< Psalmów 57 >

1 Przewodnikowi chóru. Al taszchet. Miktam Dawida, kiedy uciekał przed Saulem do jaskini. Zmiłuj się nade mną, Boże, zmiłuj się nade mną, bo moja dusza ufa tobie; w cieniu twoich skrzydeł będę się chronił, aż przeminie nieszczęście.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide, pamene anathawa Sauli kupita ku phanga. Mundichitire chifundo, Inu Mulungu mundichitire chifundo, pakuti mwa Inu moyo wanga umathawiramo. Ndidzathawira mu mthunzi wa mapiko anu mpaka chiwonongeko chitapita.
2 Będę wołał do Boga Najwyższego, do Boga, który doprowadzi moją sprawę do końca.
Ine ndikufuwulira kwa Mulungu Wammwambamwamba, kwa Mulungu amene amakwaniritsa cholinga chake pa ine.
3 On ześle [pomoc] z nieba i wybawi mnie [od] urągania tego, który chce mnie pochłonąć. (Sela) Ześle mi Bóg swoje miłosierdzie i prawdę.
Mulungu amanditumizira kuchokera kumwamba ndi kundipulumutsa, kudzudzula iwo amene akundithamangitsa kwambiri. Mulungu amatumiza chikondi chake ndi kukhulupirika kwake.
4 Moja dusza przebywa wśród lwów; leżę [wśród] płonących, [wśród] synów ludzkich, których zęby [są] jak włócznie i strzały, a język jak miecz ostry.
Ine ndili pakati pa mikango, ndagona pakati pa zirombo zolusa; anthu amene mano awo ndi milomo yawo ndi mivi, malilime awo ndi malupanga akuthwa.
5 Bądź wywyższony, Boże, ponad niebiosa, [a] twoja chwała ponad całą ziemię.
Mukwezekedwe Inu Mulungu, kuposa mayiko onse akumwamba; mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.
6 Zastawili sidła na moje kroki, zgnębili moją duszę, wykopali przede mną dół, ale sami do niego wpadli. (Sela)
Iwo anatchera mapazi anga ukonde ndipo ndinawerama pansi mosautsidwa. Anakumba dzenje mʼnjira yanga koma agweramo okha mʼmenemo.
7 Gotowe [jest] moje serce, Boże, gotowe [jest] moje serce; będę śpiewał i oddawał chwałę.
Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu mtima wanga ndi wokhazikika. Ndidzayimba nyimbo, nyimbo yake yamatamando.
8 Obudź się, moja chwało, obudź się, cytro i harfo; ja się zbudzę o świcie.
Dzuka moyo wanga! Dzukani zeze ndi pangwe! Ndidzadzuka mʼbandakucha.
9 Będę cię wysławiał wśród ludu, Panie, będę ci śpiewał wśród narodów.
Ndidzakutamandani Ambuye, pakati pa mitundu ya anthu, ndidzayimba za Inu pakati pa mayiko.
10 Bo wielkie jest twoje miłosierdzie, aż do niebios, i aż pod obłoki twoja prawda.
Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kufikira ku mayiko akumwamba; kukhulupirika kwanu kwafika ku mitambo.
11 Bądź wywyższony ponad niebiosa, Boże, a ponad całą ziemię twoja chwała.
Mukwezekedwe Inu Mulungu kuposa mayiko akumwamba, mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.

< Psalmów 57 >