< Psalmów 99 >
1 PAN króluje, niech drżą narody; siedzi między cherubinami, niech zachwieje się ziemia.
Yehova akulamulira, mitundu ya anthu injenjemere; Iye wakhala pa mpando wake waufumu, pakati pa akerubi, dziko lapansi ligwedezeke.
2 Wielki jest PAN na Syjonie i wywyższony nad wszystkie narody.
Mʼziyoni wamkulu ndi Yehova; Iye ndi wokwezeka pamwamba pa mitundu yonse ya anthu.
3 Niech wysławiają twoje wielkie i straszne imię, bo jest święte.
Anthu atamande dzina lanu lalikulu ndi loopsa kwambiri, Iye ndi woyera.
4 Moc króla miłuje sąd, ty ustanowiłeś słuszność, ty wykonujesz sąd i sprawiedliwość w Jakubie.
Mfumu yamphamvu, iyo imakonda chilungamo Inu mwakhazikitsa khalidwe losakondera; mwachita zolungama ndi zoyenera mwa Yakobo.
5 Wywyższajcie PANA, naszego Boga, i oddajcie pokłon u podnóżka jego stóp, [bo] on jest święty.
Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mulambireni pa mapazi ake; Iye ndi woyera.
6 Mojżesz i Aaron wśród jego kapłanów, a Samuel wśród tych, którzy wzywają jego imienia; wołali do PANA, a on ich wysłuchał.
Mose ndi Aaroni anali ena mwa ansembe ake, Samueli anali pamodzi ndi iwo amene anayitana pa dzina lake; iwo anayitana Yehova ndipo Iyeyo anawayankha.
7 W słupie obłoku mówił do nich, [a] oni strzegli jego świadectw i praw, [które] im dał.
Iye anayankhula nawo kuchokera mʼchipilala cha mtambo; iwo anasunga malamulo ake ndi zophunzitsa zomwe anawapatsa.
8 PANIE, nasz Boże, ty ich wysłuchiwałeś, byłeś dla nich Bogiem, który przebacza, choć karałeś ich za ich występki.
Inu Yehova Mulungu wathu, munawayankha iwo; Inu kwa Israeli munali Mulungu wokhululuka, ngakhale munawalanga pa zochita zawo zoyipa.
9 Wywyższajcie PANA, naszego Boga, i oddajcie pokłon na jego świętej górze, bo PAN, nasz Bóg, [jest] święty.
Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mumulambire pa phiri lake loyera, pakuti Yehova Mulungu wathu ndi woyera.