< Psalmów 64 >
1 Przewodnikowi chóru. Psalm Dawida. Wysłuchaj, o Boże, mego głosu, gdy się modlę; zachowaj moje życie od strachu przed wrogiem.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Ndimvereni Mulungu pomwe ndikunena madandawulo anga; tetezani moyo wanga ku chiopsezo cha mdani.
2 Ukryj mnie przed tajemną radą złoczyńców, przed zgrają czyniących nieprawość;
Ndibiseni ku chiwembu cha anthu oyipa, ku gulu laphokoso la anthu ochita zoyipa.
3 Którzy naostrzyli swój język jak miecz, nałożyli swoje strzały, słowa jadowite;
Iwo amanola malilime awo ngati malupanga, amaponya mawu awo olasa ngati mivi.
4 Aby strzelać z ukrycia w niewinnego; strzelają znienacka i nikogo się nie boją.
Iwo amaponya mivi yawo ali pa malo wobisala kwa munthu wosalakwa; amamulasa modzidzimutsa ndi mopanda mantha.
5 Utwierdzają się w złym zamiarze, zmawiają się, jak ukryć pułapki, i mówią: Któż je zobaczy?
Iwo amalimbikitsana wina ndi mnzake pa chikonzero chawo choyipa, amayankhula zobisa misampha yawo; ndipo amati, “Adzayiona ndani?”
6 Szukają nieprawości, starannie jej poszukują; ich wnętrze i serce są głębokie.
Iwo amakonzekera zosalungama ndipo amati, “Takonza ndondomeko yabwino kwambiri!” Ndithu maganizo ndi mtima wa munthu ndi zachinyengo.
7 Ale Bóg wypuści na nich strzałę, nagle odniosą rany;
Koma Mulungu adzawalasa ndi mivi; mwadzidzidzi adzakanthidwa.
8 Własny język doprowadzi ich do upadku; wszyscy, którzy ich zobaczą, uciekną.
Iye adzatembenuza milomo yawoyo kuwatsutsa ndi kuwasandutsa bwinja; onse amene adzawaona adzagwedeza mitu yawo mowanyoza.
9 I zlękną się wszyscy ludzie, będą opowiadali o dziele Boga i zrozumieją jego czyny.
Anthu onse adzachita mantha; adzalengeza ntchito za Mulungu ndi kulingalira mozama zomwe Iye wazichita.
10 A sprawiedliwy będzie się weselić w PANU i będzie mu ufał; i będą się chlubili wszyscy prawego serca.
Lolani wolungama akondwere mwa Yehova ndi kubisala mwa Iye, owongoka mtima onse atamande Iye!