< Psalmów 55 >

1 Przewodnikowi chóru, na Neginot. Pieśń pouczająca Dawida. Boże, nakłoń ucha ku mojej modlitwie i nie ukrywaj się przed moją prośbą.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya Davide. Pa zoyimbira za zingwe. Mvetserani pemphero langa, Inu Mulungu, musakufulatire kupempha kwanga,
2 Posłuchaj uważnie i wysłuchaj mnie; uskarżam się w swej modlitwie i jęczę;
mverani ndipo mundiyankhe. Maganizo anga akundisautsa ndipo ndathedwa nzeru
3 Z powodu głosu wroga, z powodu ucisku niegodziwego; zwalają na mnie nieprawość i w gniewie sprzeciwiają mi się.
chifukwa cha mawu a adani anga, chifukwa cha kupondereza kwa anthu oyipa; pakuti andidzetsera masautso ndipo akundizunza mu mkwiyo wawo.
4 Moje serce boleje we mnie i dopadł mnie strach przed śmiercią.
Mtima wanga ukupweteka mʼkati mwanga; mantha a imfa andigwera.
5 Przyszły na mnie bojaźń i drżenie i przejęła mnie trwoga.
Mantha ndi kunjenjemera zandizinga; mantha aakulu andithetsa nzeru.
6 I powiedziałem: O, gdybym miał skrzydła jak gołębica, uleciałbym i odpoczął.
Ndinati, “Ndithu, ndikanakhala ndi mapiko ankhunda! Ndikanawulukira kutali ndi kukapuma.
7 Oto bym uleciał daleko i zamieszkał na pustyni. (Sela)
Ndikanathawira kutali ndi kukakhala mʼchipululu.
8 Pospieszyłbym, aby ujść [przed] wichrem i nawałnicą.
Ndikanathamangira kumalo anga a chitetezo; kutali ndi mphepo yaukali ndi yamkuntho.”
9 Zniszcz, Panie, rozdziel ich język, bo widzę przemoc i niezgodę w mieście.
Sokonezani maganizo a oyipa, Inu Ambuye, tsutsani mawu awo; pakuti ine ndikuona chiwawa ndi mkangano mu mzinda.
10 Dniem i nocą krążą wokoło po jego murach, a wewnątrz niego zło i ucisk.
Usana ndi usiku iwo akuzungulirazungulira pa makoma ake; nkhwidzi ndi kuzunza kuli mʼkati mwake.
11 Wewnątrz niego [jest] niegodziwość, a z jego ulic nie znika oszustwo i podstęp.
Mphamvu zowononga zili pa ntchito mu mzinda; kuopseza ndi mabodza sizichoka mʼmisewu yake.
12 Bo [to] nie wróg mnie lżył, co mógłbym znieść; nie powstał przeciwko mnie ten, który mnie nienawidził – [wtedy] ukryłbym się przed nim;
Akanakhala mdani akundinyoza, ine ndikanapirira; akanakhala mdani akudzikweza yekha kutsutsana nane, ndikanakabisala.
13 Ale ty, człowiek równy mi, mój wódz i przyjaciel.
Koma iweyo mnzanga, mnzanga woyenda naye, bwenzi langa la pondaapanʼpondepo, ndi amene ukuchita zimenezi.
14 Mile naradzaliśmy się ze sobą i razem chodziliśmy do domu Bożego.
Mnzanga amene nthawi ina tinkasangalala pa chiyanjano chokoma ku nyumba ya Mulungu.
15 Niech śmierć ich zaskoczy, niech żywcem zstąpią do piekła, bo w ich domach i wśród nich [mieszka] zło. (Sheol h7585)
Mulole imfa itenge adani anga mwadzidzidzi; alowe mʼmanda ali amoyo pakuti choyipa chili pakati pawo. (Sheol h7585)
16 Ja zaś do Boga zawołam i PAN mnie wybawi.
Koma ine ndinafuwulira kwa Mulungu, ndipo Yehova anandipulumutsa.
17 Wieczorem, rano i w południe będę się modlić i głośno wołać, a on wysłucha mego głosu.
Madzulo, mmawa ndi masana ndimalira mowawidwa mtima, ndipo Iye amamva mawu anga.
18 Odkupił moją duszę, abym miał spokój od walki, jaką ze mną toczyli, bo wielu ich było przy mnie.
Iye amandiwombola ine osavulazidwa pa nkhondo imene yafika kulimbana nane, ngakhale kuti ndi ambiri amene akunditsutsa.
19 Bóg wysłucha i będzie ich trapić ten, który trwa od wieków. (Sela) [Bo] nie poprawiają się i nie boją się Boga.
Mulungu amene ali pa mpando wake kwamuyaya, adzandimenyera nkhondo; adzawatsitsa adani anga, chifukwa safuna kusintha njira zawo zoyipa ndipo saopa Mulungu.
20 Podniósł rękę na tych, którzy utrzymywali z nim pokój; złamał swoje przymierze.
Mnzanga woyenda naye wathira nkhondo abwenzi ake; iye akuphwanya pangano ake.
21 Gładsze niż masło były [słowa] jego ust, lecz wrogość [miał] w sercu; miększe niż oliwa jego słowa, ale były jak obnażone miecze.
Mawu ake ndi osalala kuposa batala komabe nkhondo ili mu mtima mwake; mawu ake ndi osalala kwambiri kuposa mafuta, komatu mawuwo ndi malupanga osololoka.
22 Przerzuć swój ciężar na PANA, a on cię podtrzyma; nie dopuści nigdy, by miał się zachwiać sprawiedliwy.
Tulani nkhawa zanu kwa Yehova ndipo Iye adzakulimbitsani; Iye sadzalola kuti wolungama agwe.
23 Ale ty, Boże, wtrącisz ich w dół zatracenia; ludzie krwawi i podstępni nie dożyją połowy swoich dni; ja zaś zaufam tobie.
Koma Inu Mulungu mudzawatsitsa anthu oyipa kulowa mʼdzenje lachiwonongeko; anthu okhetsa magazi ndi anthu achinyengo sadzakhala moyo theka la masiku awo, koma ine ndimadalira Inu.

< Psalmów 55 >