< Psalmów 83 >

1 Pieśń i psalm Asafa. Boże, nie milcz; nie bądź głuchy i bezczynny, Boże!
Nyimbo. Salimo la Asafu. Inu Mulungu musakhale chete; musangoti phee, Mulungu musangoti duu.
2 Bo oto burzą się twoi wrogowie, a ci, którzy cię nienawidzą, podnoszą głowę.
Onani adani anu akuchita chiwawa, amene amadana nanu autsa mitu yawo.
3 Przeciwko twemu ludowi knują spisek i naradzali się przeciw tym, których ochraniasz;
Mochenjera iwo akukambirana za chiwembu kutsutsana ndi anthu anu; Iwo akukonzekera kutsutsana ndi omwe mumawakonda.
4 Mówiąc: Chodźcie, wytępmy ich, niech nie będą narodem, żeby więcej nie wspominano imienia Izraela.
Iwo akunena kuti, “Bwerani” akutero, “Tiyeni tiwononge mtundu wonsewu kuti dzina la Israeli lisakumbukikenso.”
5 Zmówili się bowiem jednomyślnie, przeciwko tobie zawarli przymierze:
Ndi mtima umodzi akukonzekera chiwembu; Iwo achita mgwirizano kutsutsana nanu:
6 Namioty Edomitów i Izmaelitów, Moab i Hagaryci;
Matenti a Edomu ndi Aismaeli, Mowabu ndi Ahagiri,
7 Gebal, Ammon i Amalek; Filistyni z mieszkańcami Tyru.
Agebala, Aamoni ndi Aamaleki, Afilisti, pamodzi ndi anthu a ku Turo.
8 Także Assur przyłączył się do nich, wsparł [swym] ramieniem synów Lota. (Sela)
Ngakhalenso Aasiriya aphatikizana nawo kupereka mphamvu kwa ana a Loti. (Sela)
9 Uczyń im [tak], jak Midianitom, jak Syserze, jak Jabinowi nad potokiem Kiszon;
Muwachitire zomwe munachitira Amidiyani, monga munachitira Sisera ndi Yabini ku mtsinje wa Kisoni.
10 Którzy zostali wytępieni w Endor, stali się jak gnój dla ziemi.
Amene anawonongedwa ku Endori ndi kukhala ngati zinyalala.
11 Z ich dostojnikami postąp jak z Orebem i Zeebem, jak z Zebachem i Salmunną, ze wszystkimi ich książętami;
Anthu awo otchuka muwachite zomwe munachita Orebu ndi Zeebu ana a mafumu muwachite zomwe munachita Zeba ndi Zalimuna,
12 [Którzy] mówili: Weźmy w posiadanie przybytki Boże.
amene anati, “Tiyeni tilande dziko la msipu la Mulungu.”
13 Mój Boże, uczyń ich jak koło i jak źdźbło na wietrze.
Muwasandutse fumbi lowuluka, Inu Mulungu wanga, ngati mankhusu owuluka ndi mphepo.
14 Jak ogień, który pali las, i jak płomień, [który] wypala góry;
Monga moto umatentha nkhalango, kapena malawi a moto kuyatsa phiri,
15 Tak ty ich ścigaj swoją nawałnicą i swoją burzą zatrwóż ich.
kotero muwathamangitse ndi mphepo yamkuntho, ndi kuwachititsa mantha ndi namondwe.
16 Okryj ich twarze hańbą, aby szukali twego imienia, PANIE!
Muphimbe nkhope zawo ndi manyazi kuti adzafunefune dzina lanu Yehova.
17 Niech się zawstydzą i zatrwożą na wieki, niech się okryją hańbą i zginą.
Achite manyazi ndi mantha nthawi zonse; awonongeke mwa manyazi.
18 Niech poznają, że jedynie ty, którego imię jest PAN, ty jesteś Najwyższy ponad całą ziemią.
Adziwe kuti Inu amene dzina lanu ndi Yehova, ndinu nokha Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi.

< Psalmów 83 >