ya Davide adzayitsekulira kasupe wa madzi pamodzi ndi okhala mu Yerusalemu, kuti awachotsere tchimo lawo ndi chodetsa chawo.
2 I stanie się w tym dniu, mówi PAN zastępów, że wykorzenię imiona bożków z ziemi, tak że nie będą więcej wspominane. Usunę z ziemi także proroków i ducha nieczystego.
“Pa tsiku limenelo, ndidzafafaniziratu mayina a mafano mʼdziko, ndipo sadzawakumbukiranso,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Ndidzachotsa mʼdziko aneneri pamodzi ndi mzimu wonyansa.
3 A gdyby ktoś jeszcze prorokował, jego ojciec i matka, którzy go zrodzili, powiedzą mu: Nie będziesz żył, gdyż mówiłeś kłamstwo w imię PANA. I jego ojciec, i matka, którzy go zrodzili, przebiją go [za to], że prorokował.
Ndipo ngati wina aliyense adzafuna kunenera, abambo ndi amayi ake amene anamubereka, adzamuwuza kuti, ‘Uyenera kufa, chifukwa wayankhula bodza mʼdzina la Yehova.’ Pamene anenera, makolo ake omwe adzamubaya.
4 I stanie się w tym dniu, że każdy z tych proroków zawstydzi się z powodu swojego widzenia, gdy prorokował, i nie oblecze się w kosmatą szatę, aby kłamać.
“Pa tsiku limenelo mneneri aliyense adzachita manyazi chifukwa cha masomphenya ake. Sadzavala chovala chake chaubweya ndi cholinga chonamiza anthu.
5 Ale każdy powie: Nie jestem prorokiem, ale rolnikiem, bo tego mnie uczono od dzieciństwa.
Iye adzati, ‘Sindine mneneri. Ndine mlimi; ndakhala ndi kulima munda kuyambira ubwana wanga.’
6 A jeśli ktoś go zapyta: Co to za rany na twoich rękach? Wtedy powie: Zostałem zraniony w domu moich przyjaciół.
Ngati wina adzamufunsa, ‘Zilonda zili mʼthupi lakoli ndi chiyani?’ Iye adzayankha kuti, ‘Zilondazi ndinazilandira mʼnyumba ya abwenzi anga.’
7 Mieczu, ocknij się przeciwko mojemu pasterzowi i przeciwko mężczyźnie, który jest moim towarzyszem, mówi PAN zastępów. Uderz pasterza, a owce zostaną rozproszone. Ja zaś zwrócę swoją rękę ku malutkim.
“Dzambatuka iwe lupanga, ukanthe mʼbusa wanga, ukanthe munthu amene ali pafupi ndi Ine!” akutero Yehova Wamphamvuzonse. Kantha mʼbusa ndipo nkhosa zidzabalalika, ndipo ndidzatambalitsa dzanja langa kuwononga zazingʼono.
8 I stanie się na całej ziemi, mówi PAN, [że] dwie części w niej zostaną wycięte i zginą, a trzecia [część] pozostanie w niej.
Mʼdziko monse, akutero Yehova Wamphamvuzonse, “zigawo ziwiri mwa zigawo zitatu za anthu zidzakanthidwa ndi kuwonongeka; koma chigawo chimodzi chidzatsala mʼdzikomo.
9 I przeprowadzę tę trzecią część przez ogień i oczyszczę ich jak się czyści srebro, wypróbuję ich, jak się próbuje złoto. Będą wzywali mego imienia, a ja ich wysłucham. Powiem: Ty jesteś moim ludem, a on powie: PAN jest moim Bogiem.
Chigawo chachitatuchi ndidzachiyika pa moto; ndidzawayeretsa monga momwe amayeretsera siliva ndi kuwayesa monga momwe amayesera golide. Adzayitana pa dzina langa ndipo Ine ndidzawayankha; Ine ndidzanena kuti, ‘Awa ndi anthu anga,’ ndipo iwo adzanena kuti, ‘Yehova ndiye Mulungu wathu.’”