< Pieśń nad Pieśniami 5 >

1 Wszedłem do mojego ogrodu, moja siostro, [moja] oblubienico. Zbierałem moją mirrę z moimi wonnościami; zjadłem mój plaster z moim miodem, piję moje wino z moim mlekiem. Jedzcie, przyjaciele, pijcie, a pijcie obficie, moi mili.
Ndalowa mʼmunda mwanga, iwe mlongo wanga, iwe mkwatibwi wanga; ndasonkhanitsa mure wanga ndi zokometsera zakudya zanga. Ndadya uchi wanga pamodzi ndi zisa zake zomwe; ndamwa vinyo wanga ndi mkaka wanga. Abwenzi Idyani abwenzi anga, imwani; Inu okondana, imwani kwambiri.
2 Ja śpię, ale moje serce czuwa. [Oto] głos mego umiłowanego, który puka i [mówi]: Otwórz mi, moja siostro, moja umiłowana, moja gołębico, moja nieskalana. Moja głowa bowiem jest pełna rosy, moje kędziory – kropli nocy.
Ndinagona tulo koma mtima wanga unali maso. Tamverani, bwenzi langa akugogoda: “Nditsekulire, mlongo wanga, bwenzi langa, nkhunda yanga, wangwiro wanga. Mutu wanga wanyowa ndi mame, tsitsi langa lanyowa chifukwa cha nkhungu ya usiku.”
3 Zdjęłam już swoją suknię, jakże mam ją wkładać? Umyłam swoje nogi, jakże mam je pobrudzić?
Ndavula kale zovala zanga, kodi ndizivalenso? Ndasamba kale mapazi anga kodi ndiwadetsenso?
4 Mój umiłowany wsunął swoją rękę przez otwór, a moje wnętrze poruszyło się we mnie.
Bwenzi langa anapisa dzanja lake pa chibowo cha pa chitseko; mtima wanga unagunda chifukwa cha iye.
5 Wstałam, aby otworzyć mojemu umiłowanemu, a oto z moich rąk kapała mirra, z moich palców mirra spływała na uchwyt zasuwy.
Ndinanyamuka kukamutsekulira wachikondi wangayo, ndipo manja anga anali noninoni ndi mure, zala zanga zinali mure chuchuchu, pa zogwirira za chotsekera.
6 Otworzyłam mojemu umiłowanemu, lecz mój umiłowany [już] odszedł i zniknął. Moja dusza zasłabła na jego głos. Szukałam go, ale nie znalazłam, wołałam go, ale mi nie odpowiedział.
Ndinamutsekulira wachikondi wanga, koma nʼkuti wachikondi wangayo atachoka; iye anali atapita. Mtima wanga unafumuka chifukwa cha kuchoka kwake. Ndinamuyangʼanayangʼana koma sindinamupeze. Ndinamuyitana koma sanandiyankhe.
7 Znaleźli mnie strażnicy, którzy obchodzili miasto; pobili mnie i zranili, strażnicy murów zabrali mi zasłonę.
Alonda anandipeza pamene ankayendera mzindawo. Anandimenya ndipo anandipweteka; iwo anandilanda mwinjiro wanga, alonda a pa khoma aja!
8 Zaklinam was, córki Jerozolimy: Jeśli znajdziecie mojego umiłowanego, to powiedzcie mu, że jestem chora z miłości.
Inu akazi a ku Yerusalemu ndithu ndikukupemphani, mukapeza wokondedwa wangayo, kodi mudzamuwuza chiyani? Muwuzeni kuti ine ndadwala nacho chikondi.
9 Czym przewyższa twój umiłowany [innych] umiłowanych, o najpiękniejsza wśród kobiet? Czym przewyższa twój umiłowany [innych] umiłowanych, że tak nas zaklinasz?
Iwe wokongola kuposa akazi onsewa, kodi wokondedwa wakoyo ndi wopambana wina aliyense bwanji? Kodi wokondedwa wakoyo ndi wopambana ena onse chotani kuti uzichita kutipempha motere?
10 Mój umiłowany jest biały i rumiany, i najznakomitszy spośród dziesięciu tysięcy.
Wokondedwa wangayo ndi wowala kwambiri ndi wathanzi pakati pa anthu 1,000.
11 Jego głowa jest [jak] najczystsze złoto; jego kędziory faliste, czarne jak kruk.
Mutu wake ndi golide woyengeka bwino; tsitsi lake ndi lopotanapotana, ndiponso lakuda bwino ngati khwangwala.
12 Jego oczy są jak gołębice nad strumieniami wody, [jakby] umyte w mleku, osadzone w swej oprawie.
Maso ake ali ngati nkhunda mʼmbali mwa mitsinje ya madzi, ngati nkhunda zitasamba mu mkaka, zitayima ngati miyala yamtengowapatali.
13 Jego policzki jak grządka wonności, [jak] pachnące kwiatki; jego wargi jak lilie ociekające wyborną mirrą.
Masaya ake ali ngati timinda ta mbewu zokometsera zakudya zopatsa fungo lokoma. Milomo yake ili ngati maluwa okongola amene akuchucha mure.
14 Jego ręce [jak] złote pierścienie wysadzone berylem; jego tors [jak] jasna kość słoniowa pokryta szafirem.
Manja ake ali ngati ndodo zagolide zokongoletsedwa ndi miyala yamtengowapatali. Thupi lake ndi losalala ngati mnyanga wanjovu woyikamo miyala ya safiro.
15 Jego nogi [jak] słupy z marmuru, postawione na szczerozłotych podstawkach; jego oblicze [jak] Liban, wyborne jak cedry.
Miyendo yake ili ngati mizati yamwala, yokhazikika pa maziko a golide. Maonekedwe ake ali ngati Lebanoni, abwino kwambiri ngati mkungudza.
16 Jego usta przesłodkie i jest on cały przepiękny. Taki jest mój umiłowany i taki jest mój przyjaciel, córki Jerozolimy.
Milomo yake ndi yosangalatsa kwambiri; munthuyo ndi wokongola kwambiri! Uyu ndiye wachikondi wanga ndi bwenzi langa, inu akazi a ku Yerusalemu.

< Pieśń nad Pieśniami 5 >